< Ézéchiel 39 >

1 Toi donc, fils d'homme, prophétise contre Gog, et dis: ainsi a dit le Seigneur l'Eternel: voici, j'en veux à toi, Gog, Prince des chefs de Mésec et de Tubal.
“Iwe mwana wa munthu, nenera modzudzula Gogi ndi kumuwuza kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa Mesaki ndi Tubala.
2 Et je te ferai retourner en arrière, n'en laissant que de six l'un, après t'avoir fait monter du fond de l'Aquilon, et t'avoir fait venir sur les montagnes d'Israël.
Ine ndidzakuzunguza ndi kukupirikitsira kutsogolo. Ndidzakutenga kuchokera kutali kumpoto ndi kukutumiza kuti ukalimbane ndi anthu a ku mapiri a Israeli.
3 Car je romprai ton arc dans ta main gauche, et je ferai tomber tes flèches de ta main droite.
Kenaka Ine ndidzathyola uta wa mʼdzanja lako lamanzere ndipo ndidzagwetsa mivi ya mʼdzanja lako lamanja.
4 Tu tomberas sur les montagnes d'Israël, toi et toutes tes troupes, et les peuples qui seront avec toi; je t'ai livré aux oiseaux de proie entre tous les oiseaux, et aux bêtes des champs, pour en être dévoré.
Udzagwa ku mapiri a ku Israeli, iwe ndi magulu ako onse ankhondo ndiponso mitundu ya anthu imene ili nawe. Ndidzakusandutsa chakudya cha mitundu yonse ya mbalame zodya nyama, ndiponso cha zirombo zakuthengo.
5 Tu tomberas sur le dessus des champs, parce que j'ai parlé, dit le Seigneur l'Eternel.
Udzafera pa mtetete kuthengo, pakuti Ine ndayankhula. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
6 Et je mettrai le feu en Magog, et parmi ceux qui demeurent en assurance dans les Iles; et ils sauront que je suis l'Eternel.
Ndidzatumiza moto pa Magogi ndi pa onse amene amakhala mwamtendere mʼmbali mwa nyanja. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’
7 Et je ferai connaître le Nom de ma Sainteté au milieu de mon peuple d'Israël; et je ne profanerai plus le Nom de ma Sainteté; les nations sauront que je suis l'Eternel, le Saint en Israël.
“Ndidzachititsa kuti dzina langa loyera lidziwike pakati pa anthu anga Israeli. Sindidzalola kuti dzina langa liyipitsidwenso, ndipo mitundu ya anthu idzadziwa kuti Ine Yehova ndine Woyera mu Israeli.
8 Voici cela est arrivé, et a été fait, dit le Seigneur l'Eternel; c'est ici la journée dont j'ai parlé.
Zikubwera! Ndipo zidzachitikadi, ndikutero Ine Ambuye Yehova. Ndiye tsiku limene ndinanena lija.
9 Et les habitants des villes d'Israël sortiront, et allumeront le feu, et brûleront les armes, les boucliers, les écus, les arcs, les flèches, les bâtons qu'on lance de la main, et les javelots, et ils y tiendront le feu allumé sept ans durant.
“Pamenepo okhala mʼmizinda ya Israeli adzatuluka ndipo adzasonkhanitsa zida zankhondo kuti zikhale nkhuni ndipo adzazitentha; zishango ndi lihawo, mauta ndi mivi, zibonga za nkhondo ndi mikondo. Adzazisonkhera moto kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
10 Et on n'apportera point de bois des champs, et on n'en coupera point des forêts, parce qu'ils feront du feu de ces armes, lorsqu'ils butineront ceux qui les avaient butinés, et qu'ils pilleront ceux qui les avaient pillés, dit le Seigneur l'Eternel.
Iwo sadzatolera nkhuni kuthengo kapena kukadula ku nkhalango, chifukwa adzasonkhera moto zidazo. Ndipo iwo adzafunkha amene anawafunkhawo, ndi kulanda chuma cha amene anawalanda, ndikutero Ine Ambuye Yehova.
11 Et il arrivera en ce jour-là que je donnerai à Gog dans ces quartiers-là un lieu pour sépulcre en Israël, savoir la vallée des passants, qui est au devant de la mer, et d'étonnement elle réduira les passants au silence; on enterrera là Gog, et toute la multitude de son peuple, et on l'appellera, la vallée d'Hammon-Gog.
“Pa tsiku limenelo ndidzamupatsa Gogi manda mu Israeli, mʼchigwa cha apaulendo, kummawa kwa Nyanja Yakufa. Mandawo adzatseka njira ya apaulendo, chifukwa Gogi ndi gulu lake lankhondo adzayikidwa kumeneko. Ndipo chigwacho chidzatchedwa chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
12 Et ceux de la maison d'Israël les enterreront pendant l'espace de sept mois pour purifier le pays.
“Nyumba ya Israeli idzakhala ikukwirira mitembo kwa miyezi isanu ndi iwiri ndi cholinga choyeretsa dziko.
13 Tout le peuple, dis-je, du pays les enterrera, et cela leur sera un nom, [savoir] le jour auquel j'aurai été glorifié, dit le Seigneur l'Eternel.
Anthu onse a mʼdzikomo adzakwirira nawo mitembo. Ntchito imeneyo adzatchuka nayo pa tsiku limene ndidzaonetsa ulemerero wanga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
14 Et ils mettront à part des gens qui ne feront autre chose que parcourir le pays, lesquels avec les passants enterreront ceux qui seront demeurés de reste sur le dessus de la terre, pour la purifier, [et] ils en chercheront jusques au bout de sept mois.
“Patapita miyezi isanu ndi iwiri adzalemba ntchito anthu ena odzayenda mʼdziko lonse kufunafuna mitembo imene inatsalira nʼkumayikwirira. Choncho adzayeretseratu dzikolo.
15 Et ces passants-là iront par le pays, et celui qui verra l'os d'un homme, dressera auprès de lui un signal; jusqu'à ce que les enterreurs l'aient enterré dans la vallée d'Hammon-Gog.
Poyenda mʼdzikomo azidzati akaona fupa la munthu azidzayikapo chizindikiro pambali pake mpaka okumba manda atakalikwirira fupalo ku chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
16 Et aussi le nom de la ville sera Hamona, et on nettoiera le pays.
(Komwekonso kudzakhala mzinda wotchedwa Gulu la nkhondo). Ndipo potero adzayeretsa dziko.
17 Toi donc, fils d'homme, ainsi a dit le Seigneur l'Eternel: dis aux oiseaux de toutes espèces, et à toutes les bêtes des champs: assemblez-vous et venez; amassez-vous de toutes parts vers mon sacrifice que je fais pour vous, [qui] est un grand sacrifice sur les montagnes d'Israël, vous mangerez de la chair, et vous boirez du sang.
“Tsono iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Itana mbalame za mitundu yonse ndi zirombo zonse zakuthengo ndipo uziwuze kuti, ‘Sonkhanani ndipo bwerani kuchokera ku mbali zonse ku nsembe imene ndikukonzerani inu, nsembe yayikulu pa mapiri a Israeli. Kumeneko inu mudzadya mnofu ndi kumwa magazi.
18 Vous mangerez la chair des [hommes] forts, et vous boirez le sang des principaux de la terre, le sang des moutons, des agneaux, des boucs; et des veaux, tous grasses bêtes de Basan.
Mudzadya mnofu wa anthu ankhondo amphamvu ndi kumwa magazi a akalonga a dziko lapansi. Onsewo anaphedwa ngati nkhosa zazimuna, ana ankhosa onenepa, mbuzi ndiponso ngati ngʼombe zazimuna zonenepa za ku Basani.
19 Vous mangerez de la graisse jusques à en être rassasiés, et vous boirez au sang jusqu'à en être ivres, [de la graisse, dis-je, et du sang] de mon sacrifice, que j'aurai sacrifié pour vous.
Ku phwando lansembe limene ndikukonzera inulo, mudzadya zonona mpaka kukhuta ndi kumwa magazi mpaka kuledzera.
20 Et vous serez rassasiés à ma table, de chevaux, et de bêtes d'attelage, d'hommes forts, et de tous hommes de guerre, dit le Seigneur l'Eternel.
Pa tebulo langa mudzakhuta pakudya akavalo ndi okwerapo ake, anthu amphamvu ndi asilikali amitundumitundu,’ ndikutero Ine Ambuye Yehova.
21 Et je mettrai ma gloire entre les nations, et toutes les nations verront mon jugement que j'aurai exercé, et comment j'aurai mis ma main sur eux.
“Ine ndidzaonetsa ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina, ndipo adzaona mmene ndidzawalangire ndikadzayika dzanja langa pa iwo.
22 Et la maison d'Israël connaîtra dès ce jour-là, et dans la suite, que je suis l'Eternel leur Dieu.
Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo Aisraeli adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.
23 Et les nations sauront que la maison d'Israël avait été transportée en captivité à cause de son iniquité, parce qu'ils avaient péché contre moi, et que je leur avais caché ma face, et les avais livrés entre les mains de leurs ennemis, tellement qu'ils étaient tous tombés par l'épée.
Ndipo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti anthu a Israeli anatengedwa ukapolo chifukwa cha tchimo lawo, chifukwa anali osakhulupirika kwa Ine. Choncho Ine ndinawabisira nkhope yanga ndi kuwapereka kwa adani awo. Motero anaphedwa pa nkhondo.
24 Je leur avais fait selon leur souillure, et selon leur crime, et je leur avais caché ma face.
Ndinawachita zimenezi chifukwa cha kunyansa kwawo ndi zolakwa zawo, ndipo ndinawabisira nkhope yanga.
25 C'est pourquoi ainsi a dit le Seigneur l'Eternel: maintenant je ramènerai la captivité de Jacob, et j'aurai pitié de toute la maison d'Israël, et je serai jaloux du Nom de ma Sainteté.
“Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsopano ndidzakhazikanso pa bwino banja la Yakobo. Ndidzachitira chifundo Aisraeli onse, ndipo ndidzateteza dzina langa loyera.
26 Après qu'ils auront porté leur ignominie, et tout leur crime, par lequel ils avaient péché contre moi, quand ils demeuraient en sûreté dans leur terre, et sans qu'il y eût personne qui les épouvantât.
Anthuwo akadzakhala mwamtendere mʼdziko lawo popanda wina wowaopseza, pamenepo adzayiwala zamanyazi zawo zimene zinawachitikira chifukwa chosandikhulupirira Ine.
27 Parce que je les ramènerai d'entre les peuples, que je les rassemblerai des pays de leurs ennemis, et que je serai sanctifié en eux, en la présence de plusieurs nations.
Ndidzawabwezeranso kwawo kuchokera pakati pa anthu a mitundu ina ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko a adani awo. Poteropo ndidzaonetsa pamaso pa anthu a mitundu yambiri kuti ndine Woyera.
28 Et ils sauront que je suis l'Eternel leur Dieu, lorsqu'après les avoir transportés entre les nations, je les aurai rassemblés en leur terre, et que je n'en aurai laissé demeurer là aucun de reste.
Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo, ngakhale kuti ndinawapereka ku ukapolo pakati pa anthu a mitundu ina. Ine ndidzawasonkhanitsanso ku dziko lawo osasiyako wina mʼmbuyo.
29 Et je ne leur cacherai plus ma face, depuis que j'aurai répandu mon Esprit sur la maison d'Israël, dit le Seigneur l'Eternel.
Ine sindidzawabisiranso nkhope yanga, pakuti ndidzathira Mzimu wanga pa Aisraeli. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”

< Ézéchiel 39 >