< Josué 4 >

1 Or il arriva que quand tout le peuple eut achevé de passer le Jourdain, parce que l'Eternel avait parlé à Josué; [et lui avait] dit:
Anthu onse atatha kuwoloka Yorodani, Yehova anati kwa Yoswa,
2 Prenez du peuple douze hommes, [savoir] un homme de chaque Tribu;
“Sankha amuna khumi ndi awiri, mmodzi pa fuko lililonse.
3 Et leur commandez, en disant: Prenez d'ici du milieu du Jourdain, du lieu où les Sacrificateurs s'arrêtent [de pied] ferme, douze pierres, que vous emporterez avec vous, et vous les poserez au lieu où vous logerez cette nuit.
Tsono uwalamule kuti, ‘Tengani miyala khumi ndi iwiri pakati penipeni pa mtsinje wa Yorodani, pamalo pamene ansembe anayimirirapo. Miyalayo muwoloke nayo ndi kudzayitula pamalo pamene mukagone usiku uno.’”
4 Josué appela les douze hommes qu'il avait ordonnés d'entre les enfants d'Israël, un homme de chaque Tribu;
Choncho Yoswa anayitana amuna khumi ndi awiri amene anawasankha aja kuchokera pakati pa Aisraeli, mmodzi pa fuko lililonse,
5 Et il leur dit: Passez devant l'Arche de l'Eternel votre Dieu, au milieu du Jourdain, et que chacun de vous lève une pierre sur son épaule, selon le nombre des Tribus des enfants d'Israël;
ndipo anawawuza kuti, “Lowani pakati pa mtsinje wa Yorodani, patsogolo pa Bokosi la Yehova Mulungu wanu. Ndipo aliyense wa inu atenge mwala pa phewa lake, monga mwa chiwerengero cha mafuko a Aisraeli,
6 Afin que cela soit un signe parmi vous; [et] quand vos enfants interrogeront à l'avenir leurs pères, en disant: Que signifient ces pierres-ci?
kuti ikhale chizindikiro kwa inu. Mʼtsogolo muno ana anu akamadzakufunsani kuti, ‘Kodi miyala iyi ikutanthauza chiyani?’
7 Alors vous leur répondrez que les eaux du Jourdain ont été suspendues devant l'Arche de l'alliance de l'Eternel, que les eaux, [dis-je], du Jourdain ont été arrêtées quand elle passa le Jourdain; c'est pourquoi ces pierres-là serviront de mémorial aux enfants d'Israël à jamais.
Muzidzawawuza kuti, ‘Madzi a Yorodani analeka kuyenda pamene Bokosi la Chipangano la Yehova linkawoloka mtsinjewo. Miyala iyi idzakhala chikumbutso kwa anthu a Israeli kwa muyaya.’”
8 Les enfants d'Israël donc firent comme Josué avait commandé. Ils prirent douze pierres du milieu du Jourdain, ainsi que l'Eternel l'avait commandé à Josué, selon le nombre des Tribus des enfants d'Israël, ils les emportèrent avec eux au lieu où ils devaient loger, et les posèrent là.
Aisraeli anachitadi monga Yoswa anawalamulira. Iwo ananyamula miyala khumi ndi iwiri kuchokera pakati pa Yorodani, fuko lililonse la Israeli mwala wake, monga Yehova analamulira Yoswa. Miyalayo anapita nayo ku misasa yawo nakayikhazika kumeneko.
9 Josué aussi dressa douze pierres au milieu du Jourdain, au lieu où les pieds des Sacrificateurs qui portaient l'Arche de l'alliance s'étaient arrêtés; [et] elles y sont demeurées jusqu'à ce jour.
Yoswa anayimika miyala khumi ndi iwiri imene inali pakati pa Yorodani pamalo pamene ansembe onyamula Bokosi la Chipangano anayimapo. Ndipo miyalayo ili pamalo pomwepo mpaka lero lino.
10 Les Sacrificateurs donc qui portaient l'Arche, se tinrent debout au milieu du Jourdain, jusqu'à ce que tout ce que l'Eternel avait commandé à Josué de dire au peuple fût accompli, suivant toutes les choses que Moïse avait commandées à Josué; et le peuple se hâta de passer.
Ansembe onyamula Bokosi lija anayimirirabe pakati pa Yorodani mpaka zonse zimene Yehova analamulira Yoswa kuti awuze anthu zinatha. Zimenezi zinali monga momwe Mose anamufotokozera Yoswa. Tsono anthu anawoloka mtsinjewo mofulumira.
11 Et quand tout le peuple eut achevé de passer, alors l'Arche de l'Eternel passa, et les Sacrificateurs devant le peuple.
Anthu atatha kuwoloka, ansembe anatsogolera anthuwo atanyamula Bokosi la Yehova.
12 Et les enfants de Ruben, et les enfants de Gad, et la moitié de la Tribu de Manassé passèrent en armes devant les enfants d'Israël, comme Moïse leur avait dit.
Anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase anawoloka patsogolo pa Aisraeli ali ndi zida, monga momwe Mose anawalamulira.
13 Ils passèrent, [dis-je], vers les campagnes de Jérico environ quarante mille hommes en équipage de guerre, devant l'Eternel, pour combattre.
Asilikali pafupifupi 40,000 anawoloka napita kukayima mʼchigwa cha Yeriko kukonzekera nkhondo.
14 En ce jour-là l'Eternel éleva Josué, à la vue de tout Israël, et ils le craignirent comme ils avaient craint Moïse, tous les jours de sa vie.
Zimene Yehova anachita tsiku limeneli zinapatsa anthu mtima wolemekeza Yoswa. Ndipo anamulemekeza masiku onse a moyo wake, monga momwe analemekezera Mose.
15 Or l'Eternel avait parlé à Josué, en disant:
Kenaka Yehova anati kwa Yoswa,
16 Commande aux Sacrificateurs, qui portent l'Arche du Témoignage, qu'ils montent hors du Jourdain.
“Lamula ansembe onyamula Bokosi la Chipanganowo kuti atuluke mu Yorodani.”
17 Et Josué avait commandé aux Sacrificateurs, en disant: Montez hors du Jourdain.
Choncho Yoswa anawalamuladi ansembe aja kuti atuluke mu Yorodani muja.
18 Or sitôt que les Sacrificateurs, qui portaient l'Arche de l'alliance de l'Eternel, furent montés hors du milieu du Jourdain, et que les Sacrificateurs eurent mis sur le sec les plantes de leurs pieds, les eaux du Jourdain retournèrent en leur lieu, et coulèrent comme auparavant, par dessus tous les rivages.
Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova aja atangotuluka mu mtsinje muja nʼkuponda powuma, madzi a mu Yorodani anayambanso kuyenda ngati poyamba mpaka kumasefukira.
19 Le peuple donc monta hors du Jourdain le dixième jour du premier mois, et ils se campèrent en Guilgal, à l'Orient de Jérico.
Aisraeli anawoloka Yorodani tsiku lakhumi la mwezi woyamba ndipo anakamanga misasa yawo ku Giligala mbali ya kummawa kwa Yeriko.
20 Josué aussi dressa en Guilgal ces douze pierres qu'ils avaient prises du Jourdain.
Ku Giligala, Yoswa anayimikako miyala khumi ndi iwiri imene anayitenga mu Yorodani ija.
21 Et il parla aux enfants d'Israël, et leur dit: Quand vos enfants interrogeront à l'avenir leurs pères, et leur diront: Que [signifient] ces pierres-ci?
Ndipo iye anati kwa Aisraeli, “Mʼtsogolo muno pamene adzukulu anu adzafunsa makolo awo kuti, ‘Kodi miyala iyi ikutanthauza chiyani?’
22 Vous l'apprendrez à vos enfants, en [leur] disant, Israël a passé ce Jourdain à sec.
Muzidzawawuza kuti, ‘Aisraeli anawoloka Yorodani pansi pali powuma.’
23 Car l'Eternel votre Dieu fit tarir les eaux du Jourdain devant vous, jusqu'à ce que vous fussiez passés; comme l'Eternel votre Dieu avait fait à la mer Rouge, laquelle il mit à sec devant nous, jusqu'à ce que nous fussions passés.
Pakuti Yehova Mulungu wanu ndiye anawumitsa Yorodani pamaso panu mpaka inu mutawoloka. Yehova Mulungu wanu anaphwetsa madzi a Yorodani monga mmene anachitira ndi Nyanja Yofiira mpaka ife tinawoloka powuma.
24 Afin que tous les peuples de la terre connaissent que la main de l'Eternel est forte; [et] afin que vous craigniez toujours l'Eternel votre Dieu.
Iye anachita zimenezi kuti anthu onse pa dziko lapansi adziwe kuti dzanja la Yehova ndi lamphamvu, ndi kuti inu muziopa Yehova Mulungu wanu masiku onse.”

< Josué 4 >