< Psaumes 63 >

1 Psaume de David, lorsqu'il était dans le désert de Juda. Ô Dieu! tu es mon [Dieu] Fort, je te cherche au point du jour; mon âme a soif de toi, ma chair te souhaite en cette terre déserte, altérée, [et] sans eau.
Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda. Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga, moona mtima ine ndimakufunafunani; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu, thupi langa likulakalaka inu, mʼdziko lowuma ndi lotopetsa kumene kulibe madzi.
2 Pour voir ta force et ta gloire, ainsi que je t'ai contemplé dans ton Sanctuaire.
Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.
3 Car ta gratuité est meilleure que la vie; mes lèvres te loueront.
Chifukwa chikondi chanu ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.
4 Et ainsi je te bénirai durant ma vie, [et] j'élèverai mes mains en ton Nom.
Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga, ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.
5 Mon âme est rassasiée comme de mœlle et de graisse; et ma bouche te loue avec un chant de réjouissance.
Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona. Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.
6 Quand je me souviens de toi dans mon lit, je médite de toi durant les veilles de la nuit.
Pa bedi panga ndimakumbukira inu; ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.
7 Parce que tu m'as été en secours, à cause de cela je me réjouirai à l'ombre de tes ailes.
Chifukwa ndinu thandizo langa, ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.
8 Mon âme s'est attachée à toi pour te suivre, [et] ta droite me soutient.
Moyo wanga umakangamira Inu; dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.
9 Mais ceux-ci qui demandent que mon âme tombe en ruine, entreront au plus bas de la terre.
Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa; adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.
10 On les détruira à coups d'épée; ils seront la portion des renards.
Iwo adzaperekedwa ku lupanga ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.
11 Mais le Roi se réjouira en Dieu; [et] quiconque jure par lui s'en glorifiera; car la bouche de ceux qui mentent sera fermée.
Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu; onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo, koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.

< Psaumes 63 >