< Proverbes 14 >

1 Toute femme sage bâtit sa maison; mais la folle la ruine de ses mains.
Mkazi wanzeru amamanga banja lake, koma mkazi wopusa amalimasula ndi manja ake omwe.
2 Celui qui marche en sa droiture, révère l'Eternel; mais celui qui va de travers en ses voies, le méprise.
Amene amayenda molungama amaopa Yehova, koma amene njira zake ndi zoyipa amanyoza Yehova.
3 La verge d'orgueil est dans la bouche du fou; mais les lèvres des sages les garderont.
Kuyankhula kwa chitsiru kumamuyitanira ndodo pa msana, koma milomo ya munthu wanzeru imamuteteza.
4 Où il n'y a point de bœuf, la grange est vide; et l'abondance du revenu provient de la force du bœuf.
Pakasowa ngʼombe zolima gome limakhala lopanda chakudya, koma pakakhala ngʼombe zamphamvu zakudya zimachulukanso.
5 Le témoin véritable ne mentira [jamais]; mais le faux témoin avance volontiers des mensonges.
Mboni yokhulupirika sinama, koma mboni yonyenga imayankhula zabodza.
6 Le moqueur cherche la sagesse, et ne la trouve point; mais la science est aisée à trouver à l'homme intelligent.
Wonyoza anzake amafunafuna nzeru koma osayipeza, koma munthu womvetsa bwino amadziwa zinthu msanga.
7 Eloigne-toi de l'homme insensé, puisque tu ne lui as point connu de lèvres de science.
Khala kutali ndi munthu wopusa chifukwa sudzapeza mawu a nzeru.
8 La sagesse de l'homme bien avisé est d'entendre sa voie; mais la folie des fous n'est que tromperie.
Nzeru za munthu wochenjera zagona pakuzindikira njira zake. Koma uchitsiru wa zitsiru umapusitsidwa ndi chinyengo chawo chomwe.
9 Les fous pallient le délit; mais il n'y a que plaisir entre les hommes droits.
Zitsiru zimanyoza za kulapa machimo, awo, koma kufuna kwabwino kumapezeka mwa anthu olungama.
10 Le cœur d'un chacun connaît l'amertume de son âme; et un autre n'est point mêlé dans sa joie.
Mtima uliwonse umadziwa wokha zowawa zake, ndipo palibe wina aliyense angadziwe kukondwa kwake.
11 La maison des méchants sera abolie; mais le tabernacle des hommes droits fleurira.
Nyumba ya munthu woyipa idzapasuka, koma tenti ya munthu wowongoka mtima idzakhazikika.
12 Il y a telle voie qui semble droite à l'homme, mais dont l'issue sont les voies de la mort.
Pali njira ina yooneka ngati yabwino kwa munthu, koma kumatsiriziro kwake ndi ku imfa.
13 Même en riant le cœur sera triste, et la joie finit par l'ennui.
Ngakhale poseka mtima utha kumva kuwawa, ndipo mathero achimwemwe akhoza kukhala chisoni.
14 Celui qui a un cœur hypocrite, sera rassasié de ses voies; mais l'homme de bien [le sera] de ce qui est en lui.
Munthu wosakhulupirika adzalandira zogwirizana ndi ntchito yake, koma munthu wabwino adzalandira mphotho ya ntchito yake.
15 Le simple croit à toute parole; mais l'homme bien avisé considère ses pas.
Munthu wopusa amakhulupirira chilichonse, koma munthu wochenjera amaganizira bwino mayendedwe ake.
16 Le sage craint, et se retire du mal; mais le fou se met en colère, et se tient assuré.
Munthu wanzeru amaopa Mulungu ndipo amapewa zoyipa, koma munthu wopusa ndi wokula mtima amakhala wosasamala.
17 L'homme colère fait des folies; et l'homme rusé est haï.
Munthu wopsa mtima msanga amachita zinthu za uchitsiru, ndipo anthu amadana ndi munthu wachinyengo.
18 Les niais hériteront la folie; mais les bien-avisés seront couronnés de science.
Anthu opusa amalandira uchitsiru, koma anthu ochenjera amavekedwa chipewa cha ulemerero wa kudziwa zinthu.
19 Les malins seront humiliés devant les bons, et les méchants, devant les portes du juste.
Anthu oyipa adzagwada pamaso pa anthu abwino, ndipo anthu oyipa adzapempha thandizo kwa anthu olungama.
20 Le pauvre est haï, même de son ami; mais les amis du riche sont en grand nombre.
Munthu wosauka ngakhale anansi ake omwe amamuda, koma munthu wolemera ali ndi abwenzi ambiri.
21 Celui qui méprise son prochain s'égare; mais celui qui a pitié des débonnaires, est bienheureux.
Wonyoza mnansi wake ndi wochimwa koma ndi wodala amene amachitira chifundo anthu osowa.
22 Ceux qui machinent du mal ne se fourvoient-ils pas? Mais la bonté et la vérité seront pour ceux qui procurent le bien.
Kodi amene amakonzekera zoyipa sasochera? Koma amene amakonzekera zabwino anthu amawaonetsa chikondi ndi kukhulupirika.
23 En tout travail il y a quelque profit, mais le babil des lèvres ne tourne qu'à disette.
Ntchito iliyonse imakhala ndi phindu, koma kuyankhulayankhula kumabweretsa umphawi.
24 Les richesses des sages leur sont [comme] une couronne; mais la folie des fous n'est que folie.
Chipewa chaulemu cha anthu a nzeru ndi chuma chawo chomwe, koma malipiro a zitsiru ndi uchitsiru.
25 Le témoin véritable délivre les âmes; mais celui qui prononce des mensonges, n'est que tromperie.
Mboni yokhulupirika imapulumutsa miyoyo, koma mboni yabodza imaphetsa.
26 En la crainte de l'Eternel il y a une ferme assurance, et une retraite pour ses enfants.
Amene amaopa Yehova ali ndi chitetezo chokwanira ndipo iye adzakhala pothawira pa ana ake.
27 La crainte de l'Eternel est une source de vie pour se détourner des filets de la mort.
Kuopa Yehova ndiye kasupe wamoyo, kumathandiza munthu kuti apewe msampha wa imfa.
28 La puissance d'un Roi consiste dans la multitude du peuple; mais quand le peuple diminue, c'est l'abaissement du Prince.
Gulu lalikulu la anthu ndiye ulemerero wa mfumu, koma popanda anthu kalonga amawonongeka.
29 Celui qui est lent à la colère, est de grande intelligence; mais celui qui est prompt à se courroucer, excite la folie.
Munthu wosapsa mtima msanga amamvetsa zinthu kwambiri, koma munthu wopsa mtima msanga amaonetsa uchitsiru wake.
30 Le cœur doux est la vie de la chair; mais l'envie est la vermoulure des os.
Mtima wodekha umapatsa thupi moyo, koma nsanje imawoletsa mafupa.
31 Celui qui fait tort au pauvre, déshonore celui qui l'a fait; mais celui-là l'honore, qui a pitié du nécessiteux.
Amene amapondereza mʼmphawi amanyoza mlengi wake, koma wochitira chifundo munthu wosowa amalemekeza Mulungu.
32 Le méchant sera poussé au loin par sa malice; mais le juste trouve retraite [même] en sa mort.
Anthu oyipa adzakanthidwa chifukwa cha ntchito zawo zomwe, koma olungama adzatetezedwa mwa imfa yawo.
33 La sagesse repose au cœur de l'homme intelligent; et elle est même reconnue au milieu des fous.
Nzeru zimakhala mu mtima mwa anthu omvetsa zinthu, koma nzeru sipezeka mu mtima mwa zitsiru.
34 La justice élève une nation; mais le péché est l'opprobre des peuples.
Chilungamo chimakweza mtundu wa anthu, koma uchimo umachititsa manyazi mtundu uliwonse.
35 Le Roi prend plaisir au serviteur prudent; mais son indignation sera contre celui qui lui fait déshonneur.
Mfumu imasangalatsidwa ndi wantchito wanzeru, koma imachitira ukali wantchito wochititsa manyazi.

< Proverbes 14 >