< Isaïe 41 >

1 Iles, faites-moi silence, et que les peuples prennent de nouvelles forces; qu'ils approchent, et qu'alors ils parlent; allons ensemble en jugement.
“Khalani chete pamaso panga, inu mayiko a mʼmbali mwa nyanja! Alekeni ayandikire ndi kuyankhula; tiyeni tikhale pamodzi kuti atiweruze.
2 Qui est celui qui a fait lever de l'Orient la justice? qui l'a appelée afin qu'elle le suivit pas à pas? qui a soumis à son commandement les nations, lui a fait avoir domination sur les Rois, et les a livrés à son épée, comme de la poussière; et à son arc, comme de la paille poussée par le vent?
“Ndani anadzutsa wochokera kummawa uja amene ananka napambana kulikonse kumene ankapita? Iye amapereka anthu a mitundu ina mʼmanja mwake ndipo ndi lupanga lake anagonjetsa ndi kusandutsa mafumu kukhala ngati fumbi nawamwaza ngati mankhusu ndi uta wake.
3 Il les a poursuivis, et il est passé en paix par le chemin auquel il n'était point entré de ses pieds.
Amawalondola namayenda mosavutika, mʼnjira imene mapazi ake sanayendemo kale.
4 Qui est celui qui a opéré et fait ces choses? c'est celui qui a appelé les âges dès le commencement. Moi l'Eternel je suis le premier, et je suis avec les derniers.
Ndani anachita zimenezi ndi kuzitsiriza, si uja amene anayambitsa mitundu ya anthu? Ine Yehova, ndine chiyambi ndipo potsiriza pake ndidzakhalapo.”
5 Les Iles ont vu, et ont eu crainte, les bouts de la terre ont été effrayés, ils se sont approchés et sont venus.
Mayiko amʼmbali mwa nyanja aona zimenezi ndipo akuopa; anthu a ku mathero a dziko lapansi akunjenjemera. Akuyandikira pafupi, akubwera;
6 Chacun a aidé à son prochain, et a dit à son frère; fortifie-toi.
aliyense akuthandiza mnzake ndipo akuwuza mʼbale wake kuti, “Limba mtima!”
7 L'ouvrier a encouragé le fondeur; celui qui frappe doucement du marteau [encourage] celui qui frappe sur l'enclume, et dit; Cela est bon pour souder, puis il le fait tenir avec des clous, afin qu'il ne bouge point.
Mʼmisiri wa matabwa amalimbikitsa mʼmisiri wa golide, ndipo iye amene amasalaza fano ndi nyundo amalimbikitsa amene amalisanja pa chipala. Ponena za kuwotcherera iye amati, “Zili bwino.” Iye amalikhomerera fanolo ndi misomali kuti lisagwe.
8 Mais toi, Israël, tu es mon serviteur, et toi, Jacob, tu es celui que j'ai élu, la race d'Abraham qui m'a aimé.
“Koma Iwe Israeli mtumiki wanga, Yakobo amene ndakusankha, Ndiwe chidzukulu cha Abrahamu bwenzi langa.
9 Car je t'ai pris des bouts de la terre, je t'ai appelé, en te préférant aux plus excellents qui sont en elle, et je t'ai dit; C'est toi qui es mon serviteur, je t'ai élu, et je ne t'ai point rejeté.
Ndinakutengani kuchokera ku mapeto a dziko lapansi, ndinakuyitanani kuchokera ku mbali za kutali za dziko lapansi. Ine ndinati, ‘Iwe ndiwe mtumiki wanga;’ Ndinakusankha ndipo sindinakutaye.
10 Ne crains point, car je suis avec toi; ne sois point étonné, car je suis ton Dieu; je t'ai fortifié, et je t'ai aidé, même je t'ai maintenu par la dextre de ma justice.
Tsono usaope, pakuti Ine ndili nawe; usataye mtima chifukwa Ine ndine Mulungu wako. Ndidzakupatsa mphamvu ndipo ndidzakuthandiza, ndidzakutchinjiriza ndi dzanja langa lamanja logonjetsa.
11 Voici, tous ceux qui sont indignés contre toi seront honteux et confus; ils seront réduits à néant, et les hommes qui ont querelle avec toi périront.
“Onse amene akupsera mtima adzachita manyazi ndithu ndi kunyazitsidwa; onse amene akukangana nawe sadzakhalanso kanthu, adzawonongeka.
12 Tu chercheras les hommes qui ont querelle avec toi, et tu ne les trouveras point; ils seront réduits à néant; et ceux qui te font la guerre, seront comme ce qui n'est plus.
Udzafunafuna adani ako, koma sadzapezeka. Iwo amene akuchita nawe nkhondo sadzakhalanso kanthu.
13 Car je suis l'Eternel ton Dieu, soutenant ta main droite, celui qui te dis; ne crains point, c'est moi qui t'ai aidé.
Pakuti Ine Yehova, ndine Mulungu wako, amene ndikukugwira dzanja lako lamanja ndipo ndikuti, usaope; ndidzakuthandiza.
14 Ne crains point, vermisseau de Jacob, hommes [mortels] d'Israël; je t'aiderai dit l'Eternel, et ton défenseur c'est le Saint d'Israël.
Usachite mantha, iwe Yakobo wofowoka ngati nyongolotsi, iwe wochepa mphamvu Israeli, chifukwa Ine ndidzakuthandiza,” akutero Yehova Mpulumutsi wako, Woyerayo wa Israeli.
15 Voici, je te ferai être comme une herse pointue toute neuve, ayant des dents; tu fouleras les montagnes et les menuiseras, et tu rendras les coteaux semblables à de la balle.
“Taona, ndidzakusandutsa ngati chipangizo chopunthira tirigu chatsopano, chakunthwa ndi cha mano ambiri. Udzanyenya mapiri ndi kuwaphwanyaphwanya, ndipo zitunda adzazisandutsa ngati mankhusu.
16 Tu les vanneras, et le vent les emportera, et le tourbillon les dispersera; mais tu t'égayeras en l'Eternel, tu te glorifieras au Saint d'Israël.
Udzawapeta ndipo adzawuluka ndi mphepo komanso adzamwazika ndi kamvuluvulu. Koma iwe udzakondwera chifukwa Ine ndine Mulungu wako, ndipo udzanyadira chifukwa cha Ine Woyerayo wa Israeli:
17 Quant aux affligés et aux misérables qui cherchent des eaux, et n'en ont point, la langue desquels est tellement altérée qu'elle n'en peut plus, moi l'Eternel je les exaucerai; moi le Dieu d'Israël je ne les abandonnerai point.
“Pamene amphawi ndi osauka akufunafuna madzi, koma sakuwapeza; ndipo kummero kwawo kwawuma ndi ludzu. Ine Yehova ndidzayankha pemphero lawo; Ine, Mulungu wa Israeli, sindidzawasiya.
18 Je ferai sourdre des fleuves dans les lieux haut élevés, et des fontaines au milieu des vallées; je réduirai le désert en des étangs d'eaux, et la terre sèche en des sources d'eaux.
Ndidzayendetsa mitsinje mʼmalo owuma, ndi akasupe adzatumphuka mu zigwa. Ndidzasandutsa chipululu kukhala dziwe la madzi ndipo dziko lowuma kukhala akasupe a madzi.
19 Je ferai croître au désert le cèdre, le pin, le myrte, et l'olivier; je mettrai aux landes le sapin, l'orme et le buis ensemble.
Mʼchipululu ndidzameretsa mkungudza, kasiya mchisu ndi mtengo wa Olivi. Mʼdziko lowuma ndidzaza mitengo ya payini, ya mkuyu ndi ya mlombwa,
20 Afin qu'on voie, qu'on sache, qu'on pense, et qu'on entende pareillement que la main de l'Eternel a fait cela, et que le Saint d'Israël a créé cela.
kuti anthu aone ndi kudziwa; inde, alingalire ndi kumvetsa, kuti Yehova ndiye wachita zimenezi; kuti Woyera wa Israeli ndiye anakonza zimenezi.
21 Produisez votre procès, dit l'Eternel; et mettez en avant les fondements de votre cause, dit le Roi de Jacob.
“Yehova akuwuza milungu ina kuti, ‘Fotokozani mlandu wanu.’ Mfumu ya Yakobo ikuti, ‘Perekani umboni wanu.’
22 Qu'on les amène, et qu'ils nous déclarent les choses qui arriveront; déclarez-nous que veulent dire les choses qui ont été auparavant, et nous y prendrons garde; et nous saurons leur issue; ou faites-nous entendre ce qui est prêt à arriver.
Bwerani ndi milungu yanu kuti idzatiwuze zomwe zidzachitike mʼtsogolo. Tifotokozereni zinthu zamakedzana tiziganizire ndi kudziwa zotsatira zake. Kapena tiwuzeni zimene zidzachitike mʼtsogolo,
23 Déclarez les choses qui doivent arriver ci-après; et nous saurons que vous êtes dieux; faites aussi du bien ou du mal, et nous en serons tout étonnés; puis nous regarderons ensemble.
tiwuzeni kuti kutsogolo kuli zotani, ndipo ife tidziwa kuti ndinu milungu. Chitani chinthu chabwino kapena choyipa, ndipo mutidabwitsa ndi kutichititsa mantha.
24 Voici, vous êtes de rien, et ce que vous faites est inutile; celui qui vous choisit n'est qu'abomination.
Koma inu sindinu kanthu ndipo zochita zanu nʼzopandapake; amene amapembedza inu ali ngati chinthu chokanidwa chifukwa ndi choyipa.
25 Je l'ai suscité d'Aquilon, et il viendra; il réclamera mon Nom de devers le soleil levant, et marchera sur les Magistrats, comme sur le mortier, et les foulera, comme le potier foule la boue.
“Ndinawutsa munthu wina kumpoto ndipo anabwera, munthu wochokera kummawa amene ndinamuyitana. Amapondaponda olamulira ngati matope, ngati ndi wowumba mbiya amene akuponda dongo.
26 Qui est celui qui a manifesté ces choses dès le commencement, afin que nous le connaissions, et avant le temps où nous sommes, et nous dirons qu'il est juste? mais il n'y a personne qui les annonce, même il n'y a personne qui les donne à entendre, même il n'y a personne qui entende vos paroles.
Ndani anawululiratu zimenezi poyamba pomwe, kuti ife tidziwe, kapena kutiwuziratu zisanachitike kuti ife tinene kuti, ‘Analondola?’ Palibe amene ananena, palibe analengeza zimenezi, palibe anamva mawu anu.
27 Le premier sera pour Sion, [disant]; voici, les voici; et je donnerai quelqu'un à Jérusalem qui annoncera de bonnes nouvelles.
Ine ndinali woyamba kumuwuza Ziyoni kuti, ‘Taona, si awa akubwera apawa!’ Ndinatumiza mthenga wa nkhani yabwino ku Yerusalemu.
28 J'ai regardé, et il n'y avait point d'homme [notable]; même entre ceux-là, et il n'y avait aucun homme de conseil; je les ai aussi interrogés, afin qu'ils répondissent quelque chose.
Koma ndikayangʼana palibe ndi mmodzi yemwe, palibe ndi mmodzi yemwe pakati pawo wotha kupereka uphungu, palibe woti ayankhe pamene ine ndawafunsa.
29 Voici, quant à eux tous, leurs œuvres ne sont que vanité, une chose de néant; leurs idoles de fonte sont du vent et de la confusion.
Taonani, milungu yonseyi ndi yachinyengo! Zochita zawo si kanthu konse; mafano awo ali ngati mphepo yachabechabe.

< Isaïe 41 >