< Psaumes 114 >

1 Quand Israël sortit d'Egypte, [et] la maison de Jacob d'avec le peuple barbare,
Pamene Israeli anatuluka mu Igupto, nyumba ya Yakobo kuchoka ku mtundu wa anthu a chiyankhulo chachilendo,
2 Juda devint une chose sacrée à Dieu, [et] Israël son empire.
Yuda anasanduka malo opatulika a Mulungu, Israeli anasanduka ufumu wake.
3 La mer le vit, et s'enfuit, le Jourdain s'en retourna en arrière.
Nyanja inaona ndi kuthawa, mtsinje wa Yorodani unabwerera mʼmbuyo;
4 Les montagnes sautèrent comme des moutons, [et] les coteaux comme des agneaux.
mapiri analumphalumpha ngati nkhosa zazimuna, timapiri ngati ana ankhosa.
5 Ô mer! qu'avais-tu pour t'enfuir? [et toi] Jourdain, pour retourner en arrière?
Nʼchifukwa chiyani iwe unathawa? iwe mtsinje wa Yorodani unabwereranji mʼmbuyo?
6 [Et] vous montagnes, que vous ayez sauté comme des moutons; et vous coteaux, comme des agneaux?
inu mapiri, munalumphalumphiranji ngati nkhosa zazimuna, inu timapiri, ngati ana ankhosa?
7 Ô terre! tremble pour la présence du Seigneur, pour la présence du Dieu de Jacob;
Njenjemera pamaso pa Ambuye iwe dziko lapansi, pamaso pa Mulungu wa Yakobo,
8 Qui a changé le rocher en un étang d'eaux, [et] la pierre très dure en une source d'eaux.
amene anasandutsa thanthwe kukhala chitsime, thanthwe lolimba kukhala akasupe a madzi.

< Psaumes 114 >