< 2 Samuel 1 >

1 Or il arriva qu'après que Saül fut mort, David étant revenu de la défaite des Hamalécites, demeura à Tsiklag deux jours.
Atamwalira Sauli, Davide anabwerako kumene anakagonjetsa Aamaleki ndipo anakakhala ku Zikilagi masiku awiri.
2 Et au troisième jour, voici un homme qui revenait du camp de Saül, ayant ses vêtements déchirés, et de la terre sur sa tête, lequel étant venu à David, se jeta en terre, et se prosterna.
Pa tsiku lachitatu munthu wina wochokera ku msasa wa Sauli anafika, zovala zake zitangʼambika ndiponso anali atathira dothi pamutu pake. Atafika kwa Davide, anadzigwetsa pansi, kupereka ulemu kwa Davideyo.
3 Et David lui dit: D'où viens-tu? et il lui répondit: Je me suis échappé du camp d'Israël.
Davide anamufunsa iye kuti, “Kodi iwe wachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndathawa ku misasa ya Aisraeli.”
4 David lui dit: Qu'est-il arrivé? Je te prie, raconte-le moi. Il répondit: Le peuple s'est enfui de la bataille, et il y en a eu beaucoup du peuple qui sont tombés morts; Saül aussi et Jonathan son fils sont morts.
Davide anafunsa, “Tandiwuza, chachitika ndi chiyani?” Iye anati, “Anthu athawa ku nkhondo ndipo ambiri aphedwa. Sauli ndi mwana wake Yonatani aphedwa.”
5 Et David dit à ce jeune garçon qui lui disait ces nouvelles: Comment sais-tu que Saül et Jonathan son fils soient morts?
Ndipo Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa nkhaniyi, “Ukudziwa bwanji kuti Sauli ndi mwana wake Yonatani afa?”
6 Et le jeune garçon qui lui disait ces nouvelles, lui répondit: Je me trouvai par hasard en la montagne de Guilboah, et voici Saül se tenait penché sur sa hallebarde, car voici, un chariot et quelques Chefs de gens de cheval le poursuivaient.
Mnyamatayo anati, “Zinangochitika kuti ndinali pa phiri la Gilibowa, ndipo Sauli anali komweko ataweramira pa mkondo wake, pamodzi ndi magaleta ndi okwera ake atamuyandikira.
7 Et regardant derrière soi, il me vit, et m'appela; et je lui répondis: Me voici.
Pamene anatembenuka ndi kundiona ine, iye anandiyitana, ndipo ndinati, ‘Kodi ndichite chiyani?’”
8 Et il me dit: Qui es-tu? et je lui répondis: Je suis Hamalécite.
Iye anandifunsa, “Iwe ndiwe yani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndine Mwamaleki.”
9 Et il me dit: Tiens-toi ferme sur moi, je te prie, et me tue; car je suis dans une grande angoisse, et ma vie est encore toute en moi.
“Kenaka iye anati kwa ine, ‘Bwera pafupi ndipo undiphe! Ndikumva ululu kwambiri, koma ndikanali ndi moyo!’
10 Je me suis donc tenu ferme sur lui, et je l'ai fait mourir; car je savais bien qu'il ne vivrait pas après s'être ainsi jeté sur sa hallebarde; et j'ai pris la couronne qu'il avait sur sa tête, et le bracelet qu'il avait en son bras, et je les ai apportés ici à mon Seigneur.
“Kotero ndinabwera pafupi ndi kumupha, chifukwa ndinadziwa kuti mmene anagweramo sakanakhalanso ndi moyo. Ndipo ndatenga chipewa chaufumu chimene chinali pamutu pake ndi khoza la pa dzanja lake ndipo ndazibweretsa kwa inu mbuye wanga.”
11 Alors David prit ses vêtements, et les déchira; et tous les hommes qui étaient avec lui en firent de même.
Apo Davide ndi anthu onse amene anali nawo anangʼamba zovala zawo.
12 Ils menèrent deuil, ils pleurèrent, et ils jeûnèrent jusqu'au soir, à cause de Saül et de Jonathan son fils, et à cause du peuple de l'Eternel, et de la maison d'Israël, parce qu'ils étaient tombés par l'épée.
Iwo analira maliro ndi kusala zakudya mpaka madzulo chifukwa cha Sauli ndi mwana wake Yonatani, komanso chifukwa cha gulu la ankhondo la Yehova ndi nyumba ya Israeli, chifukwa anaphedwa ndi lupanga.
13 Mais David dit au jeune garçon qui lui avait dit ces nouvelles: D'où es-tu? Et il répondit: Je suis fils d'un étranger Hamalécite.
Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa uthengawo, “Iwe umachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine mwana wa mlendo Mwamaleki.”
14 Et David lui dit: Comment n'as-tu pas craint d'avancer ta main pour tuer l'Oint de l'Eternel?
Davide anamufunsanso kuti, “Nʼchifukwa chiyani sunaope kukweza dzanja lako ndi kupha wodzozedwa wa Yehova?”
15 Alors David appela l'un de ses gens, et lui dit: Approche-toi, et te jette sur lui; lequel le frappa, et il mourut.
Kenaka Davide anayitana mmodzi mwa anyamata ake ndipo anati, “Pita ukamukanthe!” Kotero iye anapita kukamukantha, ndipo mnyamata uja anafa.
16 Car David lui avait dit: Ton sang soit sur ta tête, puisque ta bouche a porté témoignage contre toi, en disant: J'ai fait mourir l'Oint de l'Eternel.
Pakuti Davide anali atanena kwa iye kuti, “Iwe wadzipha wekha. Pakamwa pako pakunena zokutsutsa wekha, pamene unanena kuti, ‘Ine ndapha wodzozedwa wa Yehova.’”
17 Alors David fit sur Saül, et sur Jonathan son fils, cette complainte,
Davide anayimba nyimbo iyi ya maliro, kulira Sauli ndi mwana wake Yonatani.
18 [Laquelle] il proféra pour enseigner aux enfants de Juda [à tirer de] l'arc; voici elle est écrite au Livre de Jasar.
Ndipo analamula kuti anthu a ku Yuda aphunzitsidwe nyimbo ya maliroyi imene yalembedwa mʼbuku la Yasari:
19 Ô noblesse d'Israël! ceux qui ont été tués sont sur tes hauts lieux. Comment sont tombés les hommes forts?
“Ulemerero wako iwe Israeli, wagona utaphedwa ku zitunda. Taonani amphamvu agwa kumeneko!
20 Ne l'allez point dire dans Gath, et n'en portez point les nouvelles dans les places d'Askélon; de peur que les filles des Philistins ne s'en réjouissent, de peur que les filles des incirconcis n'en tressaillent de joie.
“Musakanene zimenezi ku Gati, musazilengeze ku misewu ya ku Asikeloni, kuti ana aakazi a Afilisti angasangalale, ana aakazi a osachita mdulidwe angakondwere.
21 Montagne de Guilboah, que la rosée et la pluie [ne tombent point] sur vous, ni sur les champs qui y sont haut élevés; parce que c'est là qu'a été jeté le bouclier des forts, et le bouclier de Saül, [comme s'il] n'eût point été oint d'huile.
“Inu mapiri a ku Gilibowa, musakhalenso ndi mame kapena mvula, kapena minda yobereka zopereka za ufa. Pakuti kumeneko chishango cha munthu wamphamvu chinadetsedwa, chishango cha Sauli sanachipakenso mafuta.
22 L'arc de Jonathan ne revenait [jamais sans] le sang des morts, et sans la graisse des forts; et l'épée de Saül ne retournait [jamais] sans effet.
“Pa magazi a ophedwa, pa mnofu wa amphamvu, uta wa Yonatani sunabwerere, lupanga la Sauli silinabwere chabe.
23 Saül et Jonathan, aimables et agréables en leur vie, n'ont point été séparés dans leur mort; ils étaient plus légers que les aigles, ils étaient plus forts que des lions.
“Sauli ndi Yonatani, pa moyo wawo anali okondedwa ndi okoma mtima, ndipo pa imfa yawo sanasiyanitsidwe. Iwo anali ndi liwiro loposa ziwombankhanga, anali ndi mphamvu zoposa mkango.
24 Filles d'Israël, pleurez sur Saül, qui faisait que vous étiez vêtues d'écarlate, que vous [viviez] dans les délices, [et] que vous portiez des ornements d'or sur vos vêtements.
“Inu ana aakazi a Israeli, mulireni Sauli, amene anakuvekani zovala zofiira ndi zofewa, amene anakometsera zovala zanu ndi zokometsera zagolide.
25 Comment les forts sont-ils tombés au milieu de la bataille! [comment] Jonathan a-t-il été tué sur ces hauts lieux!
“Taonani amphamvu agwa ku nkhondo! Yonatani wagona ataphedwa ku zitunda.
26 Jonathan mon frère! Je suis dans l'angoisse pour l'amour de toi; tu faisais tout mon plaisir; l'amour que j'avais pour toi était plus grand que celui qu'on a pour les femmes.
Ine ndikuvutika mumtima chifukwa cha iwe mʼbale wanga Yonatani, unali wokondedwa kwambiri kwa ine. Chikondi chako pa ine chinali chopambana, chopambana kuposa chikondi cha akazi.
27 Comment sont tombés tes forts, et [comment] sont péris les instruments de guerre!
“Taonani amphamvu agwa! Zida zankhondo zawonongeka!”

< 2 Samuel 1 >