< Amos 8 >

1 Le Seigneur l'Eternel me fit voir cette vision, et voici, un panier de fruits d'Eté.
Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: dengu la zipatso zakupsa.
2 Et il dit: Que vois-tu, Amos? Et je répondis: Un panier de fruits d'Eté. Et l'Eternel me dit: La fin est venue sur mon peuple d'Israël, je ne lui en passerai plus.
Iye anandifunsa kuti, “Amosi nʼchiyani ukuona?” Ine ndinayankha kuti, “Dengu la zipatso zakupsa.” Ndipo Yehova anati kwa ine, “Nthawi yachimaliziro yawakwanira anthu anga Aisraeli; sindidzawakhululukiranso.
3 Les cantiques du Temple seront des hurlements en ce temps-là, dit le Seigneur l'Eternel. Il y aura grand nombre de corps morts que l'on jettera en tous lieux en silence.
“Tsiku limenelo,” Ambuye Yehova akulengeza kuti, “Nyimbo za mʼNyumba ya Mulungu zidzasanduka kulira kofuwula. Mitembo ya anthu idzachuluka, ndipo adzayiponya ponseponse! Kudzangoti zii!”
4 Ecoutez ceci vous qui engloutissez les pauvres, même jusqu'à désoler les affligés du pays;
Imvani izi, inu amene mumapondereza anthu osowa ndipo simulabadira anthu osauka a mʼdzikomu.
5 Et qui dites: Quand sera passé ce mois? et nous débiterons le blé; et [quand sera passé] ce sabbat? et nous mettrons en vente le froment, en faisant l'épha plus petit, augmentant le sicle, et falsifiant les balances pour tromper.
Mumanena kuti, “Kodi chikondwerero cha mwezi watsopano chidzatha liti kuti tigulitse zinthu? Ndipo tsiku la Sabata litha liti kuti tigulitse tirigu, kuti tichepetse miyeso, kukweza mitengo kuti tibere anthu ndi miyeso ya chinyengo,
6 Afin que nous acquérions les chétifs par argent, et le pauvre pour une paire de souliers, et que nous débitions les criblures du froment.
tigule osauka ndi ndalama zasiliva ndi osowa powapatsa nsapato, tigulitse ngakhale mungu wa tirigu?”
7 L'Eternel a juré par la magnificence de Jacob: Si j'oublie jamais aucune de leurs actions!
Yehova amene Yakobo amamunyadira, walumbira kuti: Ine sindidzayiwala chilichonse chimene anachita.
8 La terre ne sera-t-elle point émue d'une telle chose, et tous ses habitants ne lamenteront-ils point? Ne s'écoulera-t-elle pas toute comme un fleuve, et ne sera-t-elle pas emportée et submergée comme par le fleuve d'Egypte?
“Kodi dziko silidzagwedezeka chifukwa cha zimenezi, ndi onse okhala mʼmenemo kulira mwachisoni? Dziko lonse lidzavunduka ngati mtsinje wa Nailo; lidzagwedezeka kenaka nʼkukhala bata ngati mtsinje wa ku Igupto.
9 Et il arrivera en ce jour-là, dit le Seigneur l'Eternel, que je ferai coucher le soleil en plein Midi, et que je ferai venir les ténèbres sur la terre en un jour serein.
“Tsiku limenelo,” Ambuye Yehova akunena kuti, “Ndidzadetsa dzuwa masana ndi kugwetsa mdima pa dziko lapansi dzuwa likuswa mtengo.
10 Je changerai vos fêtes solennelles en deuil, et tous vos cantiques en lamentation; je mettrai le sac sur tous les reins, et je rendrai chauves toutes les têtes; et je mettrai le [pays] en une telle lamentation, que celle d'un fils unique; et sa fin sera telle que d'un jour amer.
Maphwando anu achipembedzo ndidzawasandutsa kulira kwa chisoni ndipo kuyimba kwanu konse ndidzakusandutsa maliro. Ndidzakuvekani chiguduli nonsenu ndi kumeta mipala mitu yanu. Nthawi imeneyo idzakhala ngati yolira mwana wamwamuna mmodzi yekhayo, ndipo tsikulo lidzakhala lowawa mpaka kutha kwake.
11 Voici, les jours viennent, dit le Seigneur l'Eternel, que j'enverrai la famine sur le pays, non la famine du pain, ni la soif de l'eau, mais [la famine] d'ouïr les paroles de l'Eternel.
“Nthawi ikubwera,” Ambuye Yehova akunena kuti, “Ndidzagwetsa njala mʼdziko lonse; osati njala ya chakudya kapena ludzu la madzi, koma njala yofuna kumva mawu a Yehova.
12 Ils courront depuis une mer jusqu'à l'autre, et ils iront de tous côtés depuis l'Aquilon jusqu'à l'Orient, pour chercher la parole de l'Eternel; mais ils ne la trouveront point.
Anthu azidzangoyendayenda kuchoka ku nyanja ina kupita ku nyanja ina. Azidzangoyendayenda kuchoka kumpoto kupita kummawa, kufunafuna mawu a Yehova, koma sadzawapeza.
13 En ce jour-là, pâmeront de soif les belles vierges et les jeunes hommes,
“Tsiku limenelo “anamwali okongola ndi anyamata amphamvu adzakomoka ndi ludzu.
14 qui jurent par le délit de Samarie, et disent: ô Dan! Ton Dieu est vivant: et, vive la voie de Béersébah; ils tomberont donc, et ne se relèveront plus.
Onse amene amalumbira pa tchimo la Samariya, kapena kumanena kuti, ‘Iwe Dani, pali mulungu wako wamoyo,’ kapena, ‘Pali mulungu wamoyo wa ku Beeriseba.’ Iwowo adzagwa ndipo sadzadzukanso.”

< Amos 8 >