< Psaumes 19 >

1 Psaume de David, [donné] au maître chantre. Les cieux racontent la gloire du [Dieu] Fort, et l'étendue donne à connaître l'ouvrage de ses mains.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Zakumwamba zimalengeza za ulemerero wa Mulungu; thambo limalalikira ntchito za manja ake.
2 Un jour fournit en abondance de quoi parler à [l'autre] jour, et une nuit montre la science à [l'autre] nuit.
Tsiku ndi tsiku zimayankhula mawu ambiri, usiku ndi usiku zimaonetsa poyera nzeru.
3 Il n'y a point [en eux] de langage, il n'y a point de paroles; toutefois leur voix est ouïe.
Palibe kuyankhula, palibe mawu aliwonse; liwu lawo silimveka.
4 Leur contour couvre toute la terre, et leur voix est allée jusqu'au bout du monde habitable. Il a posé en eux un pavillon pour le soleil;
Koma uthenga wawo umapita pa dziko lonse lapansi, mawuwo amafika mpaka kumalekezero a dziko lapansi.
5 Tellement qu'il est semblable à un époux sortant de son cabinet nuptial; il s'égaie comme un homme vaillant pour faire sa course.
Dzuwa lili ngati mkwatibwi wobwera kuchokera ku nsanja yake, ngati katswiri wokondwerera kuthamanga pa mpikisano.
6 Son départ est de l'un des bouts des cieux, et son tour se fait sur l'un et sur l'autre bout, et il n'y a rien qui se puisse mettre à couvert de sa chaleur.
Limatuluka kuyambira mbali ina ya thambo ndi kuzungulira mpaka mbali inanso; palibe chinthu chotha kupewa kutentha kwake.
7 La Loi de l'Eternel est parfaite, restaurant l'âme; le témoignage de l'Eternel est assuré, donnant la sagesse au simple.
Lamulo la Yehova ndi langwiro, kutsitsimutsa moyo. Maumboni a Yehova ndi odalirika, amapereka nzeru kwa wopanda nzeru.
8 Les commandements de l'Eternel sont droits, ils réjouissent le cœur; le commandement de l'Eternel est pur, et fait que les yeux voient.
Malangizo a Yehova ndi olungama, amapereka chimwemwe mu mtima. Malamulo a Yehova ndi onyezimira, amapereka kuwala.
9 La crainte de l'Eternel est pure, permanente à perpétuité; les jugements de l'Eternel ne sont que vérité, et ils se trouvent pareillement justes.
Kuopa Yehova ndiye chinthu changwiro, chimakhala mpaka muyaya. Maweruzo a Yehova ndi owona ndipo onse ndi olungama;
10 Ils sont plus désirables que l'or, même que beaucoup de fin or; et plus doux que le miel, même que ce qui distille des rayons de miel.
ndi a mtengowapatali kuposa golide, kuposa golide weniweni; ndi otsekemera kuposa uchi, kuposa uchi wochokera pa chisa chake.
11 Aussi ton serviteur est rendu éclairé par eux, et il y a un grand salaire à les observer.
Mtumiki wanu amachenjezedwa nawo; powasunga pali mphotho yayikulu.
12 Qui est-ce qui connaît ses fautes commises par erreur? Purifie-moi de mes fautes cachées.
Ndani angathe kudziwa zolakwa zake? Mundikhululukire zolakwa zanga zobisika.
13 Eloigne aussi ton serviteur des actions commises par fierté, en sorte qu'elles ne dominent point en moi; alors je serai pur, et serai net des grands crimes.
Muteteze mtumiki wanunso ku machimo ochita akudziwa; iwo asandilamulire. Kotero ndidzakhala wosalakwa, wopanda mlandu wa tchimo lalikulu.
14 Que les propos de ma bouche, et la méditation de mon cœur te soient agréables, ô Eternel! mon rocher, et mon Rédempteur.
Mawu a mʼkamwa mwanga ndi zolingalira za mu mtima mwanga zikhale zokondweretsa pamaso panu, Inu Yehova, Thanthwe langa ndi Mpulumutsi wanga.

< Psaumes 19 >