< Psaumes 47 >

1 Psaume des enfants de Coré, [donné] au maître chantre. Peuples battez tous des mains, jetez des cris de réjouissance à Dieu avec une voix de triomphe.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Ombani mʼmanja, inu anthu onse; fuwulani kwa Mulungu ndi mawu achimwemwe.
2 Car l'Eternel qui est le Souverain est terrible et il est grand Roi sur toute la terre.
Ndi woopsadi Yehova Wammwambamwamba; Mfumu yayikulu ya dziko lonse lapansi!
3 Il range les peuples sous nous, et les nations, sous nos pieds.
Iye anatigonjetsera mitundu yambirimbiri ya anthu; anayika anthu pansi pa mapazi athu.
4 Il nous a choisi, notre héritage, qui est la magnificence de Jacob, lequel il aime; (Sélah)
Iye anatisankhira cholowa chathu, chonyaditsa cha Yakobo, amene anamukonda. (Sela)
5 Dieu est monté avec un cri de réjouissance; l'Eternel [est monté] avec un son de trompette.
Mulungu wakwera, anthu akumufuwulira mwachimwemwe, Yehova wakwera, akumuyimbira malipenga.
6 Psalmodiez à Dieu, psalmodiez, psalmodiez à notre Roi, psalmodiez.
Imbani matamando kwa Mulungu, imbani matamando; imbani matamando kwa mfumu yathu, imbani matamando.
7 Car Dieu est le Roi de toute la terre; tout homme entendu, psalmodiez.
Pakuti Mulungu ndi mfumu ya dziko lonse lapansi; imbirani Iye salimo la matamando.
8 Dieu règne sur les nations; Dieu est assis sur le trône de sa sainteté.
Mulungu akulamulira mitundu ya anthu; Mulungu wakhala pa mpando wake waufumu woyera.
9 Les principaux des peuples se sont assembles [vers] le peuple du Dieu d'Abraham; car les boucliers de la terre sont à Dieu; il est fort exalté.
Anthu otchuka mwa anthu a mitundu ina asonkhana monga anthu a Mulungu wa Abrahamu, pakuti mafumu a dziko lapansi ndi ake a Mulungu; Iye wakwezedwa kwakukulu.

< Psaumes 47 >