< 2 Samuel 23 >

1 Or ce sont ici les dernières paroles de David. David fils d'Isaï, l'homme qui a été élevé, pour être l'Oint du Dieu de Jacob, et qui compose les doux cantiques d'Israël, dit:
Nawa mawu otsiriza a Davide: “Mawu a Davide mwana wa Yese, mawu a munthu amene wakwezedwa ndi Wammwambamwamba, munthu wodzozedwa ndi Mulungu wa Yakobo, woyimba nyimbo za Israeli:
2 L'Esprit de l'Eternel a parlé par moi, et sa parole a été sur ma langue.
“Mzimu wa Yehova unayankhula kudzera mwa ine; mawu ake anali pakamwa panga.
3 Le Dieu d'Israël a dit, le Rocher d'Israël m'a parlé, [en disant]: Le juste dominateur des hommes, le dominateur en la crainte de Dieu,
Mulungu wa Israeli anayankhula, Thanthwe la Israeli linati kwa ine: ‘Pamene munthu alamulira anthu mwachilungamo, pamene alamulira moopa Mulungu,
4 Est comme la lumière du matin quand le soleil se lève, du matin, [dis-je], qui est sans nuages; [il est comme] l'herbe qui sort de la [terre] après la lumière [du soleil] quand il [paraît] après la pluie.
amakhala ngati kuwala kwa mmamawa, mmawa wopanda mitambo, monga kuwala pamene mvula yaleka kugwa imene imameretsa udzu mʼnthaka.’
5 Mais il n'en sera pas ainsi de ma maison envers le [Dieu] Fort, parce qu'il a traité avec moi une alliance éternelle bien établie, et assurée; car [c'est] tout mon salut, et tout mon plaisir; c'est pourquoi il ne fera pas [simplement] germer [ma maison].
“Kodi banja langa silolungama pamaso pa Mulungu? Kodi Iye sanachite pangano losatha ndi ine, lokonzedwa ndi lotetezedwa mbali zonse? Kodi sadzakwaniritsa chipulumutso changa, ndi kundipatsa chokhumba changa chilichonse?
6 Mais les méchants seront tous ensemble comme des épines qu'on jette au loin, parce qu'on ne les prend point avec la main.
Koma anthu oyipa ndiwo ayenera kutayidwa kunja ngati minga, imene sitengedwa ndi manja.
7 Mais celui qui les veut manier, prend [ou] du fer, ou le bois d'une hallebarde; et on les brûle entièrement sur le lieu même.
Aliyense amene wayikhudza mingayo amayidula pogwiritsa ntchito chigwandali kapena ndodo ya mkondo; nayitentha pa moto.”
8 Ce sont ici les noms des vaillants hommes que David avait: Joseb-Basebeth Tachkémonite était un des principaux capitaines; c'était Hadino le Hetsnite, qui eut le dessus sur huit cents hommes qu'il tua en une seule fois.
Nawa mayina a ankhondo amphamvu a Davide: Yosebu-Basebeti wa ku Takemoni mkulu wa atsogoleri a ankhondo atatu. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 800 nthawi imodzi.
9 Après lui était Eléazar, fils de Dodo, fils d'Ahohi, [l'un de ces] trois vaillants hommes qui étaient avec David lorsqu'on rendit honteux les Philistins assemblés là pour combattre, et que ceux d'Israël se retirèrent.
Wotsatana naye anali Eliezara mwana wa Dodo Mwahohi. Monga mmodzi mwa ankhondo atatu amphamvu a Davide, iye anali ndi Davide pamene anazunza Afilisti amene anasonkhana ku Pasi-Damimu kuchita nkhondo. Kenaka ankhondo a Israeli anabwerera mʼmbuyo.
10 Il se leva, et battit les Philistins, jusqu'à ce que sa main en fut lasse, et qu'elle demeura attachée à l'épée; en ce jour-là l'Eternel accorda une grande délivrance, et le peuple retourna après Eléazar, seulement pour prendre la dépouille.
Koma iye anayima osasuntha ndipo anakantha Afilisti mpaka mkono wake unatopa ndipo unakanirira ku lupanga lake. Yehova anapereka chigonjetso chachikulu pa tsiku limenelo. Asilikali anabwerera kwa Eliezara, kukatenga katundu wa anthu ophedwa.
11 Après lui [était] Samma fils d'Agné Hararite; car les Philistins s'étant assemblés dans un bourg où il y avait un endroit d'un champ plein de lentilles, et le peuple fuyant devant les Philistins;
Wotsatana naye anali Sama mwana wa Age Mharari. Pamene Afilisti anasonkhana pamalo pamene panali munda wa mphodza, ankhondo a Israeli anathawa Afilistiwo.
12 Il se tint au milieu de cet endroit du champ, et le défendit, et frappa les Philistins; tellement que l'Eternel accorda une grande délivrance.
Koma Sama anayima pakati pa mundawo. Iye anawuteteza nakantha Afilistiwo ndipo Yehova anawapambanitsa koposa.
13 Il en descendit encore trois d'entre les trente capitaines qui vinrent au temps de la moisson vers David, dans la caverne d'Hadullam, lorsqu'une compagnie de Philistins était campée en la vallée des Réphaïms.
Pa nthawi yokolola, atatu mwa atsogoleri makumi atatu anabwera kwa Davide ku phanga la Adulamu, pamene gulu la Afilisti linali litamanga misasa mʼchigwa cha Refaimu.
14 David était alors dans la forteresse, et la garnison des Philistins était en ce même temps-là à Bethléhem.
Nthawi imeneyo Davide anali mu linga, ndipo boma la Afilisti linali ku Betelehemu.
15 Et David fit ce souhait, et dit: Qui est-ce qui me ferait boire de l'eau du puits qui est à la porte de Bethléhem?
Davide analakalaka madzi ndipo anati, “Haa, pakanapezeka munthu wokanditungira madzi a mʼchitsime chomwe chili pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu!”
16 Alors ces trois vaillants hommes passèrent au travers du camp des Philistins, et puisèrent de l'eau du puits qui est à la porte de Bethléhem, et l'ayant apportée, ils la présentèrent à David, lequel n'en voulut point boire, mais il la répandit en présence de l'Eternel.
Choncho anthu amphamvu atatuwa anadutsa mizere ya Afilisti, natunga madzi amene anali mʼchitsime chomwe chinali pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu nabwera nawo kwa Davide. Koma iye anakana kumwa. Mʼmalo mwake anathira pansi pamaso pa Yehova.
17 Car il dit: Qu'il ne m'arrive jamais, ô Eternel! de faire une telle chose. N'est-ce pas là le sang de ces hommes qui ont fait ce voyage au péril de leur vie? Il n'en voulut donc point boire. Ces trois vaillants [hommes] firent cette action-là.
Iye anati, “Inu Yehova, musalole kuti ine ndichite chinthu ichi! Kodi awa si magazi a anthu amene anayika miyoyo yawo pachiswe?” Ndipo Davide sanamwe madziwo. Zimenezi ndi zimene anachita anthu amphamvu atatuwo.
18 Il y avait aussi Abisaï frère de Joab fils de Tséruja, qui [était] un des principaux capitaines; celui-ci lançant sa hallebarde contre trois cents hommes, les blessa à mort, et il s'acquit un grand nom entre les trois.
Abisai mʼbale wa Yowabu mwana wa Zeruya ndiye anali mtsogoleri wa anthu atatuwa. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 300, choncho iyeyo anali wotchuka pakati pa anthu atatu aja.
19 Ne fut-il pas le plus estimé entre ces trois-là? c'est pourquoi aussi il fut leur chef; cependant il n égala point les trois premiers.
Kodi iyeyo sanali wolemekezeka koposa? Iye anakhala mtsogoleri wawo ngakhale kuti sanali mʼgulu la anthu atatu aja.
20 Bénaja aussi fils de Jéhojadah, fils d'un vaillant homme, de Kabtléël, avait fait de grands exploits. Il frappa deux des plus puissants hommes de Moab; il descendit aussi et frappa un lion dans une fosse en un jour de neige.
Benaya mwana wa Yehoyada wa ku Kabizeeli anali munthu wolimba mtima amene anachita zinthu zamphamvu. Iye anakantha ankhondo awiri otchuka a ku Mowabu. Tsiku lina kukuzizira kwambiri, iye analowa mʼdzenje ndi kuphamo mkango.
21 Il frappa aussi un homme Egyptien, [qui était] un bel homme. Cet Egyptien avait en sa main une hallebarde; mais Bénaja descendit contre lui avec un bâton, arracha la hallebarde de la main de l'Egyptien, et le tua de sa propre hallebarde.
Ndipo iye anakanthanso Mwigupto wamkulu msinkhu. Ngakhale kuti Mwiguptoyo anali ndi mkondo mʼdzanja mwake, Benaya anapita kukamenyana naye ali ndi chibonga chokha mʼmanja. Iye analanda mkondo mʼdzanja la Mwiguptoyo ndi kumupha ndi mkondo wake womwe.
22 Bénaja fils de Jéhojadah fit ces choses-là, et fut illustre entre les trois vaillants hommes.
Izi ndi zamphamvu zimene Benaya mwana wa Yehoyada anachita. Iyeyo analinso wotchuka ngati anthu atatu amphamvu aja.
23 Et fut plus honoré que les trente; encore qu'il n'égalât point ces trois-là: c'est pourquoi David l'établit sur ses gens de commandement.
Iye ankalemekezedwa kuposa wina aliyense mwa anthu makumi atatu aja, koma sanali mʼgulu la anthu atatu aja. Ndipo Davide anamuyika kukhala woyangʼanira asilikali omuteteza.
24 Hasaël, frère de Joab, était des trente; Elhanan fils de Dodo, de Bethléhem;
Mʼgulu la anthu makumi atatu aja munalinso awa: Asaheli mʼbale wa Yowabu, Elihanani mwana wa Dodo wa ku Betelehemu,
25 Samma Harodite; Elika Harodite;
Sama Mharodi, Elika Mherodi,
26 Helets Paltite; Hira fils de Hikkes, Tékohite;
Helezi Mpaliti, Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa,
27 Abihézer Hanathothite; Mebunnai Husathite;
Abiezeri wa ku Anatoti, Sibekai Mhusati,
28 Tsalmon Ahohite; Maharaï Nétophathite;
Zalimoni Mwahohi, Maharai Mnetofa,
29 Héleb fils de Bahana Nétophathite; Ittaï fils de Ribaï de Guibha des enfants de Benjamin;
Heledi mwana wa Baana Mnetofa, Itai mwana wa Ribai wa ku Gibeya ku Benjamini,
30 Bénaja Pirhathonite; Hiddaï des vallées de Gahas;
Benaya Mpiratoni, Hidayi wa ku zigwa za Gaasi.
31 Abi Halbon Harbathite; Hazmaveth Barhumite;
Abi-Aliboni Mwaribati, Azimaveti Mbarihumi,
32 Eliachba Sahalbonite; [des] enfants de Jesen, Jonathan;
Eliyahiba Msaaliboni, ana a Yaseni, Yonatani,
33 Samma Hararite; Ahiam fils de Sarar Hararite;
mwana wa Sama Mharari, Ahiamu mwana wa Sarari Mharari,
34 Eliphélet, fils d'Ahasbaï, fils de Mahacati; Eliham fils d'Achithophel Guilonite;
Elifeleti mwana wa Ahasibai Mmaakati, Eliamu mwana wa Ahitofele Mgiloni,
35 Hetseraï Carmélite; Parahaï Arbite;
Heziro wa ku Karimeli, Paarai Mwaribi,
36 Jiguéal fils de Nathan de Tsoba; Bani Gadite;
Igala mwana wa Natani wa ku Zoba, mwana wa Hagiri,
37 Tsélek Hammonite; Naharaï Béérothite, qui portait les armes de Joab fils de Tséruja;
Zeleki Mwamoni, Naharai wa ku Beeroti, mnyamata wonyamula zida za Yowabu mwana wa Zeruya,
38 Hira Jithrite; Gareb Jithrite;
Ira Mwitiri, Garebu Mwitiri,
39 Urie Héthien; en tout trente-sept.
ndi Uriya Mhiti. Onse pamodzi analipo 37.

< 2 Samuel 23 >