< Ézéchiel 28 >

1 La parole de l'Eternel me fut encore [adressée], en disant:
Yehova anandiyankhula nati:
2 Fils d'homme, dis au conducteur de Tyr: ainsi a dit le Seigneur l'Eternel: parce que ton cœur s'est élevé et que tu as dit: je suis le [Dieu] Fort, et je suis assis dans le siège de Dieu, au cœur de la mer, quoique tu sois un homme, et non le [Dieu] Fort, et parce que tu as élevé ton cœur comme si tu étais un Dieu.
“Iwe mwana wa munthu, iwuze mfumu ya ku Turo mawu a Ine Ambuye Yehova akuti, “‘Iwe ndi mtima wako wodzikuza umanena kuti, ‘Ine ndine mulungu; ndimakhala pa mpando wa mulungu pakati pa nyanja.’ Koma ndiwe munthu chabe osati mulungu, ngakhale ukuganiza kuti ndiwe wanzeru ngati mulungu.
3 Voici, tu es plus sage que Daniel, rien de caché ne t'a été rendu obscur.
Taona, ndiwedi wanzeru kupambana Danieli. Ndipo palibe chinsinsi chobisika kwa iwe.
4 Tu t'es acquis de la puissance par ta sagesse et par ta prudence; et tu as assemblé de l'or et de l'argent dans tes trésors.
Mwa nzeru zako ndi kumvetsa kwako unadzipezera chuma ndipo unasonkhanitsa golide ndi siliva mʼnyumba zosungira chuma chako.
5 Tu as multiplié ta puissance par la grandeur de ta sagesse dans ton commerce, puis ton cœur s'est élevé à cause de ta puissance.
Ndi nzeru zako zochitira malonda unachulukitsa chuma chako ndipo wayamba kunyada chifukwa cha chuma chakocho.
6 C'est pourquoi le Seigneur l'Eternel dit ainsi: parce que tu as élevé ton cœur, comme si tu étais un Dieu:
“‘Choncho Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Popeza umadziganizira kuti ndiwe mulungu,
7 A cause de cela voici, je m'en vais faire venir contre toi des étrangers les plus terribles d'entre les nations, qui tireront leurs épées sur la beauté de ta sagesse, et souilleront ton lustre.
Ine ndidzabwera ndi anthu achilendo, anthu ankhanza, kuti adzalimbane nawe. Adzakuthira nkhondo kuti awononge zonse zimene unazipeza ndi nzeru zako, ndipo adzawononga kunyada kwakoko.
8 Ils te feront descendre en la fosse, et tu mourras au cœur de la mer, de la mort des blessés à mort.
Iwo adzakuponyera ku dzenje ndipo udzafa imfa yoopsa mʼnyanja yozama.
9 Iras-tu disant devant celui qui te tuera, je suis Dieu? vu que tu [te trouveras] homme, et non le [Dieu] Fort, dans la main de celui qui te blessera mortellement.
Kodi udzanenabe kuti, ‘Ine ndine mulungu,’ pamaso pa iwo amene akukupha? Iwe udzaoneka kuti ndiwe munthu chabe, osati mulungu, mʼmanja mwa iwo amene akukuphawo.
10 Tu mourras de la mort des incirconcis par la main des étrangers; car j'ai parlé, dit le Seigneur l'Eternel.
Udzafa imfa ya anthu osachita mdulidwe mʼmanja mwa anthu achilendo. Ine ndayankhula zimenezi, akutero Ambuye Yehova.’”
11 La parole de l'Eternel me fut encore [adressée], en disant:
Yehova anandiyankhula kuti:
12 Fils d'homme, prononce à haute voix une complainte sur le Roi de Tyr, et lui dis: ainsi a dit le Seigneur l'Eternel: toi à qui rien ne manque, plein de sagesse, et parfait en beauté;
“Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yodandaulira mfumu ya Turo ndipo uyiwuze mawu a Ine Ambuye Yehova akuti, “‘Iwe unali chitsanzo cha ungwiro weniweni, wodzaza ndi nzeru ndi wokongola kwambiri.
13 Tu as été en Héden le jardin de Dieu; ta couverture était de pierres précieuses de toutes sortes, de Sardoine, de Topaze, de Jaspe, de Chrysolithe, d'Onyx, de Béryl, de Saphir, d'Escarboucle, d'Emeraude, et d'or; ce que savaient faire tes tambours et tes flûtes [a été] chez toi; ils ont été tous prêts au jour que tu fus créé.
Iwe unkakhala ngati mu Edeni, munda wa Mulungu. Miyala yokongola ya mitundu yonse: rubi, topazi ndi dayimondi, kirisoliti, onikisi, yasipa, safiro, kalineliyoni ndi berili ndiwo inali zofunda zako. Ndipo zoyikamo miyalayo zinali zagolide. Anakupangira zonsezi pa tsiku limene unalengedwa.
14 Tu [as été] un Chérubin, oint pour servir de protection; je t'avais établi, [et] tu as été dans la sainte montagne de Dieu; tu as marché entre les pierres éclatantes.
Ndinayika kerubi kuti azikulondera. Unkakhala pa phiri langa lopatulika, ndipo unkayendayenda pakati pa miyala ya moto.
15 Tu as été parfait en tes voies dès le jour que tu fus créé, jusqu'à ce que la perversité a été trouvée en toi.
Makhalidwe ako anali abwino kuyambira pamene unalengedwa mpaka nthawi imene unayamba kuchita zoyipa.
16 Selon la grandeur de ton trafic on a rempli le milieu de toi de violence, et tu as péché; c'est pourquoi je te jetterai comme une chose souillée hors de la montagne de Dieu, et je te détruirai d'entre les pierres éclatantes, ô Chérubin! qui sers de protection.
Unatanganidwa ndi zamalonda. Zotsatira zake zinali zoti unachulukitsa zandewu ndi kumachimwa. Choncho ndinakuchotsa ku phiri langa lopatulika. Mkerubi amene ankakulondera uja anakupirikitsa kukuchotsa ku miyala yamoto.
17 Ton cœur s'est élevé à cause de ta beauté, tu as perdu ta sagesse à cause de ton éclat; je t'ai jeté par terre, je t'ai mis en spectacle aux Rois, afin qu'ils te regardent.
Unkadzikuza mu mtima mwako chifukwa cha kukongola kwako, ndipo unayipitsa nzeru zako chifukwa chofuna kutchuka. Kotero Ine ndinakugwetsa pansi kuti ukhala chenjezo pamaso pa mafumu.
18 Tu as profané tes Sanctuaires par la multitude de tes iniquités, en usant mal de ton trafic; et j'ai fait sortir du milieu de toi un feu qui t'a consumé, et je t'ai réduit en cendre sur la terre, en la présence de tous ceux qui te voient.
Ndi malonda ako achinyengo unachulukitsa machimo ako. Motero unayipitsa malo ako achipembedzo. Choncho ndinabutsa moto pakati pako, ndipo unakupsereza, ndipo unasanduka phulusa pa dziko lapansi pamaso pa anthu onse amene amakuona.
19 Tous ceux qui te connaissent entre les peuples ont été désolés à cause de toi; tu es cause qu'on est tout étonné de ce que tu ne seras plus à jamais.
Anthu onse amitundu amene ankakudziwa akuchita mantha chifukwa cha iwe. Watheratu mochititsa mantha ndipo sudzakhalaponso mpaka muyaya.’”
20 Puis la parole de l'Eternel me fut [adressée], en disant:
Yehova anandiyankhula nati:
21 Fils d'homme, tourne ta face vers Sidon, et prophétise contre elle.
“Iwe mwana wa munthu, utembenukire ku mzinda wa Sidoni ndipo unenere mowudzudzula kuti,
22 Et dis: ainsi a dit le Seigneur l'Eternel: voici j'en veux à toi, Sidon, et je serai glorifié au milieu de toi; et on saura que je suis l'Eternel, quand j'aurai exercé des jugements contre elle, et que j'y aurai été sanctifié.
‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndine mdani wako, iwe Sidoni, ndipo ndidzalemekezedwa chifukwa cha iwe. Anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova ndikadzakulanga ndi kudzionetsa kuti ndine woyera pakati pako.
23 J'enverrai donc dans elle la mortalité, et le sang dans ses places, et les blessés à mort tomberont au milieu d'elle par l'épée qui viendra de toutes parts sur elle; et ils sauront que je suis l'Eternel.
Ndidzatumiza mliri pa iwe ndi kuchititsa magazi kuti ayende mʼmisewu yako. Anthu ophedwa ndi lupanga adzagwa mbali zonse. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
24 Et elle ne sera plus une ronce piquante à la maison d'Israël, ni une épine causant plus de douleur qu'aucun de ceux qui sont autour d'eux, et qui les pillent; et ils sauront que je suis le Seigneur l'Eternel.
“‘Nthawi imeneyo Aisraeli sadzakhalanso ndi anthu pafupi achipongwe amene ali ngati nthula zowawa ndi ngati minga zopweteka. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.
25 Ainsi a dit le Seigneur l'Eternel: quand j'aurai rassemblé la maison d'Israël d'entre les peuples parmi lesquels ils auront été dispersés, je serai sanctifié en eux, les nations le voyant, et ils habiteront sur leur terre que j'ai donnée à mon serviteur Jacob.
“‘Ine Ambuye Yehova mawu anga ndi awa: Nditasonkhanitsa Aisraeli kuchoka ku mayiko kumene anamwazikira, ndidzadzionetsa kuti ndine woyera pakati pawo pamaso pa anthu a mitundu ina. Adzakhala mʼdziko lawo, limene ndinalipereka kwa mtumiki wanga Yakobo.
26 Ils y habiteront en sûreté, ils bâtiront des maisons, ils planteront des vignes; ils [y] habiteront, dis-je, en sûreté, lorsque j'aurai exercé des jugements contre ceux qui les auront pillés de toutes parts; et ils sauront que je suis l'Eternel leur Dieu.
Adzakhala kumeneko mwamtendere ndipo adzamanga nyumba ndi kulima minda ya mpesa. Adzakhala kumeneko mwamtendere pamene ndidzalange anthu oyandikana nawo, amene ankawanyoza. Motero iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.’”

< Ézéchiel 28 >