< Apocalypse 21 >

1 Puis je vis un nouveau Ciel et une nouvelle terre; car le premier ciel et la première terre avaient disparu, et la mer n'était plus.
Kenaka ndinaona kumwamba kwatsopano ndi dziko lapansi latsopano pakuti kumwamba koyamba ndi dziko lapansi loyamba zinapita ndipo kunalibenso nyanja ina iliyonse.
2 Et moi, Jean, je vis la sainte Cité, la nouvelle Jérusalem, qui descendait du Ciel, de devers Dieu, parée comme une épouse qui s'est ornée pour son mari.
Ndinaona mzinda wopatulika, Yerusalemu watsopano, ukutsika kuchokera kumwamba kwa Mulungu, utakonzedwa ngati mkwatibwi wovala zokongola kukonzekera mwamuna wake.
3 Et j'entendis une grande voix du ciel, disant: voici le Tabernacle de Dieu avec les hommes, et il habitera avec eux; et ils seront son peuple, et Dieu lui-même sera leur Dieu, [et il sera] avec eux.
Ndipo ndinamva mawu ofuwula kuchokera ku Mpando Waufumu kuti, “Taonani! Malo wokhalapo Mulungu ali pakati pa anthu, ndipo Iye adzakhala ndi anthuwo. Iwo adzakhala anthu ake ndipo Mulungu mwini adzakhala nawo nakhala Mulungu wawo.
4 Et Dieu essuiera toutes larmes de leurs yeux, et la mort ne sera plus; et il n'y aura plus ni deuil, ni cri, ni travail; car les premières choses sont passées.
‘Mulungu adzapukuta misozi yonse mʼmaso mwawo. Sikudzakhalanso imfa kapena kukhuza maliro kapena kulira kapena ululu popeza zakale zapita.’”
5 Et celui qui était assis sur le trône, dit: voici, je fais toutes choses nouvelles. Puis il me dit: Ecris, car ces paroles sont véritables et certaines.
Amene anakhala pa mpando waufumuyo anati, “Ndikulenga zinthu zonse zikhale zatsopano!” Ndipo anati, “Lemba izi, pakuti mawu awa ndi okhulupirika ndi woona.”
6 Il me dit aussi: tout est accompli; je suis l'Alpha et l'Oméga, le commencement, et la fin. A celui qui aura soif je lui donnerai de la fontaine d'eau vive, sans qu'elle lui coûte rien.
Iye anandiwuza kuti, “Kwatha. Ine ndine Alefa ndi Omega, Woyamba ndi Wotsiriza. Kwa onse akumva ludzu, ndidzawapatsa zakumwa zaulere zochokera ku kasupe wamadzi amoyo.
7 Celui qui vaincra, héritera toutes choses; et je lui serai Dieu, et il me sera fils.
Iye amene adzapambane adzalandira zonsezi, ndipo ndidzakhala Mulungu wake ndi Iye adzakhala mwana wanga.
8 Mais quant aux timides, aux incrédules, aux exécrables, aux meurtriers, aux fornicateurs, aux empoisonneurs, aux idolâtres et à tous menteurs, leur part sera dans l'étang ardent de feu et de soufre, qui est la mort seconde. (Limnē Pyr g3041 g4442)
Koma amantha, osakhulupirira, okonda zonyansa, opha anthu, achiwerewere, amatsenga, opembedza mafano ndi abodza, malo awo adzakhala nyanja yamoto ya sulufule wotentha. Iyi ndi imfa yachiwiri.” (Limnē Pyr g3041 g4442)
9 Alors un des sept Anges qui avaient eu les sept fioles pleines des sept dernières plaies, s'approcha de moi et me parla en disant: Viens et je te montrerai l'Epouse, qui est la femme de l'Agneau.
Mmodzi wa angelo asanu ndi awiri aja, anali ndi mbale zisanu ndi ziwiri zodzaza ndi miliri yotsiriza isanu ndi iwiri anandiwuza kuti, “Bwera, ine ndidzakuonetsa mkwatibwi wa Mwana Wankhosa.”
10 Et il me transporta en esprit sur une grande et haute montagne, et il me montra la grande Cité, la sainte Jérusalem, qui descendait du Ciel de devers Dieu,
Ndipo anandinyamula mwa Mzimu Woyera kupita nane ku phiri lalikulu ndi lalitali nandionetsa mzinda wopatulika, Yerusalemu ukutsika kuchokera kumwamba kwa Mulungu.
11 Ayant la gloire de Dieu; et sa lumière était semblable à une pierre très précieuse, comme à une pierre de jaspe tirant sur le cristal.
Unawala ndi ulemerero wa Mulungu, ndipo kuthwanima kwake kunali ngati mwala wamtengowapatali, ngati jasipa; woyera ngati krustalo.
12 Et elle avait une grande et haute muraille, avec douze portes, et aux portes douze Anges; et des noms écrits sur elles, qui sont les noms des douze Tribus des enfants d'Israël.
Mzindawo unali ndi mpanda waukulu ndi wautali, unali ndi zipata khumi ndi ziwiri, ndipo panali angelo khumi ndi awiri. Pa chipata chilichonse panayima mngelo. Pa chipata chilichonse panalembedwa dzina la fuko la Israeli.
13 Du côté de l'Orient, trois portes; du côté de l'Aquilon, trois portes; du côté du Midi, trois portes; et du côté de l'Occident, trois portes.
Kummawa kunali zipata zitatu, kumpoto zitatu, kummwera zitatu ndi kumadzulo zitatu.
14 Et la muraille de la Cité avait douze fondements, et les noms des douze Apôtres de l'Agneau étaient écrits dessus.
Mpanda wa mzindawu unali ndi maziko khumi ndi awiri ndipo pa mazikopo panali mayina khumi ndi awiri a atumwi a Mwana Wankhosa.
15 Et celui qui parlait avec moi avait un roseau d'or pour mesurer la Cité, ses portes et sa muraille.
Mngelo amene ankayankhula nane uja anali ndi ndodo yagolide yoyezera mzindawo, zipata zake ndi mpanda wake.
16 Et la cité était bâtie en carré, et sa longueur était aussi grande que sa largeur. Il mesura donc la Cité avec le roseau [d'or], jusqu'à douze mille stades; la longueur, la largeur et la hauteur étaient égales.
Mzindawo unamangidwa mofanana kutalika kwake, mulitali ndi mulifupi munali mofanana. Anayeza mzindawo ndi ndodo ija ndipo anapeza kuti mulitali, mulifupi ndi msinkhu wake kutalika kwake kunali makilomita 2,200.
17 Puis il mesura la muraille, [qui fut] de cent quarante-quatre coudées, de la mesure du personnage, c'est-à-dire, de l'Ange.
Anayesa mpanda uja ndipo kuchindikala kwake kunali kopitirirapo mamita 65 monga mwa muyeso wa anthu umene mngelo anagwiritsa ntchito.
18 Et le bâtiment de la muraille était de jaspe, mais la Cité était d'or pur, semblable à du verre fort transparent.
Mpandawo unapangidwa ndi yasipa, ndipo mzindawo unali wagolide oyengeka owala ngati galasi.
19 Et les fondements de la muraille de la Cité étaient ornés de toute pierre précieuse: le premier fondement était de jaspe; le second, de saphir; le troisième, de calcédoine; le quatrième, d'émeraude;
Maziko a mpanda wa mzindawo anali okongoletsedwa ndi miyala yamtengowapatali ya mtundu uliwonse. Maziko oyamba anali yasipa, achiwiri anali safiro, achitatu ndi kalikedo, achinayi ndi simaragido,
20 Le cinquième, de sardonyx; le sixième, de sardoine; le septième, de chrysolithe; le huitième, de béryl; le neuvième, de topaze; le dixième, de chrysoprase; le onzième, d'hyacinthe; le douzième, d'améthyste.
achisanu ndi sardiyo, achisanu ndi chiwiri ndi krusolito, achisanu ndi chitatu ndi berulo, achisanu ndi chinayi ndi topaziyo, a khumi ndi krusoprazo, a khumi ndi chimodzi ndi huakito, a khumi ndi chiwiri ndi emetusto.
21 Et les douze portes [étaient] douze perles; chacune des portes était d'une perle; et la rue de la cité était d'or pur, comme du verre le plus transparent.
Zipata khumi ndi ziwiri zija zinapangidwa ndi ngale, chipata chilichonse chinapangidwa ndi ngale imodzi. Misewu ya mzindawo inali yopangidwa ndi golide oyengeka, owala ngati galasi.
22 Et je ne vis point de Temple en elle; parce que le Seigneur Dieu Tout-puissant et l'Agneau en sont le Temple.
Ine sindinaone Nyumba ya Mulungu iliyonse mu mzindawo chifukwa Ambuye Mulungu Wamphamvuzonse ndi Mwana Wankhosa ndiwo Nyumba yake.
23 Et la Cité n'a pas besoin du soleil ni de la lune, pour luire en elle; car la clarté de Dieu l'a éclairée, et l'Agneau est son flambeau.
Palibe chifukwa choti dzuwa kapena mwezi ziwale popeza mu mzindawo ulemerero wa Mulungu ndiwo umawalamo ndipo nyale yake ndi Mwana Wankhosa uja.
24 Et les nations qui auront été sauvées, marcheront à la faveur de sa lumière; et les Rois de la terre y apporteront ce qu'ils ont de plus magnifique et de plus précieux.
Mitundu ya anthu idzayenda mʼkuwala kwake ndipo mafumu a dziko lapansi adzabweretsa ulemerero wawo mu mzindamo.
25 Et ses portes ne seront point fermées de jour; or il n'y aura point là de nuit.
Zipata zake sizidzatsekedwa ngakhale tsiku limodzi lomwe pakuti sikudzakhala usiku kumeneko.
26 Et on y apportera ce que les Gentils ont de plus magnifique et de plus précieux.
Ulemerero ndi ulemu wa mitundu ya anthu adzapita nazo kumeneko.
27 Il n'y entrera aucune chose souillée, ni personne qui s'abandonne à l'abomination et au mensonge; mais seulement ceux qui sont écrits au Livre de vie de l'Agneau.
Kanthu kosayeretsedwa sikadzalowamo, kuphatikizanso aliyense wochita zinthu zochititsa manyazi ndi zachinyengo, koma okhawo amene mayina awo alembedwa mʼbuku lamoyo la Mwana Wankhosa.

< Apocalypse 21 >