< Ézéchiel 32 >

1 Il arriva aussi en la douzième année, le premier jour du douzième mois, que la parole de l'Eternel me fut [adressée], en disant:
Pa tsiku loyamba la mwezi wa khumi ndi chiwiri, chaka chakhumi ndi chiwiri, Yehova anandiyankhula kuti:
2 Fils d'homme, prononce à haute voix une complainte sur Pharaon Roi d'Egypte, et lui dis: tu as été entre les nations semblable à un lionceau, et tel qu'un grand poisson dans les mers; tu t'élançais dans tes fleuves, et tu troublais les eaux avec tes pieds, et remplissais de bourbe leurs fleuves.
“Iwe mwana wa munthu imba nyimbo ya maliro a Farao mfumu ya Igupto ndipo uyiwuze kuti, “Iwe umadziyesa ngati mkango pakati pa mitundu ya anthu. Koma iwe uli ngati ngʼona mʼnyanja. Umakhuvula mʼmitsinje yako, kuvundula madzi ndi mapazi ako ndi kudetsa madzi mʼmitsinje.
3 Ainsi a dit le Seigneur l'Eternel: j'étendrai mon rets sur toi par un amas de plusieurs peuples, qui te tireront étant dans mes filets.
“Tsono Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Pogwiritsa ntchito gulu la anthu a mitundu yambiri, ndidzakuponyera khoka langa ndi kukugwira mu ukonde wanga.
4 Et je te laisserai à l'abandon sur la terre; je te jetterai sur le dessus des champs, et je ferai demeurer sur toi tous les oiseaux des cieux, et rassasierai de toi les bêtes de toute la terre.
Ndidzakuponya ku mtunda ndi kukutayira pansi. Ndidzabweretsa mbalame zamumlengalenga kuti zidzatere pa iwe, ndipo zirombo zonse za dziko lapansi zidzakudya.
5 Car je mettrai ta chair sur les montagnes, et je remplirai tes vallées des débris de tes hauteurs.
Ndidzayanika mnofu wako pa mapiri ndipo zigwa zidzadzaza ndi zotsalira zako.
6 Et j'arroserai de ton sang jusques aux montagnes, la terre où tu nages, et les lits des eaux seront remplis de toi.
Ndidzanyowetsa dziko ndi magazi ako, mpaka kumapiri komwe, ndipo mitsinje idzadzaza ndi mnofu wako.
7 Et quand je t'aurai éteint, je couvrirai les cieux, et ferai obscurcir leurs étoiles, je couvrirai le soleil de nuages, et la lune ne donnera plus sa lumière.
Ndikadzakuwononga, ndidzaphimba miyamba ndikudetsa nyenyezi zake. Ndidzaphimba dzuwa ndi mtambo, ndipo mwezi sudzawala.
8 Je ferai obscurcir sur toi tous les luminaires qui donnent la lumière dans les cieux, et je répandrai les ténèbres sur ton pays, dit le Seigneur l'Eternel.
Zowala zonse zamumlengalenga ndidzazizimitsa; ndidzachititsa mdima pa dziko lako, akutero Ambuye Yehova.
9 Et je ferai que le cœur de plusieurs peuples frémira, quand j'aurai fait venir [la nouvelle de] ta plaie parmi les nations, en des pays que tu n'as point connus.
Ndidzasautsa mitima ya anthu a mitundu yambiri pamene ndidzakupititsa ku ukapolo pakati pa mitundu ya anthu, ku mayiko amene iwe sunawadziwe.
10 Et je remplirai d'étonnement plusieurs peuples à cause de toi, et leurs Rois seront tout épouvantés à cause de toi, quand je ferai luire mon épée à leurs yeux; et ils seront effrayés de moment en moment, chacun dans soi-même, au jour de ta ruine.
Ine ndidzachititsa kuti anthu a mitundu yambiri adabwe nawe, ndipo mafumu awo adzanjenjemera ndi mantha aakulu chifukwa cha iwe pamene ndidzaonetsa lupanga langa pamaso pawo. Pa nthawi ya kugwa kwako, aliyense wa iwo adzanjenjemera moyo wake wonse.
11 Car ainsi a dit le Seigneur l'Eternel: l'épée du Roi de Babylone viendra sur toi.
“‘Pakuti ndikunena Ine Ambuye Yehova kuti, “‘Lupanga la mfumu ya ku Babuloni lidzabwera kudzalimbana nawe.
12 J'abattrai ta multitude par les épées des hommes forts, qui tous sont les plus terribles d'entre les nations; et ils détruiront l'orgueil de l'Egypte, et toute la multitude de son peuple sera ruinée.
Ndidzachititsa gulu lako lankhondo kuti ligwe ndi lupanga la anthu amphamvu, anthu ankhanza kwambiri pakati pa mitundu yonse ya anthu. Adzathetsa kunyada kwa Igupto, ndipo gulu lake lonse la nkhondo lidzagonjetsedwa.
13 Et je ferai périr tout son bétail d'auprès des grosses eaux, et aucun pied d'homme ne les troublera plus, ni aucun pied de bête ne les agitera plus.
Ndidzawononga ziweto zake zonse zokhala mʼmbali mwa madzi ambiri. Ku madziko sikudzaonekanso phazi la munthu kapena kudetsedwa ndi phazi la ziweto.
14 Alors je rendrai profondes leurs eaux, et je ferai couler leurs fleuves comme de l'huile, dit le Seigneur l'Eternel.
Pambuyo pake ndidzayeretsa madzi ake ndipo mitsinje yake idzayenda mokometsera ngati mafuta, akutero Ambuye Yehova.
15 Quand j'aurai réduit le pays d'Egypte en désolation, et que le pays aura été dénué des choses dont il était rempli; quand j'aurai frappé tous ceux qui y habitent, ils sauront alors que je suis l'Eternel.
Ndikadzasandutsa dziko la Igupto kukhala bwinja; ndikadzawononga dziko lonse ndi kukantha onse okhala kumeneko, adzadziwa kuti ndine Yehova.’
16 C'est ici la complainte qu'on fera sur elle, les filles des nations feront cette complainte sur elle; elles feront, dis-je, cette complainte sur l'Egypte, et sur toute la multitude de son peuple, dit le Seigneur.
“Mawu angawa adzakhala nyimbo ya maliro. Ana a akazi amitundu ya anthu adzayimba, kuyimbira Igupto ndi gulu lake lonse la nkhondo, akutero Ambuye Yehova.”
17 Il arriva aussi en la douzième année, le quinzième jour du mois, que la parole de l'Eternel me fut [adressée], en disant:
Pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, chaka cha khumi ndi chiwiri, Yehova anayankhula kuti:
18 Fils d'homme, dresse une lamentation sur la multitude d'Egypte, et fais-la descendre, elle et les filles des nations magnifiques, aux plus bas lieux de la terre, avec ceux qui descendent en la fosse.
“Iwe mwana wa munthu, lirira gulu lankhondo la Igupto ndipo uwalowetse pamodzi ndi anthu ena amphamvu a mayiko ena ku dziko la anthu akufa.
19 Par dessus qui [m']aurais-tu été agréable? descends, et sois gisante avec les incirconcis.
Ufunse kuti, ‘Ndani amene akukuposa kukongola? Tsikirani ku manda ndi kukhala pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe.’
20 Ils tomberont au milieu de ceux qui auront été tués par l'épée; l'épée a [déjà] été donnée; traînez-la avec toute la multitude de son peuple.
Aigupto adzagwa pakati pa amene akuphedwa ndi lupanga. Lupanga ndi losololedwa kale. Iye adzaphedwa pamodzi ndi gulu lake lankhondo.
21 Les plus forts d'entre les puissants lui parleront du milieu du sépulcre, avec ceux qui lui donnaient du secours, et diront: ils sont descendus, ils sont gisants, les incirconcis tués par l'épée. (Sheol h7585)
Mʼkati mwa manda atsogoleri amphamvu pamodzi ndi ogwirizana nawo azidzakambirana za Igupto nʼkumati, ‘Afika kuno anthu osachita mdulidwe aja! Ndi awa agona apawa, ophedwa pa nkhondo.’ (Sheol h7585)
22 Là est l'Assyrien, et toute son assemblée; ses sépulcres sont autour de lui, eux tous, mis à mort, sont tombés par l'épée.
“Asiriya ali komweko ndipo ankhondo ake onse ali mʼmanda omuzungulira. Onsewo anaphedwa pa nkhondo.
23 Car ses sépulcres ont été posés au fond de la fosse, et son assemblée autour de sa sépulture; eux tous qui avaient répandu leur terreur sur la terre des vivants, sont tombés morts par l'épée.
Manda awo ali kumalo ozama a dzenje, ndipo ankhondo ake azungulira manda ake. Onse amene anaopseza dziko la anthu amoyo aphedwa, agwa ndi lupanga.
24 Là est Hélam, et toute sa multitude autour de son sépulcre; eux tous sont tombés morts par l'épée, ils sont descendus incirconcis dans les plus bas lieux de la terre, et après avoir répandu leur terreur sur la terre des vivants, ils ont porté leur ignominie avec ceux qui descendent dans la fosse.
“Elamu ali komweko ndipo ankhondo ake ali mʼmanda omuzungulira. Onsewa anaphedwa pa nkhondo, natsikira ku manda ali osachita mdulidwe. Iwowa kale ankaopseza anthu pa dziko lapansi. Tsopano akuchita manyazi pamodzi ndi amene ali mʼmanda.
25 On a mis sa couche parmi ceux qui ont été tués, avec toute sa multitude; ses sépulcres sont autour de lui; eux tous incirconcis tués par l'épée, quoiqu'ils aient répandu leur terreur sur la terre des vivants, toutefois ils ont porté leur ignominie avec ceux qui descendent en la fosse; il a été mis parmi ceux qui ont été tués.
Amukonzera pogona pakati pa anthu ophedwa, pamodzi ndi gulu lake lonse la nkhondo litazungulira manda ake. Onsewo ndi anthu osachita mdulidwe ophedwa ndi lupanga. Paja anthuwa ankaopsa mʼdziko la anthu a moyo. Koma tsopano akuchita manyazi pamodzi ndi amene ali mʼmanda. Iwo ayikidwa pakati pa anthu ophedwa.
26 Là est Mesec, Tubal, et toute la multitude de leurs gens; leurs sépulcres [sont] autour d'eux; eux tous incirconcis, tués par l'épée, quoiqu'ils aient répandu leur terreur sur la terre des vivants.
“Mesaki ndi Tubala ali komweko, pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo litazungulira manda awo. Onsewo ndi anthu osachita mdulidwe, ophedwa ndi lupanga. Paja ankaopsa mʼdziko la anthu amoyo.
27 Ils n'ont pourtant point été gisants avec les hommes vaillants qui sont tombés d'entre les incirconcis, lesquels sont descendus au sépulcre avec leurs instruments de guerre, dont on a mis les épées sous leurs têtes, et dont les iniquités ont reposé sur leurs os; parce que la terreur des hommes forts est en la terre des vivants. (Sheol h7585)
Iwo sanayikidwe mwaulemu ngati ankhondo amphamvu amakedzana, amene anatsikira ku dziko la anthu akufa ndi zida zawo zomwe za nkhondo. Malupanga awo anawayika ku mitu yawo, ndipo zishango zawo anaphimba mafupa awo. Kale anthu amphamvu amenewa ankaopsa dziko la anthu amoyo. (Sheol h7585)
28 Toi aussi tu seras froissé au milieu des incirconcis, et tu seras gisant avec ceux qui ont été tués par l'épée.
“Iwenso Farao, udzaphwanyidwa ndi kuyikidwa pakati pa anthu osachita mdulidwe, amene anaphedwa ndi lupanga.
29 Là est Edom, ses Rois, et tous ses Princes, qui ont été mis avec leur force parmi ceux qui ont été tués par l'épée; ils seront gisants avec les incirconcis, et avec ceux qui sont descendus dans la fosse.
“Edomu ali kumeneko pamodzi ndi mafumu ake ndi akalonga ake onse. Ngakhale anali amphamvu, koma anayikidwa. Ayikidwa pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje.
30 Là sont tous les Princes de l'Aquilon, et tous les Sidoniens, qui sont descendus avec ceux qui ont été tués, à cause de leur terreur, étant honteux de leur force; et ils sont gisants incirconcis avec ceux qui ont été tués par l'épée, et ils ont porté leur ignominie avec ceux qui sont descendus dans la fosse.
“Akalonga onse akumpoto pamodzi ndi anthu onse a ku Sidoni ali kumeneko. Anatsikira ku dziko la anthu akufa mwamanyazi ngakhale anali owopsa ndi mphamvu zawo. Iwo akugona osachita mdulidwe pamodzi ndi amene anaphedwa ndi lupanga ndipo akuchita manyazi pamodzi ndi iwo amene anatsikira kale ku manda.
31 Pharaon les verra, et il sera consolé de toute la multitude de son peuple; Pharaon, dit le Seigneur l'Eternel a vu les blessés par l'épée et toute son armée.
“Farao ndi gulu lake lankhondo akadzawaona iwowa adzathunza mtima pokumbukira kuchuluka kwa gulu lake lankhondo limene linaphedwa pa nkhondo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
32 Car j'ai mis ma terreur en la terre des vivants, c'est pourquoi Pharaon avec toute la multitude de son peuple sera gisant au milieu des incirconcis, avec ceux qui ont été tués par l'épée, dit le Seigneur l'Eternel.
Paja ankaopsa mʼdziko la anthu amoyo. Koma Faraoyo pamodzi ndi ankhondo ake onse adzayikidwa pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, pamodzi ndi amene anaphedwa pa nkhondo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”

< Ézéchiel 32 >