< Jérémie 4 >

1 Israël, si tu te retournes, dit l'Eternel, retourne-toi à moi; si tu ôtes tes abominations de devant moi, tu ne seras plus errant ça et là.
“Ngati mukufuna kubwerera, inu Aisraeli, bwererani kwa Ine,” akutero Yehova. “Chotsani mafano anu onyansa pamaso panga ndipo musasocherenso.
2 Alors tu jureras en vérité, et en jugement, et en justice, l'Eternel est vivant; et les nations se béniront en lui, et se glorifieront en lui.
Muzilumbira mokhulupirika ndiponso mwa chilungamo kuti, ‘Pali Yehova wamoyo.’ Mukatero anthu a mitundu ina yonse adzandipempha kuti ndiwadalitse ndipo adzanditamanda.”
3 Car ainsi a dit l'Eternel à ceux de Juda et de Jérusalem: défrichez-vous les terres, et ne semez point sur les épines.
Zimene Yehova akunena kwa anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu ndi izi: “Limani masala anu musadzale pakati pa minga.
4 Hommes de Juda, et vous habitants de Jérusalem, soyez circoncis à l'Eternel, et ôtez les prépuces de vos cœurs; de peur que ma fureur ne sorte comme un feu, et qu'elle ne s'embrase, sans qu'il y ait personne qui l'éteigne, à cause de la méchanceté de vos actions.
Dziperekeni nokha kwa Ine kuti munditumikire ndi mtima wanu wonse, inu anthu a ku Yuda ndi ku Yerusalemu. Muzichita zimenezi kuopa kuti mkwiyo wanga ungabuke ngati moto ndi kukutenthani, chifukwa cha ntchito zanu zoyipazo popanda wina wowuzimitsa.
5 Faites savoir en Juda, et publiez dans Jérusalem, et dites: sonnez du cor par le pays, criez, [et] vous amassez; et dites: assemblez-vous, et nous entrerons dans les villes fortes.
“Lengeza ku Yuda ndi kulalikira mu Yerusalemu kuti, ‘Lizani lipenga mʼdziko lonse!’ Ndipo fuwulani kuti, ‘Sonkhanani! Tiyeni tithawire ku mizinda yotetezedwa!’
6 Dressez l'enseigne vers Sion, retirez-vous en troupe, et ne vous arrêtez point; car je m'en vais faire venir de l'Aquilon le mal et une grande calamité.
Kwezani mbendera kuyangʼana ku Ziyoni! Musachedwe, thawani kuti mupulumuke! Pakuti Ine ndikubweretsa chilango kuchokera kumpoto, kudzakhala chiwonongeko choopsa.”
7 Le lion est sorti de la caverne, et le destructeur des nations est parti; il est sorti de son lieu pour réduire ton pays en désolation, tes villes seront ruinées, tellement qu'il n'y aura personne qui y habite.
Monga mkango umatulukira mʼngaka yake momwemonso wowononga mayiko wanyamuka ndi kutuluka ku mbuto yake. Watero kuti awononge dziko lanu. Mizinda yanu idzakhala mabwinja popanda wokhalamo.
8 C'est pourquoi ceignez-vous de sacs, lamentez, et hurlez; car l'ardeur de la colère de l'Eternel n'est point détournée de nous.
Choncho valani ziguduli, lirani ndi kubuwula, pakuti mkwiyo waukulu wa Yehova sunatichokere.
9 Et il arrivera en ce jour-là, dit l'Eternel, que le cœur du Roi, et le cœur des principaux sera épouvanté, et que les Sacrificateurs seront étonnés, et que les Prophètes seront tout confus.
“Pa tsiku limenelo, mfumu ndi nduna zake adzataya mtima, ansembe adzachita mantha kwambiri, ndipo aneneri adzathedwa nzeru,” akutero Yehova.
10 C'est pourquoi j'ai dit: ha! ha! Seigneur Eternel! oui certainement tu as abusé ce peuple et Jérusalem, en disant: vous aurez la paix; et l'épée est venue jusqu’à l'âme.
Ndipo ine ndinati, “Haa, Ambuye Yehova, ndithu munawanyenga anthu awa pamodzi ndi Yerusalemu pamene munanena kuti, ‘Mudzakhala pa mtendere,’ chonsecho lupanga lili pakhosi pathu.”
11 En ce temps-là on dira à ce peuple, et à Jérusalem: un vent éclaircissant les lieux élevés [souffle] au désert, dans le chemin de la fille de mon peuple, non pas pour vanner ni pour nettoyer:
Nthawi imeneyo anthu awa ndi Yerusalemu adzawawuza kuti, “Mphepo yotentha yochokera ku magomo a mʼchipululu ikuwomba pa anthu anga, osati mphepo yopeta kapena yoyeretsa;
12 Un vent plus véhément que ceux-là viendra à moi, et je leur ferai maintenant leur procès.
koma mphepo yamphamvu kwambiri yochokera kwa Ine. Tsono ndi Ineyo amene ndikuwaweruza.”
13 Voici, il montera comme des nuées, et ses chariots seront semblables à un tourbillon, ses chevaux seront plus légers que des aigles; malheur à nous! car nous sommes détruits.
Taonani, adani akubwera ngati mitambo, magaleta awo akubwera ngati kamvuluvulu, akavalo awo ndi aliwiro kupambana chiwombankhanga. Tsoka ilo! Tawonongeka!
14 Jérusalem, nettoie ton cœur de ta malice, afin que tu sois délivrée; jusques à quand séjourneront au dedans de toi les pensées de ton injustice?
Iwe Yerusalemu, tsuka mtima wako kuchotsa zoyipa kuti upulumuke. Kodi maganizo ako oyipawo udzakhala nawo mpaka liti?
15 Car le cri apporte des nouvelles de Dan, et publie du mont d'Ephraïm le tourment.
Pakuti amithenga akulalika mawu mʼdziko la Dani; akulengeza za masautso kuchokera ku mapiri a Efereimu.
16 Faites l'entendre aux nations, voici, publiez contre Jérusalem, [et dites]: les assiégeants viennent d'un pays éloigné, et ils ont jeté leur cri contre les villes de Juda.
Iwo akuti, “Fotokozani zimenezi kwa anthu a mitundu ina, lengezani zimenezi mu Yerusalemu kuti, ‘Ankhondo akubwera kuchokera ku dziko lakutali, akufuwula ndi kudzazinga mizinda ya Yuda.
17 Ils se sont mis tout autour d'elle comme les gardes des champs, parce qu'elle m'a été rebelle, dit l'Eternel.
Azinga Yerusalemu ngati anthu olondera munda, chifukwa Yerusalemu wandiwukira,’” akutero Yehova.
18 Ta conduite et tes actions t'ont produit ces choses; telle a été ta malice; parce que ç'a été une chose amère; certainement elle te touchera jusques au cœur.
“Makhalidwe anu ndi zochita zanu zakubweretserani zimenezi. Chimenechi ndiye chilango chanu. Nʼchowawa kwambiri! Nʼcholasa mpaka mu mtima!”
19 Mon ventre! mon ventre! je suis dans la douleur; le dedans de mon cœur, mon cœur me bat, je ne me puis taire; car ô mon âme! tu as ouï le son du cor, et le retentissement bruyant de l'alarme.
Mayo, mayo, ndikumva kupweteka! Aa, mtima wanga ukupweteka, ukugunda kuti thi, thi, thi. Sindingathe kukhala chete. Pakuti ndamva kulira kwa lipenga; ndamva mfuwu wankhondo.
20 Une ruine est appelée par l'autre, car toute la terre est détruite; mes tentes ont été incontinent détruites, [et] mes pavillons en un moment.
Tsoka limatsata tsoka linzake; dziko lonse lasanduka bwinja. Mwadzidzidzi matenti athu awonongedwa, mwa kanthawi kochepa nsalu zake zotchinga zagwetsedwa.
21 Jusques à quand verrai-je l'enseigne, et entendrai-je le son du cor?
Kodi ndikhale ndikuona mbendera ya nkhondo, ndi kumva kulira kwa lipenga mpaka liti?
22 Car mon peuple est insensé, ils ne m'ont point reconnu; ce sont des enfants insensés, et qui n'ont point d'entendement; ils sont habiles à faire le mal, mais ils ne savent pas faire le bien.
Yehova akuti, “Anthu anga ndi zitsiru; iwo sandidziwa. Iwo ndi ana opanda nzeru; samvetsa chilichonse. Ali ndi luso lochita zoyipa, koma sadziwa kuchita zabwino.”
23 J'ai regardé la terre, et voici, elle est sans forme et vide; et les cieux, et il n'y a point de clarté.
Ndinayangʼana dziko lapansi, ndipo linali lopanda anthu ndi lopanda kanthu; ndinayangʼana thambo, koma linalibe kuwala kulikonse.
24 J'ai regardé les montagnes, et voici, elles branlent; et toutes les collines sont renversées.
Ndinayangʼana mapiri, ndipo ankagwedezeka; magomo onse ankangosunthira uku ndi uku.
25 J'ai regardé, et voici, il n'y a pas un seul homme, et tous les oiseaux des cieux s'en sont fuis.
Ndinayangʼana, ndipo sindinaone anthu; mbalame iliyonse ya mlengalenga inali itathawa.
26 J'ai regardé, et voici, Carmel est un désert, et toutes ses villes ont été ruinées par l'Eternel, et par l'ardeur de sa colère.
Ndinayangʼana, dziko lachonde linali litasanduka chipululu; mizinda yake yonse inali itasanduka bwinja pamaso pa Yehova, chifukwa cha mkwiyo wake.
27 Car ainsi a dit l'Eternel: toute la terre ne sera que désolation; néanmoins je ne l'achèverai pas entièrement.
Yehova akuti, “Dziko lonse lidzasanduka chipululu komabe sindidzaliwononga kotheratu.
28 C'est pourquoi la terre mènera deuil, et les cieux seront obscurcis au-dessus, parce que je l'ai prononcé; je l'ai pensé, je ne m'en repentirai point, et je ne le révoquerai point.
Chifukwa chake dziko lapansi lidzalira ndipo thambo lidzachita mdima, pakuti ndayankhula ndipo sindidzafewa mtima, ndatsimikiza ndipo sindidzabwerera mʼmbuyo.”
29 Toute ville s'enfuit à cause du bruit des gens de cheval, et de ceux qui tirent de l'arc; ils sont entrés dans les bois épais, et sont montés sur les rochers; toute ville est abandonnée et personne n'y habite.
Pakumva phokoso la okwera pa akavalo ndi la anthu oponya mivi, anthu a mʼmizinda adzathawa. Ena adzabisala ku nkhalango; ena adzakwera mʼmatanthwe mizinda yonse nʼkuyisiya; popanda munthu wokhalamo.
30 Et quand tu auras été détruite, que feras-tu? quoique tu te vêtes de cramoisi, et que tu te pares d'ornements d'or, et que tu couvres ton visage de fard, tu t'embellis en vain; tes amoureux t'ont rebutée, ils chercheront ta vie.
Iwe Yerusalemu, ndiwe bwinja! Ukutanthauza chiyani kuvala zovala zofiira ndi kuvalanso zokometsera zagolide? Ngakhale udzikonze maso ako powapaka zokometsera, ukungodzivuta chabe. Zibwenzi zako zikukunyoza; zikufuna kuchotsa moyo wako.
31 Car j'ai ouï un cri comme celui d'une [femme] qui est en travail, et une angoisse comme celle d'une femme qui est en travail de son premier-né; c'est le cri de la fille de Sion; elle soupire, elle étend ses mains, [en disant]: Malheur maintenant à moi, car mon âme est défaillie à cause des meurtriers.
Ndikumva kulira ngati kwa mayi pa nthawi yake yobereka, kubuwula ngati kwa mayi amene akubereka mwana wake woyamba. Kuliraku ndi kwa anthu a mu Ziyoni, wefuwefu. Atambalitsa manja awo nʼkumati, “Kalanga ife! Tikukomoka. Moyo wathu waperekedwa kwa anthu otipha.”

< Jérémie 4 >