< Nombres 29 >

1 Et le premier jour du septième mois vous aurez une sainte convocation, vous ne ferez aucune œuvre servile; ce vous sera le jour de jubilation.
“‘Pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Ili ndi tsiku limene muziliza malipenga.
2 Et vous offrirez en holocauste de bonne odeur à l'Eternel, un veau pris du troupeau, un bélier, et sept agneaux d'un an sans tare.
Muzipereka mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi wopanda chilema monga nsembe zopsereza, fungo lokoma kwa Yehova.
3 Et leur gâteau sera de fine farine pétrie à l'huile, de trois dixièmes pour le veau, de deux dixièmes pour le bélier;
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzipereka chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa yayimuna iliyonse muzipereka makilogalamu awiri.
4 Et d'un dixième pour chacun des sept agneaux;
Pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja muzipereka kilogalamu imodzi.
5 Et un jeune bouc en offrande pour le péché, afin de faire propitiation pour vous.
Muziperekanso mbuzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
6 Outre l'holocauste du commencement du mois et son gâteau, et l'holocauste continuel et son gâteau, et leurs aspersions, selon leur ordonnance, en bonne odeur de sacrifice fait par feu à l'Eternel.
Izi ndi zowonjezera pa nsembe zopsereza za mwezi ndi mwezi komanso za tsiku ndi tsiku pamodzi ndi zopereka za chakudya ndi zopereka za chakumwa potsata malamulo ake. Izi ndi zopereka zotentha pa moto, zoperekedwa kwa Yehova, fungo lokoma.
7 Et au dixième jour de ce septième mois vous aurez une sainte convocation, et vous affligerez vos âmes; vous ne ferez aucune œuvre.
“‘Pa tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiriwu, muzichita msonkhano wopatulika. Muzisala zakudya ndipo musamagwire ntchito.
8 Et vous offrirez en holocauste de bonne odeur à l'Eternel, un veau pris du troupeau, un bélier, et sept agneaux d'un an, qui seront sans tare;
Muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza, yotulutsa fungo lokoma lokondweretsa Yehovayo; ngʼombe yayimuna imodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi. Zimenezi zizikhala zopanda chilema.
9 Et leur gâteau sera de fine farine pétrie à l'huile, de trois dixièmes pour le veau, et de deux dixièmes pour le bélier.
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri;
10 Et d'un dixième pour chacun des sept agneaux.
kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiriwo.
11 Un jeune bouc [aussi en offrande pour] le péché, outre [l'offrande pour] le péché, laquelle on fait le jour des propitiations, et l'holocauste continuel et son gâteau, avec leurs aspersions.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe yopepesera machimo ya pa tsiku la mwambo ija, kuwonjezanso pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija, pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi cha chakumwa.
12 Et au quinzième jour du septième mois vous aurez une sainte convocation, vous ne ferez aucune œuvre servile, et vous célébrerez à l'Eternel la fête solennelle, pendant sept jours.
“‘Pa tsiku la mwezi wachisanu ndi chiwiri, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Muzichita madyerero a Yehova masiku asanu ndi awiri.
13 Et vous offrirez en holocauste, qui sera un sacrifice fait par feu en bonne odeur à l'Eternel, treize veaux pris du troupeau, deux béliers, [et] quatorze agneaux d'un an, qui seront sans tare;
Muzipereka nsembe yotentha pa moto, kuti izikhala fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu, nkhosa zazimuna ziwiri, ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
14 Et leur gâteau sera de fine farine pétrie à l'huile, de trois dixièmes pour chacun des treize veaux, de deux dixièmes pour chacun des deux béliers,
Pa mwana wangʼombe aliyense mwa ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu aja, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa iliyonse mwa nkhosa ziwiri zija, mukonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri.
15 Et d'un dixième pour chacun des quatorze agneaux.
Pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa aamuna khumi ndi anayiwo, muzipereka chakudya cha kilogalamu imodzi.
16 Et un jeune bouc [en offrande pour] le péché, outre l'holocauste continuel, son gâteau, et son aspersion.
Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhale nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
17 Et au second jour vous offrirez douze veaux pris du troupeau, deux béliers, [et] quatorze agneaux d'un an, sans tare;
“‘Pa tsiku lachiwiri muzipereka ana angʼombe aamuna khumi ndi awiri aja, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi aja, zonse zopanda chilema.
18 Avec les gâteaux et les aspersions pour les veaux, pour les béliers, et pour les agneaux, selon leur nombre, [et] comme il les faut faire.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
19 Et un jeune bouc [en offrande pour] le péché, outre l'holocauste continuel, et son gâteau, avec leurs aspersions.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
20 Et au troisième jour vous offrirez onze veaux, deux béliers, [et] quatorze agneaux d'un an, sans tare;
“‘Pa tsiku lachitatu muzipereka ngʼombe zazimuna khumi ndi imodzi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
21 Et les gâteaux et les aspersions pour les veaux, pour les béliers et pour les agneaux, seront selon leur nombre, [et] comme il les faut faire.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
22 Et un bouc [en offrande pour] le péché, outre l'holocauste continuel, son gâteau, et son aspersion.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
23 Et au quatrième jour vous offrirez dix veaux, deux béliers, [et] quatorze agneaux d'un an, sans tare;
“‘Pa tsiku lachinayi muzipereka ngʼombe zazimuna khumi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
24 Les gâteaux et les aspersions pour les veaux, pour les béliers, et pour les agneaux, seront selon leur nombre, [et] comme il les faut faire.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
25 Et un jeune bouc [en offrande pour] le péché, outre l'holocauste continuel, son gâteau, et son aspersion.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
26 Et au cinquième jour vous offrirez neuf veaux, deux béliers, [et] quatorze agneaux d'un an, sans tare.
“‘Pa tsiku lachisanu muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zinayi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
27 Et les gâteaux et les aspersions pour les veaux, pour les béliers, et pour les agneaux, seront selon leur nombre, et comme il les faut faire.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
28 Et un bouc [en offrande pour le] péché, outre l'holocauste continuel, son gâteau, et son aspersion.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
29 Et au sixième jour vous offrirez huit veaux, deux béliers et quatorze agneaux d'un an, sans tare;
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zitatu, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
30 Et les gâteaux, et les aspersions pour les veaux, pour les béliers, et pour les agneaux seront selon leur nombre, [et] comme il les faut faire.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
31 Et un bouc [en offrande pour le] péché, outre l'holocauste continuel, son gâteau, et son aspersion.
Muziperekenso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
32 Et au septième jour vous offrirez sept veaux, deux béliers, [et] quatorze agneaux d'un an sans tare;
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa amuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
33 Et les gâteaux et les aspersions pour les veaux, pour les béliers, et pour les agneaux, seront selon leur nombre, [et] comme il les faut faire.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
34 Et un bouc [en offrande pour le] péché, outre l'holocauste continuel, son gâteau, et son aspersion.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
35 Et au huitième jour vous aurez une assemblée solennelle, vous ne ferez aucune œuvre servile.
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzichita msonkhano ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
36 Et vous offrirez en holocauste, qui sera un sacrifice fait par feu en bonne odeur à l'Eternel, un veau, un bélier, [et] sept agneaux d'un an sans tare;
Muzipereka chopereka chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ngʼombe imodzi yayimuna, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa amuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
37 Les gâteaux et les aspersions pour le veau, pour le bélier, et pour les agneaux, seront selon leur nombre, et comme il les faut faire;
Pamodzi ndi ngʼombe yayimunayo, nkhosa yayimunayo ndi ana ankhosawo, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
38 Et un bouc [en offrande pour le] péché, outre l'holocauste continuel, son gâteau, et son aspersion.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
39 Vous offrirez ces choses à l'Eternel dans vos fêtes solennelles, outre vos vœux, et vos offrandes volontaires, selon vos holocaustes, vos gâteaux, vos aspersions, et vos sacrifices de prospérités.
“‘Kuwonjezera pa zopereka zimene munalumbirira ndi pa zopereka zanu zaufulu, muzipereka zimenezi kwa Yehova pa masiku osankhika a chikondwerero chanu. Nsembe zanu zachakumwa ndi nsembe zanu zachiyanjano.’”
40 Et Moïse parla aux enfants d'Israël selon toutes les choses que l'Eternel lui avait commandées.
Mose anawuza Aisraeli zonse zimene Yehova anamulamulira.

< Nombres 29 >