< Psaumes 43 >

1 Fais-moi justice, ô Dieu! et soutiens mon droit contre la nation cruelle; délivre-moi de l'homme trompeur et pervers.
Onetsani kusalakwa kwanga Inu Mulungu; ndipo mundinenere mlandu wanga kutsutsana ndi mtundu wosapembedza; mundilanditse mʼmanja mwa achinyengo ndi anthu oyipa.
2 Puisque tu es le Dieu de ma force, pourquoi m'as-tu rejeté? pourquoi marcherai-je en deuil à cause de l'oppression de l'ennemi?
Pajatu Inu Mulungu ndinu mphamvu zanga. Nʼchifukwa chiyani mwandikana ine? Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira, woponderezedwa ndi mdani?
3 Envoie ta lumière et ta vérité, afin qu'elles me conduisent [et] m'introduisent en la montagne de ta Sainteté, et en tes Tabernacles.
Tumizani kuwunika kwanu ndi choonadi chanu kuti zinditsogolere; mulole kuti zindifikitse ku phiri lanu loyera, kumalo kumene inu mumakhala.
4 Alors je viendrai à l'Autel de Dieu, vers le [Dieu] Fort de l'allégresse de ma joie, et je te célébrerai sur le violon, ô Dieu! mon Dieu!
Ndipo ndidzapita ku guwa lansembe la Mulungu, kwa Mulungu, chimwemwe changa ndi chikondwerero changa. Ndidzakutamandani ndi zeze, Inu Mulungu wanga.
5 Mon âme, pourquoi t'abats-tu, et pourquoi frémis-tu au-dedans de moi? Attends-toi à Dieu; car je le célébrerai encore; il est ma délivrance, et mon Dieu.
Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni iwe moyo wanga? Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga? Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamutamandabe Iye, Mpulumutsi wanga ndi Mulungu wanga.

< Psaumes 43 >