< Proverbes 13 >

1 L'enfant sage écoute l'instruction de son père, mais le moqueur n'écoute point la répréhension.
Mwana wanzeru amamvera malangizo a abambo ake, koma mwana wonyoza samamvetsera chidzudzulo.
2 L'homme mangera du bien par le fruit de sa bouche; mais l'âme de ceux qui agissent perfidement, mangera l'extorsion.
Munthu amapeza zinthu zabwino chifukwa cha mawu ake, koma anthu osakhulupirika amalakalaka zachiwawa basi.
3 Celui qui garde sa bouche, garde son âme; mais celui qui ouvre à tout propos ses lèvres, tombera en ruine.
Iye amene amagwira pakamwa pake amateteza moyo wake, koma amene amayankhula zopanda pake adzawonongeka.
4 L'âme du paresseux ne fait que souhaiter, et il n'a rien; mais l'âme des diligents sera engraissée.
Munthu waulesi amakhumbira zinthu koma sapeza kanthu, koma munthu wakhama adzalemera.
5 Le juste hait la parole de mensonge, mais elle met le méchant en mauvaise odeur, et le fait tomber dans la confusion.
Munthu wolungama amadana ndi zabodza, koma zochita za munthu woyipa zimanyansa ndiponso zimachititsa manyazi.
6 La justice garde celui qui est intègre dans sa voie, mais la méchanceté renversera celui qui s'égare.
Chilungamo chimateteza munthu wangwiro, koma tchimo limagwetsa munthu wochimwa.
7 Tel fait du riche, qui n'a rien du tout; et tel fait du pauvre, qui a de grandes richesses.
Wina amadziyesa kuti ndi wolemera chonsecho alibe kanthu kalikonse; munthu wina amaoneka ngati wosauka chonsecho ali ndi chuma chambiri.
8 Les richesses font que l'homme est rançonné; mais le pauvre n'entend point de menaces.
Chuma cha munthu wolemera chitha kuwombola moyo wake, koma munthu wosauka amamva chidzudzulo.
9 La lumière des justes sera gaie; mais la lampe des méchants sera éteinte.
Nyale ya munthu wolungama ndi yokondweretsa, koma nyale ya munthu woyipa imazimitsidwa.
10 L'orgueil ne produit que querelle; mais la sagesse est avec ceux qui prennent conseil.
Chipongwe chosamalabadirako za anthu ena chimadzetsa mikangano, koma womva malangizo a anzawo ndiwo ali ndi nzeru.
11 Les richesses provenues de vanité seront diminuées; mais celui qui amasse avec la main, les multipliera.
Chuma chochipeza mofulumira chidzatha pangʼonopangʼono koma chuma chosonkhanitsidwa pangʼonopangʼono chidzachulukirachulukira.
12 L'espoir différé fait languir le cœur; mais le souhait qui arrive, est [comme] l'arbre de vie.
Chinthu chochiyembekezera chikalephereka chimalefula mtima, koma chinthu chochilakalaka chikachitikadi chimakhala ngati mtengo wamoyo.
13 Celui qui méprise la parole, périra à cause d'elle; mais celui qui craint le commandement, en aura la récompense.
Amene amanyoza malangizo adzawonongeka, koma amene amasamala lamulo amalandira mphotho.
14 L'enseignement du sage est une source de vie pour se détourner des filets de la mort.
Malangizo a munthu wanzeru ali ngati kasupe wamoyo; amathandiza munthu kuti asakondwe mu msampha wa imfa.
15 Le bon entendement donne de la grâce; mais la voie de ceux qui agissent perfidement, est raboteuse.
Munthu wa nzeru zabwino amapeza kuyanja pakati pa anthu, koma munthu wosakhulupirika adzawonongeka.
16 Tout homme bien avisé agira avec connaissance; mais le fou répandra sa folie.
Munthu wochenjera amachita zinthu mwanzeru, koma chitsiru chimaonetsa poyera uchitsiru wake.
17 Le méchant messager tombe dans le mal; mais l'ambassadeur fidèle est santé.
Wamthenga woyipa amagwetsa anthu mʼmavuto, koma nthumwi yodalirika imabweretsa mtendere.
18 La pauvreté et l'ignominie arriveront à celui qui rejette l'instruction; mais celui qui garde la répréhension, sera honoré.
Wokana mwambo adzasauka ndi kunyozedwa, koma wosamala chidzudzulo adzalemekezedwa.
19 Le souhait accompli est une chose douce à l'âme; mais se détourner du mal, est une abomination aux fous.
Chinthu chochilakalaka chikachitika chimasangalatsa mtima, koma zitsiru zimadana ndi kuleka zoyipa.
20 Celui qui converse avec les sages, deviendra sage; mais le compagnon des fous sera accablé.
Woyenda ndi anthu anzeru nayenso adzakhala wanzeru; koma woyenda ndi zitsiru adzapwetekeka.
21 Le mal poursuit les pécheurs; mais le bien sera rendu aux justes.
Choyipa chitsata mwini, koma wochita zolungama adzalandira mphotho yabwino.
22 L'homme de bien laissera de quoi hériter aux enfants de ses enfants; mais les richesses du pécheur sont réservées aux justes.
Munthu wabwino amasiyira zidzukulu zake cholowa, koma chuma cha munthu wochimwa amachilandira ndi olungama.
23 Il y a beaucoup à manger dans les terres défrichées des pauvres; mais il y a tel qui est consumé par faute de règle.
Tsala la munthu wosauka limalola chakudya chambiri, koma anthu opanda chilungamo amachilanda.
24 Celui qui épargne sa verge, hait son fils; mais celui qui l'aime, se hâte de le châtier.
Amene sakwapula mwana wake, ndiye kuti amamuda, koma wokonda mwana wake sazengereza kumulanga.
25 Le juste mangera jusqu'à être rassasié à son souhait; mais le ventre des méchants aura disette.
Munthu wolungama amakhala ndi zakudya zoti adye nʼkukhuta, koma mʼmimba mwa munthu woyipa mumakhala pululu ndi njala.

< Proverbes 13 >