< Zacharie 2 >

1 J'élevai encore mes yeux, et regardai; et voilà un homme qui avait à la main un cordeau à mesurer,
Kenaka ndinayangʼananso, ndipo ndinaona munthu atanyamula chingwe choyezera mʼmanja mwake.
2 Auquel je dis: Où vas-tu? Et il me répondit: Je vais mesurer Jérusalem, pour voir quelle est sa largeur, et quelle est sa longueur.
Ndipo ndinafunsa kuti, “Kodi ukupita kuti?” Anandiyankha kuti, “Akukayeza Yerusalemu kuti ndidziwe mulifupi mwake ndi mulitali mwake.”
3 Et voici, l'Ange qui parlait avec moi sortit, et un autre Ange sortit au-devant de lui;
Taonani, mngelo amene amayankhula nane uja akuchoka, mngelo wina anabwera kudzakumana naye
4 Et lui dit: Cours, et parle à ce jeune homme-là, en disant: Jérusalem sera habitée sans murailles, à cause de la multitude d'hommes et de bêtes qui seront au milieu d'elle.
ndipo anamuwuza kuti, “Thamanga, kamuwuze mnyamatayo kuti, ‘Yerusalemu udzakhala mzinda wopanda malinga chifukwa mudzakhala anthu ambiri ndiponso ziweto zochuluka.
5 Mais je lui serai, dit l'Eternel, une muraille de feu tout autour, et je serai pour gloire au milieu d'elle.
Ndipo Ine mwini ndidzakhala linga lamoto kuteteza mzindawo,’ akutero Yehova, ‘ndipo ndidzakhala ulemerero mʼkati mwake.’
6 Ha! Fuyez, fuyez hors du pays de l'Aquilon, dit l'Eternel: car je vous ai dispersés vers les quatre vents des cieux, dit l'Eternel.
“Tulukani! Tulukani! Thawaniko ku dziko la kumpoto,” akutero Yehova, “pakuti ndinakumwazirani ku mphepo zinayi zamlengalenga,” akutero Yehova.
7 Ha! Sion qui demeures avec la fille de Babylone, sauve-toi.
“Tuluka, iwe Ziyoni! Thawa, iwe amene umakhala mʼdziko la mwana wamkazi wa Babuloni!”
8 Car ainsi a dit l'Eternel des armées, lequel après la gloire m'a envoyé vers les nations qui vous ont pillés, que qui vous touche, touche la prunelle de son œil.
Pakuti Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Atatha kundilemekeza wanditumiza kwa anthu a mitundu ina amene anakufunkhani; pakuti aliyense wokhudza inu wakhudza mwanadiso wanga.
9 Car voici, je vais lever ma main sur eux, et ils seront en proie à leurs serviteurs, et vous connaîtrez que l'Eternel des armées m'a envoyé.
Ndithu Ine ndidzawamenya anthuwo ndi dzanja langa ndipo amene anali akapolo awo ndiye adzawalande zinthu. Pamenepo mudzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse ndiye wandituma.
10 Réjouis-toi avec chant de triomphe, et t'égaye, fille de Sion; car voici, je viens, et j'habiterai au milieu de toi, dit l'Eternel.
“Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, fuwula ndipo sangalala. Pakuti taona ndikubwera, ndipo ndidzakhala pakati pako,” akutero Yehova.
11 Et plusieurs nations se joindront à l’Eternel en ce jour-là, et deviendront mon peuple; et j'habiterai au milieu de toi; et tu sauras que l'Eternel des armées m'a envoyé vers toi.
“Nthawi imeneyo anthu a mitundu yambiri adzabwera kwa Yehova ndipo adzasanduka anthu anga. Ndidzakhala pakati pako ndipo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse wandituma kwa iwe.
12 Et l'Eternel héritera Juda pour son partage en la terre de sa sainteté, et il choisira encore Jérusalem.
Yehova adzachititsa kuti Yuda akhale chuma chake mʼdziko lopatulika ndipo adzasankhanso Yerusalemu.
13 Que toute chair se taise, devant la face de l'Eternel, car il s'est réveillé de la demeure de sa sainteté.
Khalani chete pamaso pa Yehova anthu nonse, chifukwa Iye wavumbuluka kuchoka ku malo ake opatulika.”

< Zacharie 2 >