< Jérémie 17 >

1 Le péché de Juda est écrit avec un burin d’acier de fer, [et] avec une pointe de diamant; il est gravé sur la table de leur cœur, et aux cornes de leurs autels.
“Tchimo la Yuda lazokotedwa ndi cholembera cha chitsulo, lalembedwa ndi msonga ya mwala wadayimondi. Uchimowo walembedwa pa mitima yawo ndiponso pa nyanga za maguwa awo.
2 De sorte que leurs fils se souviendront de leurs autels, et de leurs bocages, auprès des arbres verts sur les hautes collines.
Ngakhale ana awo amakumbukira maguwa awo ndi zoyimiritsa ngati zifanizo za mulungu wawo Asera, pa tsinde la mitengo ya masamba ambiri, pa mapiri aatali mʼdzikomo.
3 Montagnard, je livrerai par les champs tes richesses [et] tous tes trésors au pillage; tes hauts lieux [sont pleins] de péché dans toutes tes contrées.
Chuma chanu ndiponso katundu wanu yense ndidzazipereka kwa ofunkha kuti zikhale dipo lawo chifukwa cha machimo ochitika mʼdziko lonse.
4 Et toi, et [ceux qui sont] avec toi, vous laisserez vacant l'héritage que je t'avais donné, et je ferai que tu seras asservi à tes ennemis, dans un pays que tu ne connais point, parce que vous avez allumé le feu en ma colère; [et] il brûlera à toujours.
Mudzataya dziko limene ndinakupatsani kuti likhale cholowa chanu. Ndidzakusandutsani akapolo otumikira adani anu mʼdziko limene inu simukulidziwa, chifukwa mwabutsa mkwiyo wanga ngati moto, ndipo udzayaka mpaka muyaya.”
5 Ainsi a dit l'Eternel: maudit soit l'homme qui se confie en l'homme, et qui fait de la chair son bras, et dont le cœur se retire de l'Eternel.
Yehova akuti, “Ndi wotembereredwa munthu amene amadalira munthu mnzake, amene amatsamira pa munthu mnzake kuti amuthandize pamene mtima wake wafulatira Yehova.
6 Car il sera comme la bruyère en une lande, et il ne s'apercevra point quand le bien sera venu; mais il demeurera au désert en des lieux secs, en une terre salée et inhabitable.
Munthuyo adzakhala ngati chitsamba mʼchipululu; iye sadzapeza zabwino. Adzakhala mʼchipululu mopanda madzi, mʼdziko lamchere limene munthu sangathe kukhalamo.
7 Béni soit l'homme qui se confie en l'Eternel, et duquel l'Eternel est la confiance.
“Koma ndi wodala munthu amene amadalira Yehova, amene amatsamira pa Iye.
8 Car il sera comme un arbre planté près des eaux, et qui étend ses racines le long d'une eau courante; quand la chaleur viendra, il ne s'en apercevra point; et sa feuille sera verte, il ne sera point en peine en l'année de la sécheresse, et ne cessera point de porter du fruit.
Adzakhala ngati mtengo wodzalidwa mʼmphepete mwa madzi umene umatambalitsa mizu yake mʼmbali mwa mtsinje. Mtengowo suopa pamene kukutentha; masamba ake amakhala obiriwira nthawi zonse. Suchita mantha pa chaka cha chilala ndipo sulephera kubereka chipatso.”
9 Le cœur est rusé, et désespérément malin par dessus toutes choses; qui le connaîtra?
Mtima wa munthu ndi wonyenga kupambana zinthu zonse ndipo kuyipa kwake nʼkosachizika. Ndani angathe kuwumvetsa?
10 Je suis l'Eternel, qui sonde le cœur, et qui éprouve les reins; même pour rendre à chacun selon sa voie, [et] selon le fruit de ses actions.
“Ine Yehova ndimafufuza mtima ndi kuyesa maganizo, ndimachitira munthu aliyense molingana ndi makhalidwe ake ndiponso moyenera ntchito zake.”
11 Celui qui acquiert des richesses, sans observer la justice, est une perdrix [qui] couve ce qu'elle n'a point pondu; il les laissera au milieu de ses jours, et à la fin il sera trouvé insensé.
Munthu amene amapeza chuma mwachinyengo ali ngati nkhwali imene imafungatira mazira amene sinayikire. Pamene ali pakatikati pa moyo wake, chumacho chidzamuthera, ndipo potsiriza adzasanduka chitsiru.
12 Le lieu de notre Sanctuaire est un trône de gloire, un lieu haut élevé dès le commencement.
Nyumba yathu yopemphereramo ili ngati mpando waufumu waulemerero wokhazikitsidwa pa phiri lalitali chiyambire.
13 Eternel, qui es l'attente d'Israël, tous ceux qui t'abandonnent seront honteux; ceux qui se détournent de moi, seront écrits en la terre, parce qu'ils ont délaissé la source des eaux vives, l'Eternel.
Inu Yehova, chiyembekezo cha Israeli, onse amene amakusiyani adzachita manyazi. Iwo amene amakufulatirani mayina awo adzafafanizika ngati olembedwa pa fumbi chifukwa anakana Yehova, kasupe wa madzi amoyo.
14 Eternel, guéris-moi, et je serai guéri; sauve-moi, et je serai sauvé; car tu es ma louange.
Inu Yehova, chiritseni, ndipo ndidzachira; pulumutseni ndipo ndidzapulumuka, chifukwa ndinu amene ndimakutamandani.
15 Voici, ceux-ci me disent: où est la parole de l'Eternel? qu'elle vienne présentement!
Anthu akumandinena kuti, “Mawu a Yehova ali kuti? Zichitiketu lero kuti tizione!”
16 Mais je ne me suis point avancé plus qu'un pasteur après toi, et je n'ai point désiré le jour de l'extrême affliction, tu le sais; et ce qui est sorti de mes lèvres a été devant toi.
Ine sindinakuwumirizeni kuti muwalange. Mukudziwa kuti ine sindilakalaka tsiku la tsoka. Zonse zimene ndinayankhula Inu mukuzidziwa.
17 Ne me sois point en effroi, tu es ma retraite au jour du mal.
Musandichititse mantha; ndinu pothawira panga pa tsiku la mavuto.
18 Que ceux qui me persécutent soient honteux, mais que je ne sois point honteux; qu'ils soient épouvantés, mais que je ne sois point épouvanté; amène sur eux le jour du mal, et les accable d'une double plaie.
Ondizunza anga achite manyazi, koma musandichititse manyazi; iwo achite mantha kwambiri, koma ine mundichotsere manthawo. Tsiku la mavuto liwafikire; ndipo muwawononge kotheratu.
19 Ainsi m'a dit l'Eternel: va, et tiens-toi debout à la porte des enfants du peuple, par laquelle les Rois de Juda entrent, et par laquelle ils sortent; et à toutes les portes de Jérusalem.
Yehova anandiwuza kuti, “Pita ukayime pa chipata chodzerapo anthu, chimene mafumu a ku Yuda amalowerapo ndi kutulukirapo. Ukayimenso pa zipata zina zonse za Yerusalemu.
20 Et leur dis: écoutez la parole de l'Eternel, Rois de Juda, et vous tous [hommes] de Juda, et vous tous habitants de Jérusalem qui entrez par ces portes;
Ukawawuze kuti, ‘Imvani mawu a Yehova, inu mafumu onse a ku Yuda ndi anthu onse a ku Yuda ndi inu nonse okhala mu Yerusalemu amene mumatulukira pa zipata izi.’
21 Ainsi a dit l'Eternel: prenez garde à vos âmes, et ne portez aucun fardeau le jour du Sabbat, et ne les faites point passer par les portes de Jérusalem.
Yehova akuti: samalani kuti pa tsiku la Sabata musanyamule katundu kapena kulowa naye pa zipata za Yerusalemu.
22 Et ne tirez point hors de vos maisons aucun fardeau le jour du Sabbat, et ne faites aucune œuvre, mais sanctifiez le jour du Sabbat, comme j'ai commandé à vos pères.
Musalowetse katundu mʼnyumba zanu kapena kugwira ntchito pa tsiku la Sabata, koma mulipatule tsiku la Sabatalo, monga ndinalamulira makolo anu.
23 Mais ils n'ont point écouté, et n'ont point incliné leur oreille, mais ils ont raidi leur cou, pour n'écouter point, et pour ne recevoir point d'instruction.
Komatu iwo sanandimvere kapena kulabadira. Ndi mitima yawo yowumayo sanamvere kapena kulandira malangizo anga.
24 Il arrivera donc si vous m'écoutez attentivement, dit l'Eternel pour ne faire passer aucun fardeau par les portes de cette ville le jour du Sabbat, et si vous sanctifiez le jour du Sabbat, tellement que vous ne fassiez aucune œuvre en ce jour-là;
Yehova akuti, ‘Muzimvera Ine ndi kuleka kulowetsa kapena kutulutsa katundu pa zipata za mzinda pa tsiku la Sabata. Muzisunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika posachita ntchito iliyonse pa tsikuli.
25 Que les Rois et les principaux, ceux qui sont assis sur le trône de David, montés sur des chariots et sur des chevaux, eux et les principaux d'entre eux, les hommes de Juda, et les habitants de Jérusalem, entreront par les portes de cette ville; et cette ville sera habitée à toujours.
Mukatero ndiye mafumu anu amene akukhala pa mpando wa Davide adzatulukira pa zipata za mzindawu pamodzi ndi nduna zawo. Iwo pamodzi ndi nduna zawo azidzalowa atakwera magaleta ndi akavalo, akuperekezedwa ndi anthu a ku Yuda ndi amene amakhala mu Yerusalemu, ndipo mu mzinda muno mudzakhala anthu mpaka muyaya.
26 On viendra aussi des villes de Juda, et des environs de Jérusalem et du pays de Benjamin, et de la campagne, et des montagnes, et de devers le Midi, et on apportera des holocaustes, des sacrifices, des oblations et de l'encens; on apportera aussi [des sacrifices] d'action de grâces en la maison de l'Eternel.
Anthu adzabwera kuchokera ku mizinda ya Yuda ndi ku midzi yozungulira Yerusalemu, kuchokera ku dziko la Benjamini ndi ku mapiri a kumadzulo, kuchokera ku dziko la mapiri ndi ku Negevi. Adzabwera ndi nsembe zopsereza, nsembe zaufa ndi za chakudya, nsembe za lubani ndi zopereka zachiyamiko ku nyumba ya Yehova.
27 Mais si vous ne m'écoutez point pour sanctifier le jour du Sabbat, et pour ne porter aucun fardeau, et n'en faire entrer aucun par les portes de Jérusalem le jour du Sabbat, je mettrai le feu à ses portes, il consumera les palais de Jérusalem, et ne sera point éteint.
Koma ngati simundimvera; mukapanda kusunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika ndi kumanyamula katundu nʼkumalowa naye pa zipata za Yerusalemu pa tsikuli, Ine ndidzabutsa moto pa zipata za Yerusalemu. Moto umenewo udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu ndipo moto wake sudzazima.’”

< Jérémie 17 >