< Juges 18 >

1 En ce temps-là il n'y avait point de Roi en Israël, et en ce même temps la tribu de Dan cherchait un héritage pour soi afin d'y demeurer; car jusqu'à ce temps-là il ne lui en était point échu entre les Tribus d'Israël pour le posséder.
Masiku amenewo munalibe mfumu mu Israeli. Ndipo anthu a fuko la Dani amafunafuna malo okhalamo ngati cholowa chawo, chifukwa kufikira nthawi imeneyo anali asanalandire cholowa chawo pakati pa mafuko a Israeli.
2 C'est pourquoi les enfants de Dan envoyèrent de leur famille cinq hommes, d'une et d'autre qualité, gens vaillants, de Tsorah et d'Estaol, pour reconnaître le pays, et le reconnaître exactement; et leur dirent: Allez [et] reconnaissez exactement le pays. Ils vinrent donc en la montagne d'Ephraïm jusqu'à la maison de Mica, et y passèrent la nuit.
Choncho fuko la Dani linatumiza kuchokera ku mabanja awo onse anthu olimba mtima asanu. Anthuwa anachokera ku Zora ndi ku Esitaoli ndipo anatumidwa kukazonda ndi kuliyendera dzikolo. Anthu amenewa ankayimira fuko lonse la Dani. Anthuwa anawawuza kuti, “Pitani mukazonde dzikolo.” Anthuwa anafika ku dziko la mapiri la Efereimu ndi kupita ku nyumba ya Mika komwe anakagona.
3 Et quand ils furent auprès de la maison de Mica, ils reconnurent la voix du jeune homme Lévite; et s'étant détournés vers cette maison-là, ils lui dirent: Qui t'a amené ici, qu'y fais-tu? et qu'as-tu ici?
Ali ku nyumba ya Mika anazindikira mawu a mnyamata, Mlevi uja. Choncho anapita kwa iye namufunsa kuti, “Unabwera ndi ndani kuno? Nanga ukuchita chiyani ku malo ano? Komanso nʼchifukwa chiyani uli kuno?”
4 Et il répondit: Mica a fait pour moi telle et telle chose; il m'a donné des gages et je lui sers de Sacrificateur.
Iye anawawuza zimene Mika anamuchitira ndipo anati, “Iye anandilemba ntchito ndipo ndine wansembe wake.”
5 Ils dirent encore: Nous te prions de consulter Dieu, afin que nous sachions si le voyage que nous entreprenons prospérera.
Kenaka iwo anati kwa iye, “Chonde tifunsire kwa Mulungu kuti tidziwe ngati ulendo wathuwu tiyende bwino.”
6 Et le Sacrificateur leur dit: Allez en paix; l'Eternel a devant ses yeux le voyage que vous entreprenez.
Wansembeyo anawayankha kuti, “Pitani mu mtendere, Yehova ali ndi inu pa ulendo wanuwu.”
7 Ces cinq hommes donc s'en allèrent, et arrivèrent à Laïs, et ils virent que le peuple de cette ville habitait en assurance, et vivait en repos, et se croyait en sûreté, à la façon des Sidoniens; et qu'il n'y avait personne au pays qui leur fît de la peine en aucune chose, parce qu'ils étaient libres de toute ancienneté; et aussi ils étaient éloignés des Sidoniens, et n'avaient commerce avec personne.
Choncho anthu asanuwo ananyamuka ndipo anafika ku Laisi, kumene anaona kuti anthu ankakhala mwabata monga anthu a ku Sidoni. Anali anthu opanda chowavuta ndiponso aphee. Tsono popeza mʼdziko mwawo analibe chosowa, iwo anali a chuma. Anaonanso kuti anthuwo ankakhala kutali ndi Sidoni ndipo analibe ubale ndi wina aliyense.
8 Puis étant revenus à leurs frères à Tsorah [et] à Estaol, leurs frères leur dirent: Que [rapportez]-vous?
Ozonda dziko aja atabwerera kwa abale awo ku Zora ndi Esitaoli, abale awowo anawafunsa kuti, “Mwaonako zotani?”
9 Et ils répondirent: Allons, montons contr'eux; car nous avons vu le pays, et nous l'avons trouvé très-bon; et vous êtes sans rien faire? ne soyez point paresseux à partir pour aller posséder le pays.
“Tiyeni tikamenyane nawo nkhondo popeza taliona dziko lawolo kuti ndi lachonde kwambiri. Kodi simuchitapo kanthu? Musachite mphwayi kupita mʼdzikomo ndi kukalilanda.
10 Quand vous y entrerez, vous viendrez vers un peuple qui se tient assuré, et en un pays de grande étendue, car Dieu l'a livré entre vos mains; c'est un lieu où il ne manque rien de tout ce qui est sur la terre.
Mukalowa, mukapeza anthu amene ali osatekeseka ndi dziko lalikulu. Yehova wakupatsani dziko limeneli. Malowo ngosasowa kanthu kalikonse kopezeka pa dziko lapansi.”
11 Il partit donc de là, [savoir] de Tsorah et d'Estaol, six cents hommes armés de la famille de Dan.
Kenaka anthu 600 a fuko la Dani ananyamuka ku Zora ndi Esitaoli atanyamula zida za nkhondo.
12 Et montant, ils campèrent à Kirjath-jéharim, qui est en Juda; c'est pourquoi on a appelé ce lieu-là Mahané-dan, jusqu'à ce jour, et il est derrière Kirjath-jéharim.
Tsono anakamanga msasa ku Kiriati-Yearimu mʼdziko la Yuda. Malowa ali kumadzulo kwa Kiriati-Yearimu. Ichi ndi chifukwa chake malowo akutchedwa Mahane Dani mpaka lero.
13 Puis de là ils passèrent à la montagne d'Ephraïm, et arrivèrent à la maison de Mica.
Kuchokera kumeneko anapita ku dziko lamapiri la Efereimu ndipo anafika ku nyumba ya Mika.
14 Alors les cinq hommes qui étaient allés pour reconnaître le pays de Laïs, prenant la parole, dirent à leurs frères: Savez-vous bien qu'en ces maisons il y a un Ephod et des Théraphims, une image de taille et une de fonte? Voyez donc maintenant ce que vous aurez à faire.
Anthu asanu amene anakazonda dziko la Laisi anati kwa abale awo, “Kodi mukudziwa kuti imodzi mwa nyumba izi muli efodi, mafano a mʼnyumba otchedwa terafimu, fano losema ndiponso fano lokuta ndi siliva? Ndiye mudziwe chochita.”
15 Alors ils se détournèrent vers ce lieu-là, et vinrent en la maison où était le jeune homme Lévite, savoir en la maison de Mica, et le saluèrent.
Choncho anthuwa anapatuka napita ku nyumba ya Mika kumene mnyamata, Mlevi uja ankakhala ndipo anamufunsa za mmene zinthu zilili.
16 Or les six cents hommes des enfants de Dan, qui étaient sous les armes, s'arrêtèrent à l'entrée de la porte;
Nthawi imeneyi nʼkuti anthu 600 a fuko la Dani aja atayima pa chipata atanyamula zida za nkhondo.
17 Mais les cinq hommes qui étaient allés pour reconnaître le pays, montèrent et entrèrent dans la maison, et prirent l'imagé taillée, l'Ephod, les Théraphims, et l'image de fonte, pendant que le Sacrificateur était à l'entrée de la porte, avec les six cents hommes armés.
Anthu asanu amene anakazonda dziko aja analowa ndi kukatenga fano losema, efodi, fano la mʼnyumba lotchedwa terafimu, ndi fano lokutidwa ndi siliva. Nthawiyi nʼkuti wansembe uja ndi anthu 600 okhala ndi zida za nkhondo aja ali chiyimire pa chipata.
18 Etant donc entrés dans la maison de Mica, ils prirent l'image taillée, l'Ephod, les Théraphims, et l'image de fonte. Et le Sacrificateur leur dit: Que faites-vous?
Anthuwo atalowa mʼnyumba ya Mika ndi kutenga fano losema, efodi, fano la mʼnyumba, ndi fano lokutidwa ndi siliva, wansembeyo anawafunsa kuti, “Kodi mukuchita chiyani?”
19 Et ils lui dirent: Tais-toi, et mets ta main sur ta bouche, et viens avec nous, et sois-nous pour père et pour Sacrificateur. Lequel te vaut-il mieux, d'être Sacrificateur de la maison d'un homme seul, ou d'être Sacrificateur d'une Tribu et d'une famille en Israël?
Iwo anamuyankha kuti, “Khala chete usayankhule. Tsagana nafe ndipo udzakhala mlangizi wathu ndi wansembe wathu. Kodi si kwabwino kwa iwe kukhala wansembe wa fuko lonse la Israeli mʼmalo mokhala wansembe wa munthu mmodzi yekha?”
20 Et le Sacrificateur en eut de la joie en son cœur, et ayant pris l'Ephod, les Théraphims, et l'image taillée, il se mit au milieu du peuple.
Wansembeyo anakondwera ndipo anatenga efodi, fano la mʼnyumba ndi fano losema natsagana nawo.
21 Après quoi ils retournèrent et reprirent leur chemin, et mirent devant eux les petits enfants, le bétail, et le bagage.
Choncho iwo anatembenuka nachoka, atatsogoza ana, zoweta ndi katundu wawo yense.
22 Et quand ils furent loin de la maison de Mica, ceux qui [demeuraient] dans les maisons voisines de celle de Mica furent assemblés à grand cri; et ils atteignirent les enfants de Dan.
Atayenda mtunda pangʼono kuchokera pa nyumba ya Mika, anthu amene amakhala pafupi ndi nyumba ya Mika anasonkhana kulondola a fuko la Dani aja, ndipo anawapeza.
23 Et ils crièrent après eux; mais eux tournant visage dirent à Mica: Qu'as-tu, que tu te sois ainsi écrié pour amasser des gens?
Atawafuwulira, a fuko la Dani aja anachewuka ndipo anafunsa Mika kuti, “Chavuta nʼchiyani kuti usonkhanitse anthu chotere?”
24 Il répondit: Vous avez enlevé mes dieux que j'avais faits, vous [avez pris] le Sacrificateur, et vous en êtes allés. Et que me reste-t-il? Comment donc me dites-vous: Qu'as-tu?
Iye anayankha kuti, “Inu mwanditengera milungu imene ndinapanga pamodzi ndi wansembe nʼkumapita. Tsono ine ndatsala ndi chiyani? Ndiye inu mungafunse kuti chavuta nʼchiyani?”
25 Et les enfants de Dan lui dirent: Ne fais point entendre ta voix après nous, de peur que ces gens en colère ne se jettent sur vous, et que vous n'y laissiez la vie, toi, et tous ceux de ta famille.
Anthu a fuko la Dani aja anayankha kuti, “Usayankhuleponso kanthu chifukwa anthu awa angapse mtima nakumenya ndipo iwe ndi banja lako lonse nʼkutayapo miyoyo yanu.”
26 Les enfants donc de Dan continuèrent leur chemin, mais Mica ayant vu qu'ils étaient plus forts que lui, tourna visage, et s'en revint en sa maison.
Choncho anthu a fuko la Dani anapitiriza ulendo wawo. Mika ataona kuti anthuwo anali amphamvu kuposa iye, anangotembenuka kubwerera kwawo.
27 Ainsi ayant pris les choses que Mica avait faites, et le Sacrificateur qu'il avait, ils arrivèrent à Laïs, vers un peuple qui était en repos, et qui se tenait assuré, et ils les firent passer au fil de l'épée, et ayant mis le feu dans la ville, ils la brûlèrent.
Anthu a fuko la Dani aja anatenga zinthu zimene Mika anapanga pamodzi ndi wansembe uja. Iwo anakafika ku Laisi kwa anthu a phee, osatekeseka aja ndipo anawathira nkhondo, nawapha ndi kutentha mzindawo ndi moto.
28 Et il n'y eut personne qui la délivrât; car elle était loin de Sidon, et n'avait commerce avec personne, et elle était située en la vallée qui appartenait au [pays de] Beth-réhob: puis ils bâtirent [là] une ville, et y habitèrent.
Panalibe wowapulumutsa chifukwa anali kutali ndi Sidoni ndiponso sanali pa ubale ndi wina aliyense. Mzindawo unali mʼchigwa cha Beti-Rehobu. Anthu a fuko la Adaniwo anawumanganso mzindawo ndi kumakhalamo.
29 Et ils nommèrent cette ville-là, Dan; selon le nom de Dan leur père qui était né à Israël, au lieu que la ville avait nom auparavant Laïs.
Iwo anawutcha mzindawo Dani, kutengera dzina la kholo lawo Dani, amene anali mwana wa Israeli, ngakhale kuti mzindawo poyamba unali Laisi.
30 Et les enfants de Dan se dressèrent cette image taillée, et Jonathan fils de Guerson, fils de Manassé, lui et ses enfants furent Sacrificateurs pour la Tribu de Dan jusqu'au jour qu'elle partit du pays.
Anthu a fuko la Dani anayimiritsa fano losema lija. Yonatani mwana wa Geresomu, mwana wa Mose pamodzi ndi ana ake onse anakhala ansembe a fuko la Dani mpaka pa tsiku la ukapolo wa dzikolo.
31 Ils y dressèrent donc l'image taillée que Mica avait faite, tout le temps que la maison de Dieu fut à Silo.
Choncho anthu a fuko la Dani ankapembedza fano limene Mika anapanga nthawi yonse pamene nyumba ya Mulungu inali ku Silo.

< Juges 18 >