< Matthieu 20 >

1 Car le Royaume des cieux est semblable à un père de famille, qui sortit dès le point du jour afin de louer des ouvriers pour sa vigne.
“Ufumu wakumwamba uli ngati mwini munda amene anapita mmawa kukalemba anthu aganyu kuti akagwire ntchito mʼmunda wake wa mpesa.
2 Et quand il eut accordé avec les ouvriers à un denier par jour, il les envoya à sa vigne.
Anagwirizana kuwalipira dinari monga malipiro a tsiku limodzi ndipo anawatumiza mʼmunda wake wamphesa.
3 Puis étant sorti sur les trois heures, il en vit d'autres qui étaient au marché, sans rien faire;
“Nthawi 9 koloko mmawa, anatulukanso naona ena atayimirira pa msika akungokhala.
4 Auxquels il dit: allez-vous-en aussi à ma vigne, et je vous donnerai ce qui sera raisonnable.
Anawawuza kuti, ‘Inunso pitani mukagwire ntchito mʼmunda wanga wa mpesa, ndipo ndidzakulipirani malipiro oyenera.’
5 Et ils y allèrent. Puis il sortit encore environ sur les six heures, et sur les neuf heures, et il en fit de même.
Ndipo anapita. “Anatulukanso nthawi ya 12 koloko masana, ndi nthawi ya 3 koloko masananso nachita chimodzimodzi.
6 Et étant sorti sur les onze heures, il en trouva d'autres qui étaient sans rien faire, auxquels il dit: pourquoi vous tenez-vous ici tout le jour sans rien faire?
Nthawi ya 5 koloko madzulo anatulukanso ndipo anapeza enanso atangoyimirira. Anawafunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani mukungoyimirira pano tsiku lonse osagwira ntchito?’
7 Ils lui répondirent: parce que personne ne nous a loués. Et il leur dit: allez-vous-en aussi à ma vigne, et vous recevrez ce qui sera raisonnable.
“Iwo anayankha kuti, ‘Chifukwa palibe munthu amene watilemba ganyu.’ “Iye anawawuza kuti, ‘Inunso pitani mukagwire ntchito mʼmunda wanga wa mpesa.’
8 Et le soir étant venu, le maître de la vigne dit à celui qui avait la charge de ses affaires: appelle les ouvriers, et leur paye leur salaire, en commençant depuis les derniers jusques aux premiers.
“Ndipo pofika madzulo, mwini munda wamphesa anayitana kapitawo wake nati, ‘Itana antchito ndipo uwapatse malipiro awo, kuyambira omalizira aja mpaka oyamba.’
9 Alors ceux qui avaient été loués vers les onze heures étant venus, ils reçurent chacun un denier.
“Antchito amene anawalemba ganyu pa 5 koloko masana anafika ndipo aliyense analandira dinari.
10 Or quand les premiers furent venus ils croyaient recevoir davantage, mais ils reçurent aussi chacun un denier.
Ndipo atabwera kwa amene analembedwa poyamba anayembekezera kuti alandira zambiri. Koma aliyense wa iwo analandira dinari.
11 Et l'ayant reçu, ils murmuraient contre le père de famille,
Atalandira, anayamba kuderera kwa mwini mundayo.
12 En disant: ces derniers n'ont travaillé qu'une heure, et tu les as faits égaux à nous, qui avons porté le faix du jour, et la chaleur.
Iwo anati, ‘Anthu amene munawalemba pomalizira agwira ntchito ora limodzi, ndipo mwawafananitsa ndi ife amene tathyoka nayo ntchito ndi kutentha kwa dzuwa tsiku lonse.’
13 Et il répondit à l'un d'eux, et lui dit: mon ami, je ne te fais point de tort, n'as-tu pas accordé avec moi à un denier?
“Koma iye anamuyankha mmodzi wa iwo nati, ‘Bwenzi, ine sikuti sindinachite chilungamo. Kodi sunavomereze kuti ugwira ntchito ndi kulandira dinari?
14 Prends ce qui est à toi, et t'en va; mais si je veux donner à ce dernier autant qu'à toi,
Tenga malipiro ako pita. Ndikufuna kumupatsa munthu amene ndinamulemba pomaliza mofanana ndi mmene ndakupatsira iwe.
15 Ne m'est-il pas permis de faire ce que je veux de mes biens? ton œil est-il malin de ce que je suis bon?
Kodi ndilibe ufulu wochita zimene ndikufuna ndi ndalama zanga? Kapena ukuyipidwa chifukwa ndine wopereka mowolowamanja?’
16 Ainsi les derniers seront les premiers, et les premiers seront les derniers, car il y a beaucoup d'appelés, mais peu d'élus.
“Momwemo omalizira adzakhala oyamba ndipo oyamba adzakhala omalizira.”
17 Et Jésus montant à Jérusalem, prit à part sur le chemin ses douze Disciples, et leur dit:
Tsopano pamene Yesu ankapita ku Yerusalemu, anatengera pambali ophunzira ake khumi ndi awiriwo nati kwa iwo,
18 Voici, nous montons à Jérusalem, et le Fils de l'homme sera livré aux principaux Sacrificateurs et aux Scribes, et ils le condamneront à la mort.
“Tikupita ku Yerusalemu, ndipo Mwana wa Munthu adzaperekedwa kwa akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo. Iwo adzamuweruza kuti aphedwe,
19 Ils le livreront aux Gentils pour s'en moquer, le fouetter, et le crucifier; mais le troisième jour il ressuscitera.
ndipo adzamupereka kwa anthu a mitundu ina kuti amunyoze ndi kumukwapula ndi kumupachika. Pa tsiku lachitatu adzaukitsidwa!”
20 Alors la mère des fils de Zébédée vint à lui avec ses fils, se prosternant, et lui demandant une grâce.
Amayi a ana a Zebedayo anabwera ndi ana ake kwa Yesu, nagwada pansi namupempha Iye.
21 Et il lui dit: que veux-tu? Elle lui dit: ordonne que mes deux fils, qui sont ici, soient assis l'un à ta main droite, et l'autre à ta gauche dans ton Royaume.
Yesu anawafunsa kuti, “Mukufuna chiyani?” Amayiwo anati, “Lolani kuti ana anga awiriwa adzakhale mmodzi ku dzanja lanu lamanja ndi wina ku dzanja lanu lamazere mu ufumu wanu.”
22 Et Jésus répondit et dit: vous ne savez ce que vous demandez, pouvez-vous boire la coupe que je dois boire, et être baptisés du baptême dont je dois être baptisé; ils lui répondirent: nous le pouvons.
Yesu anawawuza kuti, “Simukudziwa chimene mukupempha. Kodi mungathe kumwera chikho chimene ndidzamwera Ine?” Iwo anayankha nati, “Inde tingathe.”
23 Et il leur dit: il est vrai que vous boirez ma coupe, et que vous serez baptisés du baptême dont je serai baptisé; mais d'être assis à ma droite ou à ma gauche, ce n'est point à moi de le donner, mais [il sera donné] à ceux à qui cela est destiné par mon Père.
Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi mudzamwera chikho changa, koma kuti mudzakhale ku dzanja langa lamanja kapena lamazere si kwa Ine kupereka. Malo awa ndi a iwo amene anakonzeredweratu ndi Atate anga.”
24 Les dix [autres Disciples] ayant ouï cela, furent indignés contre les deux frères.
Ophunzira khumi aja, anawapsera mtima abale awiriwo.
25 Mais Jésus les ayant appelés, leur dit: vous savez que les Princes des nations les maîtrisent, et que les Grands usent d'autorité sur elles.
Yesu anawayitana onse pamodzi nati, “Mukudziwa kuti olamulira a mitundu ina ali ndi mphamvu pa iwo, ndipo akuluakulu awo amawalamulira.
26 Mais il n'en sera pas ainsi entre vous: au contraire, quiconque voudra être grand entre vous, qu'il soit votre serviteur.
Siziyenera kutero ndi inu. Mʼmalo mwake, aliyense amene akufuna kukhala wamkulu pakati panu akhale wotumikira wanu.
27 Et quiconque voudra être le premier entre vous, qu'il soit votre serviteur.
Ndipo aliyense amene akufuna kukhala woyamba akhale kapolo wanu.
28 De même que le Fils de l'homme n'est pas venu pour être servi, mais pour servir, et afin de donner sa vie en rançon pour plusieurs.
Momwenso Mwana wa Munthu sanabwere kudzatumikiridwa, koma kudzatumikira, ndi kupereka moyo wake kukhala dipo la anthu ambiri.”
29 Et comme ils partaient de Jéricho, une grande troupe le suivit.
Pamene Yesu ndi ophunzira ake ankachoka ku Yeriko, gulu lalikulu la anthu linawatsata.
30 Et voici, deux aveugles qui étaient assis au bord du chemin, ayant ouï que Jésus passait, crièrent, en disant: Seigneur, Fils de David! aie pitié de nous!
Amuna awiri osaona anakhala mʼmbali mwa msewu, ndipo pamene anamva kuti Yesu akudutsa anafuwula kuti, “Ambuye, Mwana wa Davide, tichitireni chifundo!”
31 Et la troupe les reprit, afin qu'ils se tussent; mais ils criaient encore plus fort: Seigneur, Fils de David! aie pitié de nous!
Gulu la anthulo linawadzudzula iwo ndi kuwawuza kuti akhale chete, koma anafuwulitsabe kuti, “Ambuye, Mwana wa Davide, tichitireni chifundo!”
32 Et Jésus s'arrêtant, les appela, et leur dit: que voulez-vous que je vous fasse?
Yesu anayima ndi kuwayitana ndipo anawafunsa kuti, “Mukufuna ndikuchitireni chiyani?”
33 Ils lui dirent: Seigneur, que nos yeux soient ouverts.
Anamuyankha nati, “Ambuye, tikufuna tione!”
34 Et Jésus étant ému de compassion, toucha leurs yeux, et incontinent leurs yeux recouvrèrent la vue; et ils le suivirent.
Yesu anamva nawo chifundo ndipo anakhudza maso awo. Nthawi yomweyo anaona namutsata Iye.

< Matthieu 20 >