< Nahum 2 >

1 Le destructeur est monté contre toi; garde la forteresse, prends garde aux avenues, fortifie tes reins, ramasse toutes tes forces.
Wodzathira nkhondo akubwera kudzalimbana nawe, Ninive. Tetezani malinga anu, dziyangʼanani ku msewu, konzekerani nkhondo, valani dzilimbe.
2 Car l'Eternel a abaissé la fierté de Jacob comme la fierté d'Israël; parce que les videurs les ont vidés, et qu'ils ont ravagé leurs sarments.
Yehova adzabwezeretsa ulemerero wa Yakobo ngati ulemerero wa Israeli, ngakhale anthu owononga anawawononga kotheratu ndipo anawononganso mpesa wawo.
3 Le bouclier de ses hommes forts est rendu rouge; ses hommes vaillants sont teints de vermillon; les chariots [marcheront] avec un feu de torches, au jour qu'il aura rangé [ses batailles], et que les sapins branleront.
Zishango za ankhondo ake ndi zofiira; asilikali ake avala zovala zofiirira. Zitsulo za pa magaleta zikunyezimira tsiku la kukonzekera kwake. Akuonetsa mikondo ya mkungudza yonoledwa.
4 Les chariots couront avec rapidité dans les rues, et s'entre-heurteront dans les places, ils seront, à les voir comme des flambeaux, et courront comme des éclairs.
Magaleta akuthamanga mʼmisewu akungothamangathamanga pa mabwalo. Akuoneka ngati miyuni yoyaka; akuthamanga ngati chingʼaningʼani.
5 Il se souviendra de ses hommes vaillants, mais ils seront renversés en chemin; ils se hâteront [de venir] à ses murailles, et la contre-défense sera toute prête.
Iye akuyitanitsa asilikali ake wolemekezeka, koma iwo akubwera napunthwa. Akuthamangira ku linga la mzinda; akuyimika chodzitchinjirizira pamalo pake.
6 Les portes des fleuves sont ouvertes, et le palais s'est fondu.
Atsekula zipata zotchinga madzi a mu mtsinje ndipo nyumba yaufumu yagwa.
7 On y a fait tenir [chacun] debout, [la Reine] a été emmenée prisonnière, on l'a fait monter, et ses servantes l'ont accompagnée, comme avec une voix de colombe, frappant leurs poitrines comme un tambour.
Zatsimikizika kuti mzinda utengedwa ndi kupita ku ukapolo. Akapolo aakazi akulira ngati nkhunda ndipo akudziguguda pachifuwa.
8 Or Ninive, depuis qu'elle a été bâtie, a été comme un vivier d'eaux; mais ils s'enfuient; arrêtez-vous, arrêtez-vous; mais il n'y a personne qui tourne visage.
Ninive ali ngati dziwe, ndipo madzi ake akutayika. Iwo akufuwula kuti, “Imani! Imani!” Koma palibe amene akubwerera.
9 Pillez l'argent, pillez l'or; il y a de bornes à son fane, qui l'emporte sur tous les vaisseaux précieux.
Funkhani siliva! Funkhani golide! Katundu wake ndi wochuluka kwambiri, chuma chochokera pa zinthu zake zamtengowapatali!
10 [Qu'elle soit] toute vidée et revidée, même tout épuisée; que leur cœur se fonde, que leurs genoux se heurtent l'un contre l'autre; que le tourment soit dans les reins de tous, et que leurs visages deviennent noirs comme un pot [qui a été mis sur le feu.]
Iye wawonongedwa, wafunkhidwa ndipo wavulidwa! Mitima yasweka, mawondo akuwombana, anthu akunjenjemera ndipo nkhope zasandulika ndi mantha.
11 Où [est] le repaire des lions, et le viandis des lionceaux, dans lequel se retiraient les lions, et où [se tenaient] les vieux lions, et les faons des lions, sans qu'aucun les effarouchât?
Kodi tsopano dzenje la mikango lili kuti, malo amene mikango inkadyetserako ana ake, kumene mkango waumuna ndi waukazi unkapitako, ndipo ana a mkango sankaopa kanthu kalikonse?
12 Les lions ravissaient tout ce qu'il fallait pour leurs faons, et étranglaient [les bêtes] pour leurs vielles lionnes, et ils remplissaient leurs tanières de proie, et leurs repaires de rapine.
Mkango waumuna unkapha nyama yokwanira ana ake ndiponso kuphera nyama mkango waukazi, kudzaza phanga lake ndi zimene wapha ndiponso dzenje lake ndi nyama imene waphayo.
13 Voici, j'en veux à toi, dit l'Eternel des armées, et je brûlerai tes chariots, [et ils s'en iront] en fumée, et l'épée consumera tes lionceaux; je retrancherai de la terre ta proie, et la voix de tes ambassadeurs ne sera plus entendue.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikutsutsana nawe. Ndidzatentha magaleta ako mpaka utsi tolotolo, ndipo lupanga lidzapha mikango yako yayingʼono; sindidzakusiyira chilichonse choti udye pa dziko lapansi. Mawu a amithenga anu sadzamvekanso.”

< Nahum 2 >