< Proverbes 10 >

1 L'enfant sage réjouit son père, mais l'enfant insensé est l'ennui de sa mère.
Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.
2 Les trésors de méchanceté ne profiteront de rien; mais la justice garantira de la mort.
Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
3 L'Eternel n'affamera point l'âme du juste; mais la malice des méchants les pousse au loin.
Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala; koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.
4 La main paresseuse fait devenir pauvre; mais la main des diligents enrichit.
Wochita zinthu mwaulesi amasauka, koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.
5 L'enfant prudent amasse en été; [mais] celui qui dort durant la moisson, est un enfant qui fait honte.
Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru, koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.
6 Les bénédictions seront sur la tête du juste; mais la violence couvrira la bouche des méchants.
Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama, koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.
7 La mémoire du juste sera en bénédiction; mais la réputation des méchants sera flétrie.
Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso, koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.
8 Le sage de cœur recevra les commandements; mais le fou de lèvres tombera.
Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.
9 Celui qui marche dans l'intégrité, marche en assurance; mais celui qui pervertit ses voies, sera connu.
Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka; koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.
10 Celui qui fait signe de l'œil, donne de la peine; et le fou de lèvres sera renversé.
Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto, koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.
11 La bouche du juste est une source de vie; mais l'extorsion couvrira la bouche des méchants.
Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo, koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.
12 La haine excite les querelles; mais la charité couvre tous les forfaits.
Udani umawutsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.
13 La sagesse se trouve sur les lèvres de l'homme intelligent; mais la verge est pour le dos de celui qui est dépourvu de sens.
Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu, koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.
14 Les sages mettent en réserve la science; mais la bouche du fou [est] une ruine prochaine.
Anzeru amasunga chidziwitso koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.
15 Les biens du riche sont la ville de sa force; mais la pauvreté des misérables est leur ruine.
Chuma cha munthu wolemera ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.
16 L'œuvre du juste tend à la vie; mais le rapport du méchant tend au péché.
Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama, koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.
17 Celui qui garde l'instruction, tient le chemin qui tend à la vie; mais celui qui néglige la correction, se fourvoie.
Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo, koma wonyoza chidzudzulo amasochera.
18 Celui qui couvre la haine, use de fausses lèvres; et celui qui met en avant des choses diffamatoires, est fou.
Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama, ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.
19 La multitude des paroles n'est pas exempte de péché; mais celui qui retient ses lèvres, est prudent.
Mawu akachuluka zolakwa sizisowa, koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.
20 La langue du juste est un argent choisi; mais le cœur des méchants est bien peu de chose.
Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri, koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.
21 Les lèvres du juste en instruisent plusieurs; mais les fous mourront faute de sens.
Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri; koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.
22 La bénédiction de l'Eternel est celle qui enrichit, et [l'Eternel] n'y ajoute aucun travail.
Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma, ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.
23 C'est comme un jeu au fou de faire quelque méchanceté; mais la sagesse est de l'homme intelligent.
Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa, koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.
24 Ce que le méchant craint, lui arrivera; mais [Dieu] accordera aux justes ce qu'ils désirent.
Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira; chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.
25 Comme le tourbillon passe, ainsi le méchant n'est plus; mais le juste est un fondement perpétuel.
Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa, koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.
26 Ce qu'est le vinaigre aux dents, et la fumée aux yeux; tel est le paresseux à ceux qui l'envoient.
Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso, ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.
27 La crainte de l'Eternel accroît le nombre des jours; mais les ans des méchants seront retranchés.
Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo; koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.
28 L'espérance des justes n'est que joie; mais l'attente des méchants périra.
Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe, koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.
29 La voie de l'Eternel est la force de l'homme intègre; mais elle est la ruine des ouvriers d'iniquité.
Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino, koma wochita zoyipa adzawonongeka.
30 Le juste ne sera jamais ébranlé; mais les méchants n'habiteront point en la terre.
Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.
31 La bouche du juste produira la sagesse; mais la langue hypocrite sera retranchée.
Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru, koma lilime lokhota lidzadulidwa.
32 Les lèvres du juste connaissent ce qui est agréable; mais la bouche des méchants n'est que renversements.
Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula, koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.

< Proverbes 10 >