< Psaumes 116 >

1 J'aime l'Eternel, car il a exaucé ma voix, [et] mes supplications.
Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
2 Car il a incliné son oreille vers moi, c'est pourquoi je l'invoquerai durant mes jours.
Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
3 Les cordeaux de la mort m'avaient environné, et les détresses du sépulcre m'avaient rencontré; j'avais rencontré la détresse et l'ennui. (Sheol h7585)
Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol h7585)
4 Mais j'invoquai le Nom de l’Eternel, [en disant]: je te prie, ô Eternel! délivre mon âme.
Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
5 L'Eternel est pitoyable et juste, et notre Dieu fait miséricorde.
Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
6 L'Eternel garde les simples; j'étais devenu misérable, et il m'a sauvé.
Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
7 Mon âme, retourne en ton repos; car l'Eternel t'a fait du bien.
Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
8 Parce que tu as mis à couvert mon âme de la mort, mes yeux de pleurs, [et] mes pieds de chute.
Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
9 Je marcherai en la présence de l'Eternel dans la terre des vivants.
kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
10 J'ai cru, c'est pourquoi j'ai parlé; j'ai été fort affligé.
Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
11 Je disais en ma précipitation: tout homme est menteur.
Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
12 Que rendrai-je à l'Eternel? tous ses bienfaits sont sur moi.
Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
13 Je prendrai la coupe des délivrances, et j'invoquerai le Nom de l’Eternel.
Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
14 Je rendrai maintenant mes vœux à l'Eternel, devant tout son peuple.
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
15 [Toute sorte] de mort des bien-aimés de l'Eternel est précieuse devant ses yeux.
Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
16 Ouï, ô Eternel! car je suis ton serviteur, je suis ton serviteur, fils de ta servante, tu as délié mes liens.
Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
17 Je te sacrifierai des sacrifices d'actions de grâces, et j'invoquerai le Nom de l’Eternel.
Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
18 Je rendrai maintenant mes vœux à l'Eternel, devant tout son peuple;
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
19 Dans les parvis de la maison de l'Eternel, au milieu de toi, Jérusalem. Louez l'Eternel.
mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.

< Psaumes 116 >