< Matthieu 5 >

1 Or [Jésus] voyant tout ce peuple, monta sur une montagne; puis s'étant assis, ses Disciples s'approchèrent de lui;
Iye ataona anthu ambiri, anakwera pa phiri nakhala pansi. Ndipo ophunzira ake anabwera kwa Iye,
2 Et ayant commencé à parler, il les enseignait, de la sorte;
ndipo anayamba kuwaphunzitsa kuti,
3 Bienheureux sont les pauvres en esprit; car le Royaume des cieux est à eux.
“Odala ndi amene ali osauka mu mzimu, chifukwa ufumu wakumwamba ndi wawo.
4 Bienheureux sont ceux qui pleurent; car ils seront consolés.
Odala ndi amene ali achisoni, chifukwa adzatonthozedwa.
5 Bienheureux sont les débonnaires; car ils hériteront la terre.
Odala ndi amene ali ofatsa, chifukwa adzalandira dziko lapansi.
6 Bienheureux sont ceux qui sont affamés et altérés de la justice; car ils seront rassasiés.
Odala ndi amene akumva njala ndi ludzu la chilungamo, chifukwa adzakhutitsidwa.
7 Bienheureux sont les miséricordieux; car la miséricorde leur sera faite.
Odala ndi amene ali ndi chifundo, chifukwa adzawachitira chifundo.
8 Bienheureux sont ceux qui sont nets de cœur; car ils verront Dieu.
Odala ndi amene ali oyera mtima, chifukwa adzaona Mulungu.
9 Bienheureux sont ceux qui procurent la paix; car ils seront appelés enfants de Dieu.
Ndi odala amene amabweretsa mtendere, chifukwa adzatchedwa ana a Mulungu.
10 Bienheureux sont ceux qui sont persécutés pour la justice; car le Royaume des cieux est à eux.
Odala ndi amene akuzunzidwa chifukwa cha chilungamo, pakuti ufumu wakumwamba ndi wawo.”
11 Vous serez bienheureux quand on vous aura injuriés et persécutés, et quand, à cause de moi, on aura dit faussement contre vous toute sorte de mal.
“Inu ndinu odala anthu akamakunyozani, kukuzunzani, kukunenerani zoyipa zilizonse ndi kukunamizirani chifukwa cha Ine.
12 Réjouissez-vous, et tressaillez de joie; parce que votre récompense est grande dans les cieux; car on a ainsi persécuté les Prophètes qui ont été avant vous.
Sangalalani, kondwerani chifukwa mphotho yanu ndi yayikulu kumwamba, chifukwa moterenso ndi mmene anazunzira aneneri inu musanabadwe.
13 Vous êtes le sel de la terre; mais si le sel perd sa saveur, avec quoi le salera-t-on? il ne vaut plus rien qu'à être jeté dehors, et foulé des hommes.
“Inu ndinu mchere wa dziko lapansi. Koma ngati mcherewo usukuluka, adzawukometsanso ndi chiyani? Ulibenso ntchito koma kungowutaya kunja, anthu nawuponda.
14 Vous êtes la lumière du monde; une ville située sur une montagne ne peut point être cachée.
“Inu ndinu kuwunika kwa dziko lapansi. Mzinda wa pa phiri sungathe kubisika.
15 Et on n'allume point la lampe pour la mettre sous un boisseau, mais sur un chandelier, et elle éclaire tous ceux qui sont dans la maison.
Anthu sayatsa nyale ndikuyivundikira ndi mbiya, mʼmalo mwake amayika poonekera ndipo imawunikira onse mʼnyumbamo.
16 Ainsi, que votre lumière luise devant les hommes, afin qu'ils voient vos bonnes œuvres, et qu'ils glorifient votre Père qui est aux cieux.
Momwemonso kuwunika kwanu kuwale pamaso pa anthu kuti aone ntchito zanu zabwino ndi kulemekeza Atate anu akumwamba.
17 Ne croyez pas que je sois venu anéantir la Loi, ou les Prophètes; je ne suis pas venu les anéantir, mais les accomplir.
“Musaganize kuti ndinadza kudzathetsa malamulo kapena zonena za aneneri; sindinabwere kudzathetsa koma kukwaniritsa.
18 Car je vous dis en vérité, que jusqu'à ce que le ciel et la terre soient passés, un seul Iota, ou un seul trait de lettre ne passera point, que toutes choses ne soient faites.
Ine ndikukuwuzani zoonadi kuti, kufikira kutha kwa thambo ndi dziko lapansi, chilichonse chimene chinalembedwa mʼmalamulo, ngakhale kalemba kakangʼonongʼono, chidzakwaniritsidwa.
19 Celui donc qui aura violé l'un de ces petits commandements, et qui aura enseigné ainsi les hommes, sera tenu le plus petit au Royaume des cieux; mais celui qui les aura faits et enseignés, sera tenu grand au Royaume des cieux.
Chifukwa chake aliyense amene aphwanya limodzi la malamulowa ngakhale lalingʼonongʼono ndi kuphunzitsa ena kuti achite chimodzimodzi, adzakhala wotsirizira mu ufumu wakumwamba, koma aliyense amene achita ndi kuphunzitsa malamulo awa adzakhala wamkulu mu ufumu wakumwamba.
20 Car je vous dis que si votre justice ne surpasse celle des Scribes et des Pharisiens, vous n'entrerez point dans le Royaume des cieux.
Chifukwa chake ndikuwuzani kuti ngati chilungamo chanu sichiposa cha Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo, zoonadi, simudzalowa mu ufumu wakumwamba.
21 Vous avez entendu qu'il a été dit aux Anciens: Tu ne tueras point; et qui tuera, sera punissable par le jugement.
“Munamva kuti kunanenedwa kwa anthu kale kuti, ‘Usaphe ndipo kuti aliyense amene apha munthu adzaweruzidwa.’
22 Mais moi je vous dis: que quiconque se met en colère sans cause contre son frère, sera punissable par le jugement; et celui qui dira à son frère, Racha, sera punissable par le conseil; et celui qui lui dira, fou, sera punissable par la géhenne du feu. (Geenna g1067)
Koma Ine ndikukuwuzani kuti aliyense wokwiyira mʼbale wake adzapezeka wolakwa ku bwalo la milandu. Ndiponso aliyense amene wonena mʼbale wake kuti, ‘Ndiwe wopanda phindu,’ adzapezeka wolakwa ku bwalo la milandu lalikulu. Ndipo aliyense amene anganene mnzake ‘wopandapake’ adzatengeredwa ku bwalo la milandu. Ndiponso aliyense amene angamunene mnzake kuti, ‘Chitsiru iwe,’ adzaponyedwa ku gehena. (Geenna g1067)
23 Si donc tu apportes ton offrande à l'autel, et que là il te souvienne que ton frère a quelque chose contre toi;
“Nʼchifukwa chake, pamene ukupereka chopereka chako pa guwa lansembe ndipo nthawi yomweyo ukumbukira kuti mʼbale wako ali nawe chifukwa,
24 Laisse-là ton offrande devant l'autel, et va te réconcilier premièrement avec ton frère, puis viens, et offre ton offrande.
usiye choperekacho pa guwa lansembepo, choyamba pita kayanjane ndi mʼbale wako; ukatero bwera kudzapereka chopereka chakocho.
25 Sois bientôt d'accord avec ta partie adverse, tandis que tu es en chemin avec elle; de peur que ta partie adverse ne te livre au juge, et que le juge ne te livre au sergent, et que tu ne sois mis en prison.
“Fulumira kuyanjana ndi mnzako amene unamulakwira nthawi ya milandu isanafike chifukwa angakupereke kwa oweruza amene angakupereke kwa mlonda ndipo mlondayo angakutsekere mʼndende.
26 En vérité, je te dis, que tu ne sortiras point de là, jusqu'à ce que tu aies payé le dernier quadrin.
Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti sudzatuluka mʼndende mpaka utalipira zonse.
27 Vous avez entendu qu'il a été dit aux Anciens: Tu ne commettras point adultère.
“Munamva kuti kunanenedwa kuti, ‘Usachite chigololo.’
28 Mais moi je vous dis, que quiconque regarde une femme pour la convoiter, il a déjà commis dans son cœur un adultère avec elle.
Koma Ine ndikuwuzani kuti aliyense woyangʼana mkazi momusirira wachita naye kale chigololo mu mtima mwake.
29 Que si ton œil droit te fait broncher, arrache-le, et le jette loin de toi; car il vaut mieux qu'un de tes membres périsse, que si tout ton corps était jeté dans la géhenne. (Geenna g1067)
Ngati diso lako lakumanja likuchimwitsa, ulichotse ndi kulitaya. Pakuti nʼkwabwino kwa iwe kutaya chiwalo chimodzi cha thupi lako, kusiyana ndi kuti thupi lonse liponyedwe mʼgehena. (Geenna g1067)
30 Et si ta main droite te fait broncher, coupe-la, et la jette loin de toi; car il vaut mieux qu'un de tes membres périsse, que si tout ton corps était jeté dans la géhenne. (Geenna g1067)
Ndipo ngati dzanja lako lamanja likuchimwitsa, ulidule ndi kulitaya. Pakuti nʼkwabwino kwa iwe kutaya chiwalo chimodzi cha thupi lako, kusiyana ndi kuti thupi lonse liponyedwe mʼgehena. (Geenna g1067)
31 Il a été dit encore: si quelqu'un répudie sa femme, qu'il lui donne la Lettre de divorce.
“Ananena kuti, ‘Aliyense wosudzula mkazi wake ayenera amupatse kalata ya chisudzulo.’
32 Mais moi je vous dis, que quiconque aura répudié sa femme, si ce n'est pour cause d'adultère, il la fait devenir adultère; et quiconque se mariera à la femme répudiée, commet un adultère.
Koma Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene asudzula mkazi wake pa chifukwa china chilichonse osati chifukwa cha chiwerewere, akumuchititsa mkaziyo chigololo ndipo aliyense wokwatira mkaziyo, akuchitanso chigololo.
33 Vous avez aussi appris qu'il a été dit aux Anciens: tu ne te parjureras point, mais tu rendras au Seigneur ce que tu auras promis par jurement.
“Munamvanso kuti kunanenedwa kwa anthu akale kuti, ‘Musaphwanye lonjezo; koma sungani malonjezo anu amene mwachita kwa Yehova.’
34 Mais moi, je vous dis: ne jurez en aucune manière; ni par le ciel, car c'est le trône de Dieu;
Koma ndikuwuzani kuti musalumbire ndi pangʼono pomwe kutchula kumwamba chifukwa kuli mpando waufumu wa Mulungu.
35 Ni par la terre, car c'est le marchepied de ses pieds; ni par Jérusalem, parce que c'est la ville du grand Roi.
Kapena kutchula dziko lapansi, chifukwa ndi chopondapo mapazi ake; kapena kutchula Yerusalemu, chifukwa ndi mzinda wa mfumu yayikulu.
36 Tu ne jureras point non plus par ta tête; car tu ne peux faire un cheveu blanc ou noir.
Ndipo musalumbire ndi mutu wanu chifukwa simungathe kuyeretsa ngakhale kudetsa tsitsi limodzi.
37 Mais que votre parole soit: oui, oui; non, non; car ce qui est de plus, est mauvais.
Koma ‘Inde’ wanu akhaledi ‘Inde’ kapena ‘Ayi’ wanu akhaledi ‘Ayi,’ chilichonse choposera apa, chichokera kwa woyipayo.
38 Vous avez appris qu'il a été dit: œil pour œil, et dent pour dent.
“Munamva kuti, ‘Diso kulipira diso ndi dzino kulipira dzino.’
39 Mais moi, je vous dis: ne résistez point au mal; mais si quelqu'un te frappe à ta joue droite, présente-lui aussi l'autre.
Koma ndikuwuzani kuti musamukanize munthu woyipa, akakumenya patsaya mupatseni tsaya linalo.
40 Et si quelqu'un veut plaider contre toi, et t'ôter ta robe, laisse-lui encore le manteau.
Ndipo ngati wina afuna kukuzenga mlandu kuti akulande malaya ako, umupatsenso mkanjo wako.
41 Et si quelqu'un te veut contraindre d'aller avec lui une lieue, vas-en deux.
Ngati wina akukakamiza kuti uyende naye mtunda umodzi, iwe uyende naye mitunda iwiri.
42 Donne à celui qui te demande, et ne te détourne point de celui qui veut emprunter de toi.
Wina akakupempha kanthu umupatse, ndipo wofuna kubwereka usamukanize.
43 Vous avez appris qu'il a été dit: tu aimeras ton prochain, et tu haïras ton ennemi.
“Munamva kuti, ‘Konda mnansi wako ndi kudana ndi mdani wako.’
44 Mais moi je vous dis: aimez vos ennemis, et bénissez ceux qui vous maudissent, faites du bien à ceux qui vous haïssent, et priez pour ceux qui vous courent sus, et vous persécutent.
Koma Ine ndikuwuzani kuti, ‘Kondani adani anu ndi kuwapempherera okuzunzani
45 Afin que vous soyez les enfants de votre Père qui est aux cieux; car il fait lever son soleil sur les méchants, et sur les gens de bien, et il envoie sa pluie sur les justes, et sur les injustes.
kuti mukhale ana a Atate anu akumwamba, amene awalitsa dzuwa lake pa oyipa ndi pa abwino, nagwetsa mvula pa olungama ndi pa osalungama.’
46 Car si vous aimez [seulement] ceux qui vous aiment, quelle récompense en aurez-vous? Les péagers mêmes n'en font-ils pas tout autant?
Ngati mukonda amene akukondani inu, mudzapeza mphotho yanji? Kodi ngakhale amisonkho sachita chimodzimodzi?
47 Et si vous faites accueil seulement à vos frères, que faites-vous plus [que les autres]? les péagers mêmes ne le font-ils pas aussi?
Ndipo ngati inu mupatsa moni abale anu okhaokha mukuchita chiyani choposa ena? Kodi ngakhale akunja sachita chimodzimodzi?
48 Soyez donc parfaits, comme votre Père qui est aux cieux est parfait.
Nʼchifukwa chake, inu khalani angwiro monga Atate anu akumwamba ali wangwiro.”

< Matthieu 5 >