< Michée 1 >

1 La parole de l'Eternel qui fut [adressée] à Michée Morasite au temps de Jotham, Achaz, et Ezéchias, Rois de Juda, laquelle lui [fut adressée] dans une vision, contre Samarie et Jérusalem.
Yehova anayankhula ndi Mika wa ku Moreseti pa nthawi ya ulamuliro wa Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda. Awa ndi masomphenya amene iye anaona onena za Samariya ndi Yerusalemu.
2 Vous tous peuples, écoutez; et toi terre, sois attentive, et que tout ce qui est en elle [écoute]; et que le Seigneur l'Eternel soit témoin contre vous, le Seigneur, [dis-je, sortant] du palais de sa sainteté.
Tamverani, inu anthu a mitundu yonse, mvetsera iwe dziko lapansi ndi okhala mʼmenemo, pakuti Ambuye Yehova achitira umboni wokutsutsani, Ambuye akuyankhula ali mʼnyumba yake yopatulika.
3 Car voici, l'Eternel s'en va sortir de son lieu, il descendra, et marchera sur les lieux hauts de la terre;
Taonani! Yehova akubwera kuchokera ku malo ake; Iye akutsika ndipo akuponda pa malo okwera a dziko lapansi.
4 Et les montagnes se fondront sous lui, et les vallées se fendront, elles seront comme de la cire devant le feu, et comme des eaux qui coulent en une descente.
Mapiri akusungunuka pansi pake, ndipo zigwa zikugawikana ngati phula pa moto, ngati madzi ochokera mʼphiri.
5 Tout ceci arrivera à cause du crime de Jacob, et à cause des péchés de la maison d'Israël. [Or] quel est le crime de Jacob? N'est-ce pas Samarie? Et quels sont les hauts lieux de Juda? N'est-ce pas Jérusalem?
Zonsezi ndi chifukwa cha cholakwa cha Yakobo, chifukwa cha machimo a nyumba ya Israeli. Kodi cholakwa cha Yakobo nʼchiyani? Kodi si Samariya? Kodi malo achipembedzo a Yuda ndi ati? Kodi si Yerusalemu?
6 C'est pourquoi je réduirai Samarie [comme] en un monceau de pierres [ramassées] dans les champs [où l'on veut planter des vignes]; et je ferai rouler ses pierres dans la vallée, et je découvrirai ses fondements.
“Choncho Ine ndidzasandutsa Samariya kukhala bwinja, malo odzalamo mphesa. Miyala yake ndidzayitaya ku chigwa ndipo ndidzafukula maziko ake.
7 Et toutes ses images taillées seront brisées, tous les salaires de sa prostitution seront brûlés au feu, et je mettrai tous ses faux dieux en désolation; parce qu'elle les a entassés par le moyen du salaire de sa prostitution, ils serviront de salaire à une prostituée.
Mafano ake onse ndidzawaphwanyaphwanya; mphatso zake zonse ndidzazitentha ndi moto; ndidzawononga zifanizo zonse za milungu yake. Popeza analandira mphatso zake kuchokera ku malipiro a akazi achiwerewere, mphatsozonso zidzagwiritsidwa ntchito ndi ena ngati malipiro a akazi achiwerewere.”
8 C'est pourquoi je me plaindrai, et je hurlerai; je m'en irai dépouillé et nu; je ferai une lamentation comme celle des dragons, et je mènerai un deuil comme celui des chats-huants.
Chifukwa cha zimenezi ine ndidzalira momvetsa chisoni; ndidzayenda wopanda nsapato ndi wamaliseche. Ndidzafuwula ngati nkhandwe ndi kulira ngati kadzidzi.
9 Car il n'y a pas une de ses plaies qui ne soit incurable, chacune d'elles est venue jusqu'en Juda, et [l'ennemi] est parvenu jusqu'à la porte de mon peuple, jusqu'à Jérusalem.
Pakuti chilonda cha Samariya nʼchosachizika; chafika ku Yuda. Chafika pa chipata chenicheni cha anthu anga, mpaka mu Yerusalemu mwenimwenimo.
10 Ne l'annoncez point dans Gath, ne pleurez nullement; vautre-toi sur la poussière dans la maison d'Haphra.
Musanene zimenezi ku Gati; musalire nʼkomwe. Mugubuduzike mu fumbi ku Beti-Leafura.
11 Habitante de Saphir passe, ayant ta nudité toute découverte; l'habitante de Tsaanan n'est point sortie pour la complainte de la maison d'Esel; on apprendra de vous à se tenir dans la maison.
Inu anthu okhala ku Safiro, muzipita ku ukapolo muli amaliseche ndi amanyazi. Iwo amene akukhala ku Zanaani sadzatuluka. Beti-Ezeli akulira mwachisoni; chitetezo chake chakuchokerani.
12 Car l'habitante de Maroth aura été dans l'angoisse pour [son] bien; parce que le mal est descendu de par l'Eternel sur la porte de Jérusalem.
Anthu amene amakhala ku Maroti akubuwula ndi ululu, akuyembekezera thandizo, chifukwa Yehova wabweretsa tsoka, lafika mpaka pa chipata cha Yerusalemu.
13 Attelle le cheval au chariot, habitante de Lakis, [toi qui] es le commencement du péché de la fille de Sion; car en toi ont été trouvés les crimes d'Israël.
Inu anthu okhala ku Lakisi mangani akavalo ku magaleta. Inu amene munayamba kuchimwitsa mwana wamkazi wa Ziyoni, pakuti zolakwa za Israeli zinapezeka pakati panu.
14 C'est pourquoi donne des présents à cause de Moreseth de Gath; les maisons d'Aczib mentiront aux Rois d'Israël.
Chifukwa chake perekani mphatso zolawirana ndi a ku Moreseti Gati. Mzinda wa Akizibu udzaonetsa kunama kwa mafumu a Israeli.
15 Je te ferai aussi venir un héritier, habitante de Maresa; et la gloire d'Israël viendra jusqu'à Hadullam.
Ndidzabweretsa mgonjetsi kudzalimbana ndi inu okhala mu Maresa. Ulemerero wa Israeli udzafika ku Adulamu.
16 Arrache tes cheveux, et te fais tondre à cause de tes fils qui font tes délices; arrache tout le poil de ton corps comme un aigle [qui mue], car ils sont emmenés prisonniers [loin] de toi.
Metani mipala mitu yanu kuonetsa kuti mukulirira ana anu amene mumawakonda; mudzichititse dazi ngati dembo, pakuti anawo adzatengedwa pakati panu kupita ku ukapolo.

< Michée 1 >