< Job 22 >

1 Alors Eliphas Témanite prit la parole, et dit:
Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
2 L'homme apportera-t-il quelque profit au [Dieu] Fort? c'est plutôt à soi-même que l'homme sage apporte du profit.
“Kodi munthu nʼkukhala waphindu kwa Mulungu? Kodi munthu wanzeru angamupindulire Iye?
3 Le Tout-puissant reçoit-il quelque plaisir, si tu es juste? ou quelque gain, si tu marches dans l'intégrité?
Kodi Wamphamvuzonse akanapeza chabwino chotani iweyo ukanakhala wolungama? Kodi iyeyo akanapeza phindu lanji makhalidwe ako akanakhala angwiro?
4 Te reprend-il, [et] entre-t-il avec toi en jugement pour la crainte qu'il ait de toi?
“Kodi nʼchifukwa choti umamuopa, kuti azikudzudzula, kuti azifuna kukukokera ku mlandu?
5 Ta méchanceté n'est-elle pas grande? et tes injustices ne sont-elles pas sans fin?
Kodi osati nʼchifukwa chakuti kuyipa kwako nʼkwakukulu? Kodi machimo ako si opanda malire?
6 Car tu as pris sans raison le gage de tes frères; tu as ôté la robe à ceux qui étaient nus.
Iwe unkawumiriza abale ako kuti akupatse chikole popanda chifukwa; umalanda anthu zovala zawo ndi kuwasiya amaliseche.
7 Tu n'as pas donné de l'eau à boire à celui qui était fatigué [du chemin]; tu as refusé ton pain à celui qui avait faim.
Sunawapatse madzi anthu otopa, ndipo unawamana chakudya anthu anjala,
8 La terre était à l'homme puissant, et celui qui était respecté y habitait.
ngakhale unali munthu wamphamvu, wokhala ndi malo akeake, munthu waulemu wake, wokhala mʼdzikomo.
9 Tu as envoyé les veuves vides, et les bras des orphelins ont été cassés.
Ndipo akazi amasiye unawachotsa wopanda kanthu, ndipo unapondereza ana amasiye.
10 C'est pour cela que les filets sont tendus autour de toi, et qu'une frayeur subite t'épouvante.
Nʼchifukwa chake misampha yakuzungulira, nʼchifukwa chake tsoka ladzidzidzi lakuchititsa mantha,
11 Et les ténèbres [sont autour de toi], tellement que tu ne vois point; et le débordement des eaux te couvre.
nʼchifukwa chake kuli mdima kuti sungathe kuona kanthu, nʼchifukwa chakenso madzi achigumula akumiza.
12 Dieu n'habite-t-il pas au plus haut des cieux? Regarde donc la hauteur des étoiles; [et] combien elles sont élevées.
“Kodi Mulungu sali kutalitali kumwamba? Ndipo ona nyenyezi zili mmwamba kwambirizo, ona kutalika kwake pamene zililipo!
13 Mais tu as dit: Qu'est-ce que le [Dieu] Fort connaît? Jugera-t-il au travers des nuées obscures?
Komabe iweyo ukunena kuti, ‘Kodi Mulungu amadziwa chiyani? Kodi Iye amaweruza mu mdima woterewu?
14 Les nuées nous cachent à ses yeux, et il ne voit rien, il se promène sur le tour des cieux.
Mitambo yakuda yamuphimba, kotero kuti Iye sakutiona pamene akuyendayenda pamwamba pa thambopo.’
15 [Mais] n'as-tu pas pris garde au vieux chemin dans lequel les hommes injustes ont marché?
Kodi iwe udzayendabe mʼnjira yakale imene anthu oyipa ankayendamo?
16 [Et n'as-tu pas pris garde] qu'ils ont été retranchés avant le temps; et que ce sur quoi ils se fondaient s'est écoulé comme un fleuve.
Iwo anachotsedwa nthawi yawo isanakwane, maziko awo anakokoloka ndi madzi achigumula.
17 Ils disaient au [Dieu] Fort: Retire-toi de nous. Mais qu'est-ce que leur faisait le Tout-puissant?
Anthuwo anati kwa Mulungu, ‘Tichokereni! Kodi Wamphamvuzonse angatichitire chiyani?’
18 Il avait rempli leur maison de biens. Que le conseil des méchants soit [donc] loin de moi!
Chonsecho ndi Iye amene anadzaza nyumba zawo ndi zinthu zabwino, choncho ine sindigwirizana ndi uphungu wa anthu oyipa.
19 Les justes le verront, et s'en réjouiront, et l'innocent se moquera d'eux.
“Anthu olungama amaona kuwonongeka kwawo ndipo amakondwera; anthu osalakwa amangoseka, akamuona woyipa akulangidwa.
20 Certainement notre état n'a point été aboli, mais le feu a dévoré leur excellence.
Amanena kuti, ‘Ndithudi adani athu awonongeka ndipo moto wawononga chuma chawo!’
21 Attache-toi à lui, je te prie, et demeure en repos, par ce moyen il t'arrivera du bien.
“Gonjera Mulungu kuti ukhale naye pamtendere; ukatero udzaona zabwino.
22 Reçois, je te prie, la loi de sa bouche, et mets ses paroles en ton cœur.
Landira malangizo a pakamwa pake ndipo usunge mawu ake mu mtima mwako.
23 Si tu retournes au Tout-puissant, tu seras rétabli. Chasse l'iniquité loin de ta tente.
Ukabwerera kwa Wamphamvuzonse udzabwezeretsedwa; ukachotsa zoyipa zonse zimene zimachitika mʼnyumba mwako,
24 Et tu mettras l'or sur la poussière, et l'or d'Ophir sur les rochers des torrents.
ndipo chuma chamtengowapatali nuchiona ngati fumbi, golide wa ku Ofiri numutaya ku miyala ya ku zigwa.
25 Et le Tout-puissant sera ton or, et l'argent de tes forces.
Pamenepo Wamphamvuzonseyo adzakhala golide wako, siliva wako wamtengowapatali.
26 Car alors tu trouveras tes délices dans le Tout-puissant, et tu élèveras ton visage vers Dieu.
Pamenepo udzakondwera naye Wamphamvuzonse ndipo udzakweza nkhope yako kwa Mulungu.
27 Tu le fléchiras par tes prières, et il t'exaucera, et tu lui rendras tes vœux.
Udzamupempha ndipo adzakumvera, ndipo udzapereka zimene unalonjeza.
28 Si tu as quelque dessein, il te réussira, et la lumière resplendira sur tes voies.
Chimene watsimikiza kuti uchite, chidzachitikadi, kuwala kudzakuwunikira pa njira yako.
29 Quand on aura abaissé quelqu'un, et que tu auras dit: Qu'il soit élevé; alors [Dieu] délivrera celui qui tenait les yeux baissés.
Pamene anthu agwetsedwa pansi, iwe nʼkunena kuti, ‘Akwezeni!’ Pamenepo Iye adzapulumutsa anthu oponderezedwa.
30 Il délivrera celui qui n'est pas innocent, et il sera délivré par la pureté de tes mains.
Iye adzapulumutsa ngakhale munthu amene ndi wolakwa, ameneyo adzapulumutsidwa kudzera mʼkulungama kwako.”

< Job 22 >