< Nombres 10 >

1 Puis l'Eternel parla à Moïse, en disant:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Fais-toi deux trompettes d'argent, fais-les d'ouvrage battu au marteau; et elles te serviront pour convoquer l'assemblée, et pour faire partir les compagnies.
“Sula malipenga awiri a siliva, ndipo uziwagwiritsa ntchito posonkhanitsa anthu pamodzi ndiponso powasamutsa mʼmisasa.
3 Quand on en sonnera, toute l'assemblée s'assemblera vers toi à l'entrée du Tabernacle d'assignation.
Pamene akuliza malipenga onse awiri, anthu onse asonkhane kwa iwe pa khomo la tenti ya msonkhano.
4 Et quand on sonnera d'une seule, les principaux, qui sont les chefs des milliers d'Israël, s'assembleront vers toi.
Akaliza limodzi lokha, atsogoleri, akulu a mafuko a Aisraeli, asonkhane kwa iwe.
5 Mais quand vous sonnerez avec un retentissement bruyant, les compagnies qui sont campées vers l'Orient partiront.
Akaliza lipenga lochenjeza, misasa yomwe ili kummawa iyambe kusamuka.
6 Et quand vous sonnerez la seconde fois avec un retentissement bruyant, les compagnies qui sont campées vers le Midi partiront; on sonnera avec un retentissement bruyant, quand on voudra partir.
Akaliza lipenga lochenjeza lachiwiri, misasa yakummwera iyambe kusamuka. Kuliza kwa lipenga lochenjeza kudzakhala chizindikiro choyamba ulendo.
7 Et quand vous convoquerez l'assemblée, vous sonnerez, mais non point avec un retentissement bruyant.
Pofuna kusonkhanitsa anthu, muziliza malipenga, koma mosiyana ndi mmene malipenga ochenjeza amalizidwira.
8 Or les fils d'Aaron Sacrificateurs, sonneront des trompettes; et ceci vous sera une ordonnance perpétuelle en vos âges.
“Ana a Aaroni, ansembe aja, ndiwo aziliza malipengawo. Zimenezi zikhale zokhazikika kwa inu ndi ku mibado yanu yonse.
9 Et quand vous marcherez en bataille dans votre pays contre votre ennemi, venant vous attaquer; vous sonnerez des trompettes avec un retentissement bruyant, et l'Eternel votre Dieu se souviendra de vous, et vous serez délivrés de vos ennemis.
Pamene mukupita ku nkhondo mʼdziko lanu lomwe, kulimbana ndi mdani amene akukuzunzani, muziliza malipenga ochenjeza ndipo Yehova Mulungu wanu adzakukumbukirani ndi kukulanditsani mʼmanja mwa adani anu.
10 Aussi dans vos jours de joie, dans vos fêtes solennelles, et au commencement de vos mois, vous sonnerez des trompettes sur vos holocaustes, et sur vos sacrifices de prospérités, et elles vous serviront de mémorial devant votre Dieu; je [suis] l'Eternel, votre Dieu.
Komanso pa nthawi yanu ya chisangalalo, pa maphwando anu oyikika ndi maphwando a mwezi watsopano, muziliza malipenga pa nsembe zanu zopsereza ndi nsembe zanu za chiyanjano, ndipo zidzakhala chikumbutso chanu pamaso pa Mulungu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.”
11 Or il arriva le vingtième jour du second mois de la seconde année, que la nuée se leva de dessus le pavillon du Témoignage.
Pa chaka chachiwiri, mwezi wachiwiri, tsiku la 20, mtambo unachoka pamwamba pa chihema cha umboni.
12 Et les enfants d'Israël partirent selon leurs traittes, du désert de Sinaï, et la nuée se posa au désert de Paran.
Ndipo Aisraeli ananyamuka kuchoka mʼchipululu cha Sinai ndipo anayenda malo osiyanasiyana mpaka pamene mtambo unayima mʼchipululu cha Parani.
13 Ils partirent donc pour la première fois, suivant le commandement de l'Eternel, déclaré par Moïse.
Kameneka kanali koyamba kuti Aisraeli anyamuke monga momwe Yehova analamulira Mose.
14 Et la bannière des compagnies des enfants de Juda partit la première, selon leurs troupes; et Nahasson, fils de Hamminadab, conduisait la bande de Juda;
Magulu a msasa wa Yuda ndiwo anayamba kunyamuka potsata mbendera yawo. Mtsogoleri wa gulu lawo anali Naasoni mwana wa Aminadabu.
15 Et Nathanaël, fils de Tsuhar, conduisait la bande de la Tribu des enfants d'Issacar.
Mtsogoleri wa gulu la fuko la Isakara anali Netanieli mwana wa Zuwara,
16 Et Eliab, fils de Hélon, conduisait la bande de la Tribu des enfants de Zabulon.
Eliabu mwana wa Heloni ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Zebuloni.
17 Et le pavillon fut désassemblé; puis les enfants de Guerson, et les enfants de Mérari, qui portaient le pavillon, partirent.
Kenaka anagwetsa chihema, ndipo Ageresoni ndi Amerari amene ananyamula chihemacho, ananyamuka.
18 Puis la bannière des compagnies de Ruben partit, selon leurs troupes; et Elitsur, fils de Sédéur, conduisait la bande de Ruben.
Kenaka magulu a msasa wa fuko la Rubeni ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Elizuri mwana wa Sedeuri.
19 Et Sélumiel, fils de Tsurisaddaï, conduisait la bande de la Tribu des enfants de Siméon.
Mtsogoleri wa fuko la Simeoni anali Selumieli mwana wa Zurisadai,
20 Et Eliasaph, fils de Déhuël, conduisait la bande des enfants de Gad.
ndipo Eliyasafu mwana wa Deuweli ndiye ankatsogolera fuko la Gadi.
21 Alors les Kéhathites, qui portaient le Sanctuaire, partirent; cependant on dressait le Tabernacle, tandis que ceux-ci venaient.
Kenaka Akohati ananyamuka atanyamula zinthu zopatulika. Chihema chinkayenera kuyimikidwa iwo asanafike.
22 Puis la bannière des compagnies des enfants d'Ephraïm partit, selon leurs troupes; et Elisamah, fils de Hammihud, conduisait la bande d'Ephraïm.
Magulu a msasa wa Aefereimu anatsatira potsatira mbendera yawo. Elisama mwana wa Amihudi ndiye anali mtsogoleri wawo.
23 Et Gamaliel, fils de Pédatsur, conduisait la bande de la Tribu des enfants de Manassé.
Gamalieli mwana wa Pedazuri ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Manase.
24 Et Abidan, fils de Guidhoni, conduisait la bande de la Tribu des enfants de Benjamin.
Abidani mwana wa Gideoni ndiye anali mtsogoleri wa mtundu wa Benjamini.
25 Enfin la bannière des compagnies des enfants de Dan, qui faisait l'arrière-garde, partit, selon leurs troupes; et Ahihézer, fils de Hammisaddaï, conduisait la bande de Dan.
Pambuyo pa magulu onse panali magulu a msasa wa Dani, omwe ankateteza magulu onsewa ndipo ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
26 Et Paghiel, fils de Hocran, conduisait la bande de la Tribu des enfants d'Aser.
Pagieli mwana wa Okirani ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Aseri,
27 Et Ahirah, fils de Hénan, conduisait la bande de la Tribu des enfants de Nephthali.
ndipo mtsogoleri wa mtundu wa Nafutali anali Ahira mwana wa Enani.
28 Tels étaient les décampements des enfants d'Israël selon leurs troupes, quand ils partaient.
Umenewu ndiwo unali mndandanda wa kayendedwe ka magulu a Aisraeli pamene ankanyamuka ulendo wawo mʼmagulumagulu.
29 Or Moïse dit à Hobab, fils de Réhuel Madianite, son beau-père: Nous allons au lieu duquel l'Eternel a dit, je vous le donnerai. Viens avec nous, et nous te ferons du bien; car l'Eternel a promis de faire du bien à Israël.
Ndipo Mose anawuza Hobabu mwana wa Reueli Mmidiyani, mpongozi wa Mose kuti, “Tikunyamuka kupita ku malo amene Yehova anati, ‘Ndidzakupatsani.’ Tiye upite nafe ndipo tidzakusamalira bwino, pakuti Yehova analonjeza zinthu zabwino kwa Israeli.”
30 Et Hobab lui répondit: Je n'y irai point, mais je m'en irai en mon pays, et vers ma parenté.
Hobabu anayankha kuti, “Ayi, sindipita nanu, ndibwerera ku dziko la kwathu ndi kwa abale anga.”
31 Et Moïse lui dit: Je te prie, ne nous quitte point; car tu nous serviras de guide, parce que tu connais les lieux où nous aurons à camper dans le désert.
Ndipo Mose anati, “Pepa usatisiye popeza ukudziwa kumene tingamange misasa mʼchipululu muno ndipo udzakhala maso athu.
32 Et il arrivera que quand tu seras venu avec nous, et que le bien que l'Eternel nous doit faire sera arrivé, nous te ferons aussi du bien.
Iweyo ukapita nafe, tidzagawana nawe zinthu zabwino zomwe Yehova adzatipatsa.”
33 Ainsi ils partirent de la montagne de l'Eternel, [et ils marchèrent] le chemin de trois jours; et l'Arche de l'alliance de l'Eternel alla devant eux pendant le chemin de trois jours pour chercher un lieu où ils se reposassent.
Motero ananyamuka ku Phiri la Yehova nayenda ulendo wa masiku atatu. Bokosi la Chipangano cha Yehova linkayenda patsogolo pawo pa masiku atatuwo kuti apeze malo woti apumulepo.
34 Et la nuée de l'Eternel était sur eux le jour, quand ils partaient du lieu où ils avaient campé.
Mtambo wa Yehova unkawaphimba masana pamene ankasamuka pa misasa yawo.
35 Or il arrivait qu'au départ de l'Arche, Moïse disait: Lève-toi, ô Eternel, et tes ennemis seront dispersés, et ceux qui te haïssent s'enfuiront de devant toi.
Nthawi iliyonse imene Bokosi la Chipangano likunyamuka, Mose ankanena kuti, “Dzukani, Inu Yehova! Adani anu abalalike; Odana nanu athawe pamaso panu.
36 Et quand on la posait, il disait: Retourne, ô Eternel, aux dix mille milliers d'Israël.
“Pamene likupumula, ankanena kuti, “Bwererani, Inu Yehova, ku chinamtindi cha Aisraeli.”

< Nombres 10 >