< Jérémie 26 >

1 Au commencement du règne de Jéhojakim, fils de Josias, Roi de Juda, cette parole fut [adressée] à Jérémie par l'Eternel, en disant:
Yehoyakimu, mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda atayamba kulamulira, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
2 Ainsi a dit l'Eternel: tiens-toi debout au parvis de la maison de l'Eternel, et prononce à toutes les villes de Juda qui viennent pour se prosterner dans la maison de l'Eternel, toutes les paroles que je t'ai commandé de leur prononcer; n'en retranche pas une parole.
“Kayime mʼbwalo la Nyumba ya Yehova. Ndipo ukayankhule kwa anthu onse okhala mʼmizinda ya ku Yuda amene amabwera kudzapembedza ku Nyumba ya Yehova. Ukawawuze zonse zomwe ndakulamula; usakasiyeko ndi mawu amodzi omwe.
3 Peut-être qu'ils écouteront, et qu'ils se détourneront chacun de son mauvais train; et je me repentirai du mal que je pense de leur faire à cause de la malice de leurs actions.
Mwina mwake adzamvera, ndipo aliyense adzatembenuka kuleka njira yake yoyipa. Ndiye ine ndidzaleka osapatsa chilango chimene ndinakonzekera kuti ndiwalange nacho chifukwa cha ntchito zawo zoyipa.
4 Tu leur diras donc: ainsi a dit l'Eternel: si vous ne m'écoutez point pour marcher dans ma Loi, laquelle je vous ai proposée,
Ukawawuze kuti, ‘Yehova akuti: Ngati simundimvera Ine ndi kuleka kutsatira malamulo anga, amene ndakupatsani,
5 Pour obéir aux paroles des Prophètes mes serviteurs que je vous envoie, me levant dès le matin, et [les] envoyant, lesquels vous n'avez point écoutés:
ndipo ngati simumvera mawu a atumiki anga, aneneri amene ndakhala ndikukutumizirani, ngakhale kuti simunawamvere,
6 Je mettrai cette maison en même état que Silo, et je livrerai cette ville en malédiction à toutes les nations de la terre.
ndiye kuti Ine ndidzasandutsa Nyumba ino kukhala ngati Silo ndipo mzinda uno udzakhala chinthu chotembereredwa pakati pa mitundu yonse ya pa dziko lapansi.’”
7 Or les Sacrificateurs et les Prophètes, et tout le peuple entendirent Jérémie prononçant ces paroles dans la maison de l'Eternel.
Ansembe, aneneri ndi anthu onse anamva Yeremiya akuyankhula mawu amenewa mʼNyumba ya Yehova.
8 Et il arriva qu'aussitôt que Jérémie eut achevé de prononcer tout ce que l'Eternel lui avait commandé de prononcer à tout le peuple, les Sacrificateurs et les Prophètes et tout le peuple le saisirent, en disant: tu mourras de mort.
Yeremiya atangotsiriza kuwawuza anthu aja zonse zimene Yehova anamulamula kuti ayankhule, ansembe, aneneri pamodzi ndi anthu onse anamugwira ndipo anati, “Uyenera kuphedwa!
9 Pourquoi as-tu prophétisé au Nom de l'Eternel, disant: cette maison sera comme Silo, et cette ville sera déserte, tellement que personne n'y habitera? Et tout le peuple s'assembla vers Jérémie dans la maison de l'Eternel.
Chifukwa chiyani walosera mʼdzina la Yehova kuti Nyumba ino idzakhala ngati Silo ndipo mzinda uno udzakhala wopanda anthu ngati chipululu?” Anthu onse anamuzungulira Yeremiya mʼNyumba ya Yehova.
10 Et les principaux de Juda ayant ouï toutes ces choses montèrent de la maison du Roi à la maison de l'Eternel, et s'assirent à l'entrée de la porte neuve de la maison de l'Eternel.
Koma nduna za ku Yuda zitamva zomwe zinachitikazi, zinanyamuka kuchokera ku nyumba yaufumu kupita ku Nyumba ya Yehova, nakakhala pamalo pawo, pa Chipata Chatsopano cha Nyumba ya Yehova.
11 Et les Sacrificateurs et les Prophètes parlèrent aux principaux, et à tout le peuple, en disant: cet homme mérite d'être condamné à la mort, car il a prophétisé contre cette ville, comme vous l'avez entendu de vos oreilles.
Pamenepo ansembe ndi aneneri anawuza ndunazo pamodzi ndi anthu onse kuti, “Munthu uyu ayenera kuphedwa chifukwa amalosera zoyipira mzinda uno. Inu mwadzimvera nokha zimenezi!”
12 Et Jérémie parla à tous les principaux, et à tout le peuple, en disant: l'Eternel m'a envoyé pour prophétiser contre cette maison, et contre cette ville, [selon] toutes les paroles que vous avez ouïes.
Ndipo Yeremiya anawuza nduna zija ndi anthu onse kuti, “Yehova anandituma kunenera mawu onse amene mwawamva otsutsa Nyumba ino ndi mzinda uno.
13 Maintenant donc, corrigez votre conduite et vos actions; et écoutez la voix de l'Eternel votre Dieu, et l'Eternel se repentira du mal qu'il a prononcé contre vous.
Tsopano konzani njira zanu ndi zochita zanu ndipo mverani Yehova Mulungu wanu. Mukatero ndiye kuti Yehova adzaleka osakupatsani chilango chimene ankati akupatseni.
14 Pour moi, me voici entre vos mains, faites de moi comme il vous semblera bon et juste.
Kunena za ine, ndili mʼmanja mwanu; mundichite chilichonse chimene mukuganiza kuti ndi chabwino ndi choyenera.
15 Mais sachez comme une chose certaine, que si vous me faites mourir, vous mettrez du sang innocent sur vous, et sur cette ville, et sur ses habitants; car en vérité l'Eternel m'a envoyé vers vous, afin de prononcer toutes ces paroles, vous l'entendant.
Komatu dziwani kuti ngati mundipha, inu pamodzi ndi mzinda uno ndi onse amene amakhala muno, mudzapalamula mlandu wokhetsa magazi a munthu wosalakwa. Ndithudi Yehova anandituma kuti ndidzayankhule mawu onsewa inu mukumva.”
16 Alors les principaux et tout le peuple dirent aux Sacrificateurs et aux Prophètes: cet homme ne mérite pas d'être condamné à la mort; car il nous a parlé au Nom de l'Eternel notre Dieu.
Pamenepo ndunazo pamodzi ndi anthu onse anawuza ansembe ndi aneneri kuti, “Munthu uyu sayenera kuphedwa! Pakuti wayankhula kwa ife mʼdzina la Yehova Mulungu wathu.”
17 Et quelques-uns des Anciens du pays se levèrent, et parlèrent à toute l'assemblée du peuple, en disant:
Akuluakulu ena a mʼdzikomo anayimirira ndi kuwuza gulu lonse la anthu kuti,
18 Michée Morastite a prophétisé aux jours d'Ezéchias Roi de Juda, et a parlé à tout le peuple de Juda, en disant: ainsi a dit l'Eternel des armées, Sion sera labourée [comme] un champ, et Jérusalem sera réduite en monceaux de pierres, et la montagne du Temple en de hauts lieux d'une forêt.
“Mʼmasiku a Hezekiya mfumu ya ku Yuda, Mika wa ku Moreseti ankalosera. Iye ankawuza anthu kuti Yehova Wamphamvuzonse akuti, “‘Ziyoni adzatipulidwa ngati munda, Yerusalemu adzasanduka bwinja, ndipo phiri la Nyumba ya Mulungu lidzasanduka nkhalango yowirira.’
19 Ezéchias le Roi de Juda, et tous ceux de Juda le firent-ils mourir? Ne craignit-il pas l'Eternel, et ne supplia-t-il pas l'Eternel? et l'Eternel se repentit du mal qu'il avait prononcé contre eux; nous faisons donc un grand mal contre nos âmes.
Kodi Hezekiya mfumu ya ku Yuda ndi anthu onse anamupha amene uja? Kodi suja mfumu inaopa Yehova ndi kupempha kuti ayikomere mtima? Ndipo suja Yehova anasintha maganizo ake nʼkuleka kuwalanga monga mʼmene anakonzera? Ifetu tikudziyitanira tsoka lalikulu!”
20 Mais aussi, [dirent les autres], il y eut un homme qui prophétisa au Nom de l'Eternel, [savoir] Urie, fils de Sémahia, de Kiriath-jéharim, lequel ayant prophétisé contre cette même ville, et contre ce même pays, en la même manière que Jérémie;
(Panalinso munthu wina, Uriya mwana wa Semaya wa ku Kiriati-Yeyarimu, amene ankalosera mʼdzina la Yehova. Iyeyu analosera za mzinda uno ndi dziko lino monga mmene wachitira Yeremiya.
21 Et le Roi Jéhojakim, avec tous ses officiers, et les principaux ayant entendu ses paroles, le Roi chercha à le faire mourir; mais Urie l'ayant appris, et ayant craint, s'enfuit, et se retira en Egypte.
Mfumu Yehoyakimu, ankhondo ake onse ndi nduna zake anamva mawu akewo, ndipo anafuna kumupha. Koma Uriya atamva zimenezi, anachita mantha nathawira ku Igupto.
22 Et le Roi Jéhojakim envoya des hommes en Egypte, [savoir] Elnathan, fils de Hacbor, et quelques gens avec lui, qui allèrent en Egypte,
Komabe Mfumu Yehoyakimu anatuma Elinatani mwana wa Akibori pamodzi ndi anthu ena, ku Igupto.
23 Et qui firent revenir Urie d'Egypte, et l'amenèrent au Roi Jéhojakim, qui le frappa avec l'épée, et jeta son corps mort aux sépulcres du peuple.
Iwo anakamutenga Uriya ku Igupto kuja nabwera naye kwa Mfumu Yehoyakimu. Iye anamupha ndi lupanga ndipo mtembo wake anakawutaya ku manda a anthu wamba).
24 Toutefois la main d'Ahikam fils de Saphan fut pour Jérémie, afin qu'on ne le livrât point entre les mains du peuple, pour le faire mourir.
Koma Ahikamu mwana wa Safani ndiye anateteza Yeremiya, motero sanamupereke kwa anthu kuti amuphe.

< Jérémie 26 >