< Apocalypse 6 >

1 Et quand l'agneau eut ouvert l'un des sceaux, je regardai, et j'entendis l'un des quatre animaux, qui disait, comme avec une voix de tonnerre: Viens, et vois.
Ndinaona pamene Mwana Wankhosa anatsekula chomatira choyamba cha zomatira zisanu ndi ziwiri zija. Ndipo ndinamva chimodzi mwa zamoyo zinayi zija chikunena liwu lomveka ngati bingu kuti, “Bwera!”
2 Et je regardai, et je vis un cheval blanc; et celui qui était monté dessus avait un arc, et il lui fut donné une couronne; et il sortit victorieux, et afin de vaincre.
Nditayangʼana patsogolo pake ndinaona kavalo woyera! Wokwerapo wake anali ndi uta ndipo anapatsidwa chipewa chaufumu, ndipo anatuluka kupita kukagonjetsa anthu ena.
3 Et quand il eut ouvert le second sceau, j'entendis le second animal, qui disait: Viens, et vois.
Mwana Wankhosa atatsekula chomatira chachiwiri, ndinamva chamoyo chachiwiri chija chikuti, “Bwera!”
4 Et il sortit un autre cheval, qui était roux; et il fut donné à celui qui était monté dessus, de pouvoir ôter la paix de la terre, afin qu'on se tue l'un l'autre; et il lui fut donné une grande épée.
Pamenepo kavalo wina wofiira anatulukira. Wokwerapo wake anapatsidwa mphamvu yochotsa mtendere pa dziko lapansi ndi kuchititsa anthu kuti aziphana wina ndi mnzake. Iyeyu anapatsidwa lupanga lalikulu.
5 Et quand il eut ouvert le troisième sceau, j'entendis le troisième animal qui disait: Viens, et vois; et je regardai, et je vis un cheval noir, et celui qui était monté dessus avait une balance en sa main.
Mwana Wankhosa atatsekula chomatira chachitatu, ndinamva chamoyo chachitatu chikuti, “Bwera!” Nditayangʼana patsogolo panga ndinaona kavalo wakuda! Wokwerapo wake anali ndi masikelo awiri mʼmanja mwake.
6 Et j'entendis au milieu des quatre animaux une voix qui disait: Le chenix de froment pour un denier, et les trois chenix d'orge pour un denier; mais ne nuis point au vin, ni à l'huile.
Ndinamva ngati liwu kuchokera pakati pa zamoyo zinayi zija likuti, “Kilogalamu imodzi ya tirigu mtengo ndi malipiro a tsiku limodzi ndipo makilogalamu atatu a barele mtengo wake ndi malipiro a tsiku limodzi koma usawononge mafuta ndi vinyo!”
7 Et quand il eut ouvert le quatrième sceau, j'entendis la voix du quatrième animal, qui disait: Viens, et vois.
Mwana Wankhosa atatsekula chomatira chachinayi, ndinamva chamoyo chachinayi chija chikunena kuti, “Bwera!”
8 Et je regardai, et je vis un cheval fauve; et celui qui était monté dessus avait nom la Mort, et l'Enfer suivait après lui; et il leur fut donné puissance sur la quatrième partie de la terre, pour tuer avec l'épée, par la famine, par la mortalité, et par les bêtes sauvages de la terre. (Hadēs g86)
Nditayangʼana patsogolo panga ndinaona kavalo wotuwa! Wokwerapo wake dzina lake linali Imfa ndipo Hade inali kumutsatira pambuyo pake. Anapatsidwa ulamuliro pa gawo limodzi la magawo anayi a dziko lapansi kuti aphe ndi lupanga, njala, mliri, ndi zirombo zakuthengo za mʼdziko lapansi. (Hadēs g86)
9 Et quand il eut ouvert le cinquième sceau, je vis sous l'autel les âmes de ceux qui avaient été tués pour la parole de Dieu, et pour le témoignage qu'ils avaient maintenu.
Mwana Wankhosa atatsekula chomatira chachisanu, ndinaona kunsi kwa guwa lansembe kunali mizimu ya anthu amene anaphedwa chifukwa cha Mawu a Mulungu ndi chifukwa chochitira umboni.
10 Et elles criaient à haute voix, disant: Jusqu'à quand, Seigneur, qui es saint et véritable, ne juges-tu point, et ne venges-tu point notre sang de ceux qui habitent sur la terre?
Iwo anafuwula kuti, “Mudzawaleka mpaka liti, Inu Ambuye wamkulu, woyera ndi woona, osawaweruza anthu okhala mʼdziko lapansi ndi kulipsira magazi athu?”
11 Et il leur fut donné à chacun des robes blanches, et il leur fut dit qu'ils se reposassent encore un peu de temps, jusqu'à ce que le nombre de leurs compagnons de service, et de leurs frères qui doivent être mis à mort comme eux, soit complet.
Pamenepo aliyense wa anthuwo anapatsidwa mwinjiro woyera ndipo anawuzidwa kuti adikire pangʼono kufikira chiwerengero cha anzawo ndi abale awo amene anayeneranso kuphedwa ngati iwo, chitakwanira.
12 Et je regardai quand il eut ouvert le sixième sceau, et voici, il se fit un grand tremblement de terre, et le soleil devint noir comme un sac fait de poil, et la lune devint toute comme du sang.
Ndinayangʼanitsitsa pamene ankatsekula chomatira chachisanu ndi chimodzi. Ndipo panachitika chivomerezi champhamvu. Dzuwa linada ngati chiguduli chopanga ndi bweya wambuzi wakuda. Mwezi wonse unafiira ngati magazi,
13 Et les étoiles du ciel tombèrent sur la terre, comme lorsque le figuier étant agité par un grand vent, laisse tomber ses figues [encore] vertes.
ndipo nyenyezi zakuthambo zinagwa pa dziko lapansi ngati muja zimagwera nkhuyu zotsalira mu mtengo mphepo yamphamvu ikawomba.
14 Et le ciel se retira comme un Livre qu'on roule; et toutes les montagnes, et les îles furent remuées de leurs places.
Thambo linachoka ngati amayalulira mphasa ndipo phiri lililonse ndi chilumba chilichonse zinachotsedwa pa malo pake.
15 Et les Rois de la terre, les Princes, les riches, les capitaines, les puissants, tout esclave, et tout [homme] libre se cachèrent dans les cavernes, et entre les rochers des montagnes.
Kenaka, mafumu a pa dziko lapansi, ana a mafumu, atsogoleri a ankhondo, olemera, amphamvu, kapolo aliyense, ndi mfulu aliyense anakabisala kumapanga ndi pakati pa matanthwe a ku mapiri.
16 Et ils disaient aux montagnes et aux rochers: tombez sur nous, et cachez-nous de devant la face de celui qui est assis sur le trône, et de devant la colère de l'agneau;
Iwo anafuwulira mapiri ndi matanthwe kuti, “Tigwereni ndi kutivundikira kuti asatione wokhala pa mpando waufumuyo ndi kupulumuka ku mkwiyo wa Mwana Wankhosa!
17 Car la grande journée de sa colère est venue; et qui est-ce qui pourra subsister?
Pakuti tsiku lalikulu la mkwiyo wawo lafika ndipo ndi ndani angathe kulimbapo?”

< Apocalypse 6 >