< Apocalypse 2 >

1 Ecris à l'Ange de l'Eglise d'Ephèse: celui qui tient les sept étoiles en sa main droite, et qui marche au milieu des sept chandeliers d'or, dit ces choses:
“Lembera mngelo wa mpingo wa ku Efeso kuti: Awa ndi mawu ochokera kwa amene ali ndi nyenyezi zisanu ndi ziwiri zija mʼdzanja lake lamanja amene akuyenda pakati pa zoyikapo nyale zisanu ndi ziwiri zagolide.
2 Je connais tes œuvres, ton travail et ta patience, et [je sais] que tu ne peux souffrir les méchants, et que tu as éprouvé ceux qui se disent être apôtres, et ne le sont point, et que tu les as trouvés menteurs.
Ine ndimadziwa zochita zako, ntchito yako yowawa ndi kupirira kwako. Ine ndimadziwa kuti sungalekerere anthu oyipa amene amadzitcha atumwi pamene sichoncho, unawayesa, ndipo unawapeza kuti ndi abodza.
3 Et que tu as souffert, et que tu as eu patience, et que tu as travaillé pour mon Nom, et que tu ne t'es point lassé.
Iwe wapirira ndipo wakumana ndi zovuta chifukwa cha dzina langa, ndipo sunatope.
4 Mais j'ai [quelque chose] contre toi, c'est que tu as abandonné ta première charité.
Komabe ndili ndi chotsutsana nawe: Wataya chikondi chako chapoyamba.
5 C'est pourquoi souviens-toi d'où tu es déchu, et t'en repens, et fais les premières œuvres; autrement je viendrai à toi bientôt, et j'ôterai ton chandelier de son lieu, si tu ne te repens.
Kumbukirani kuti munagwa kuchokera patali. Lapa ndikuchita zinthu zimene unkachita poyamba. Ngati sulapa ndidzabwera ndikukuchotsera choyikapo nyale chako pamalo pake.
6 Mais pourtant tu as ceci [de bon] que tu hais les actions des Nicolaïtes, lesquelles je hais moi aussi.
Komabe chokomera chako ndi chakuti umadana ndi zochita za Anikolai, zimene Inenso ndimadana nazo.
7 Que celui qui a des oreilles, écoute ce que l'Esprit dit aux Eglises. A celui qui vaincra je lui donnerai à manger de l'arbre de vie, qui est au milieu du paradis de Dieu.
Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo. Amene adzapambana, ndidzamupatsa ufulu wakudya zipatso za mtengo wopatsa moyo umene uli ku paradizo wa Mulungu.
8 Ecris aussi à l'Ange de l'Eglise de Smyrne: Le premier et le dernier, qui a été mort, et qui est retourné en vie, dit ces choses:
“Lembera mngelo wa mpingo wa ku Simurna kuti: Awa ndi mawu ochokera kwa amene ndi Woyamba ndi Wotsiriza, amene anafa nʼkukhalanso ndi moyo.
9 Je connais tes œuvres, ton affliction et ta pauvreté (mais tu es riche), et le blasphème de ceux qui se disent être Juifs, et qui ne le sont point, mais [qui sont] la Synagogue de satan.
Ine ndimadziwa masautso ako ndi umphawi wako, chonsecho ndiwe wolemera! Ndikudziwa zimene amakusinjirira anthu amene amati ndi Ayuda pamene sizili choncho, koma ndi a mpingo wa Satana.
10 Ne crains rien des choses que tu as à souffrir. Voici, il arrivera que le Démon mettra quelques-uns de vous en prison, afin que vous soyez éprouvés; et vous aurez une affliction de dix jours. Sois fidèle jusques à la mort, et je te donnerai la couronne de vie.
Musachite mantha ndi zimene muti musauke nazo posachedwapa. Ndithu, Satana adzayika ena a inu mʼndende pofuna kukuyesani, ndipo mudzazunzika kwa masiku khumi. Khalani okhulupirika ngakhale zitafika pa imfa, ndipo Ine ndidzakupatsani chipewa cha ulemerero wamoyo.
11 Que celui qui a des oreilles, écoute ce que l'Esprit dit aux Eglises. Celui qui vaincra sera mis à couvert de la mort seconde.
Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo. Amene adzapambana sadzapwetekedwa ndi pangʼono pomwe ndi imfa yachiwiri.
12 Ecris aussi à l'Ange de l'Eglise de Pergame: Celui qui a l'épée aiguë à deux tranchants, dit ces choses.
“Lembera mngelo wa mpingo wa ku Pergamo kuti: Awa ndi mawu ochokera kwa amene ali ndi lupanga lakuthwa konsekonse.
13 Je connais tes œuvres, et où tu habites, [savoir] là où est le siège de satan, et que cependant tu retiens mon Nom, et que tu n'as point renoncé ma foi, non pas même lorsqu'Antipas, mon fidèle martyr, a été mis à mort entre vous, là où satan habite.
Iye akuti, ‘Ine ndimadziwa kumene mumakhala, kumene kuli mpando waufumu wa Satana. Komabe inu ndinu okhulupirika kwa Ine. Simunataye chikhulupiriro chanu pa Ine, ngakhale mʼmasiku a Antipa, mboni yanga yokhulupirika, amene anaphedwa mu mzinda wanu, kumene amakhala Satana.
14 Mais j'ai quelque peu de chose contre toi: c'est que tu en as là qui retiennent la doctrine de Balaam, lequel enseignait Balac à mettre un scandale devant les enfants d'Israël, afin qu'ils mangeassent des choses sacrifiées aux idoles, et qu'ils se livrassent à la fornication.
Komabe, ndili ndi zinthu zingapo zotsutsana nanu. Kumeneko muli ndi anthu ena amene amatsata ziphunzitso za Balaamu, uja amene anaphunzitsa Baraki kukopa Aisraeli kuti azidya nsembe zoperekedwa ku mafano ndi kumachita chigololo.
15 Ainsi tu en as, toi aussi, qui retiennent la doctrine des Nicolaïtes; ce que je hais.
Chimodzimodzinso inuyo muli ndi ena amene amatsatira ziphunzitso za Anikolai.
16 Repens-toi: autrement je viendrai à toi bientôt; et je combattrai contre eux par l'épée de ma bouche.
Tsono tembenukani mtima. Mukapanda kutero, ndidzabwera kwanuko posachedwa ndipo ndidzachita nanu nkhondo ndi lupanga lotuluka mʼkamwa mwanga lija.
17 Que celui qui a des oreilles, écoute ce que l'Esprit dit aux Eglises. A celui qui vaincra je lui donnerai à manger de la manne qui est cachée, et je lui donnerai un caillou blanc, et sur [ce] caillou sera écrit un nouveau nom, que nul ne connaît, sinon celui qui le reçoit.
Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo. Kwa amene adzapambane ndidzamupatsa chakudya chobisika cha mana. Ndidzamupatsanso mwala woyera wolembedwapo dzina latsopano, lodziwa iye yekha amene walandirayo.’”
18 Ecris aussi à l'Ange de l'Eglise de Thyatire: Le Fils de Dieu, qui a ses yeux comme une flamme de feu, et dont les pieds sont semblables à de l'airain très luisant, dit ces choses.
“Lembera mngelo wampingo wa ku Tiyatira kuti: Awa ndi mawu ochokera kwa Mwana wa Mulungu, amene maso ake ali ngati moto woyaka ndi mapazi ake ngati chitsulo chonyezimira.
19 Je connais tes œuvres, [ta] charité, ton ministère, ta foi, ta patience, et que tes dernières œuvres surpassent les premières;
Iye akuti: Ndimadziwa ntchito zanu, chikondi chanu ndi chikhulupiriro chanu, kutumikira kwanu ndi kupirira kwanu. Ndikudziwa tsopano kuti ntchito zanu ndi zabwino kuposa zoyamba zija.
20 Mais j'ai quelque peu de chose contre toi: c'est que tu souffres que [cette] femme Jézabel, qui se dit prophétesse, enseigne, et qu'elle séduise mes serviteurs, pour les porter à la fornication, et pour [leur faire] manger des choses sacrifiées aux idoles.
Komabe ndili ndi chinthu chokudzudzula nacho. Umamulekerera mkazi uja Yezebeli amene amadzitcha yekha kuti ndi mneneri. Iye amaphunzitsa atumiki anga kuti azichita zadama ndi kumadya zansembe zoperekedwa ku mafano.
21 Et je lui ai donné du temps, afin qu'elle se repentit de sa prostitution; mais elle ne s'est point repentie.
Ndamupatsa nthawi kuti aleke zachigololo zake koma sakufuna.
22 Voici, je vais la réduire au lit, et [mettre] dans une grande affliction ceux qui commettent adultère avec elle, s'ils ne se repentent de leurs œuvres;
Tsono ndidzamugwetsa mʼmasautso ndipo amene amachita naye zadama zakezo ndidzawasautsa kwambiri akapanda kulapa ndi kuleka njira za mkaziyo.
23 Et je ferai mourir de mort ses enfants; et toutes les Eglises connaîtront que je suis celui qui sonde les reins et les cœurs; et je rendrai à chacun de vous selon ses œuvres.
Ana ake ndidzawakantha ndi kuwapheratu. Kotero mipingo yonse idzadziwa kuti Ine ndine uja amene ndimafufuza mʼmitima mwa anthu ndi mʼmaganizo mwawo. Aliyense wa inu ndidzachita naye monga mwa ntchito zake.
24 Mais je vous dis à vous et aux autres qui sont à Thyatire, à tous ceux qui n'ont point cette doctrine, et qui n'ont point connu les profondeurs de satan, comme ils parlent, que je ne mettrai point sur vous d'autre charge.
Tsopano ndikunena kwa enanu a ku Tiyatira, kwa inu amene simunatsate chiphunzitso cha mkaziyo ndipo simunaphunzire zimene iwo amati ndi ‘zinsinsi zonama’ za Satana. Kwa inu mawu anga ndi akuti sindikuwunjikirani malamulo ena.
25 Mais retenez ce que vous avez, jusqu'à ce que je vienne.
Inu mungogwiritsa zimene munaphunzira basi, mpaka Ine ndidzabwere.
26 Car à celui qui aura vaincu, et qui aura gardé mes œuvres jusqu'à la fin, je lui donnerai puissance sur les nations:
Amene adzapambana ndi kuchita chifuniro changa mpaka kumapeto, ndidzamupatsa ulamuliro pa mitundu yonse ya anthu.
27 Et il les gouvernera avec une verge de fer, et elles seront brisées comme les vaisseaux d'un potier, selon que je l'ai aussi reçu de mon Père.
Adzayilamulira ndi ndodo yachitsulo ndipo nadzayiphwanyaphwanya ngati mbiya. Ulamuliro umenewu ndi omwe ndinalandira kwa Atate anga.
28 Et je lui donnerai l'étoile du matin.
Ine ndidzamupatsanso nthanda, nyenyezi yowala mʼmamawa ija.
29 Que celui qui a des oreilles, écoute ce que l'Esprit dit aux Eglises.
Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo.

< Apocalypse 2 >