< 1 Samuel 3 >

1 Or le jeune garçon Samuel servait l'Eternel en la présence d'Héli; et la parole de l'Eternel était rare en ces jours-là, et il n'y avait point d'apparition de visions.
Samueli ankatumikira Yehova moyangʼaniridwa ndi Eli. Masiku amenewo mawu a Yehova sankamveka pafupipafupi. Kuona zinthu mʼmasomphenya sikunkachitikanso kawirikawiri.
2 Et il arriva un jour, qu'Héli étant couché en son lieu, (or ses yeux commençaient à se ternir, et il ne pouvait voir.)
Tsiku lina Eli, amene maso anali ofowoka ndi kuti sankatha kuona bwino, anagona pa malo ake.
3 Et avant que les lampes de Dieu fussent éteintes, Samuel étant aussi couché au Tabernacle de l'Eternel, dans lequel était l'Arche de Dieu;
Nthawiyi nʼkuti nyale ya Mulungu isanazimitsidwe. Samueli anali gone mu Nyumba ya Yehova, kumene kunali Bokosi la Chipangano cha Mulungu.
4 L'Eternel appela Samuel; et il répondit: Me voici.
Yehova anayitana Samueli. Iye anayankha kuti, “Wawa.”
5 Et il courut vers Héli, et lui dit: Me voici, car tu m'as appelé; mais [Héli] dit: Je ne t'ai point appelé, retourne[-t'en], [et] te couche; et il s'en retourna, et se coucha.
Ndipo iyeyo anathamangira kwa Eli ndipo anati, “Ndabwera ndamva kuyitana.” Koma Eli anati, “Ine sindinakuyitane, bwerera kagone.” Ndipo iye anapita kukagona.
6 Et l'Eternel appela encore Samuel; et Samuel se leva, et s'en alla vers Héli, et lui dit: Me voici, car tu m'as appelé. Et [Héli] dit: Mon fils, je ne t'ai point appelé, retourne[-t'en], [et] te couche.
Yehova anayitananso, “Samueli!” Ndipo Samueli anadzuka ndi kupita kwa Eli nati, “Ndabwera popeza ndamva mukundiyitana.” Eli nati, “Mwana wanga, ine sindinakuyitane, bwerera kagone.”
7 Or Samuel ne connaissait point encore l'Eternel, et la parole de l'Eternel ne lui avait point encore été révélée.
Nthawiyi nʼkuti Samueli asanadziwe Yehova ndipo Mawu a Yehova nʼkuti asanawululidwe kwa iye.
8 Et l'Eternel appela encore Samuel pour la troisième fois; et [Samuel] se leva, et s'en alla vers Héli, et dit: Me voici, car tu m'as appelé; [et] Héli reconnut que l'Eternel appelait ce jeune garçon.
Yehova anayitananso Samueli kachitatu ndipo Samueli anadzuka ndikupita kwa Eli ndipo anati, “Ndabwera popeza mwandiyitana ndithu.” Apo Eli anazindikira kuti Yehova ndiye ankayitana mnyamatayo.
9 Alors Héli dit à Samuel: Va-t'en, et te couche; et si on t'appelle, tu diras: Eternel parle, car ton serviteur écoute. Samuel donc s'en alla, et se coucha en son lieu.
Tsono Eli anamuwuza Samueli kuti, “Pita ukagone ndipo akakuyitananso ukanene kuti, ‘Yankhulani Yehova, pakuti mtumiki wanu ndikumvetsera.’” Choncho Samueli anapita ndi kukagona pamalo pake.
10 L'Eternel donc vint, et se tint là; et appela comme les autres fois: Samuel, Samuel; et Samuel dit: Parle, car ton serviteur écoute.
Yehova anabwera ndi kuyima pomwepo, ndi kuyitana monga nthawi zina zija, “Samueli! Samueli!” Ndipo Samueli anayankha, “Yankhulani, pakuti mtumiki wanu akumvetsera.”
11 Alors l'Eternel dit à Samuel: Voici, je m'en vais faire une chose en Israël, laquelle quiconque entendra, ses deux oreilles lui corneront.
Ndipo Yehova anati kwa Samueli, “Taona, patsala pangʼono kuti ndichite chinthu china mu Israeli chimene chidzadabwitsa aliyense amene adzamve.
12 En ce jour-là j'effectuerai contre Héli tout ce que j ai dit touchant sa maison; en commençant, et en achevant.
Tsiku limenelo ndidzachitadi zonse zimene ndinayankhula zokhudza banja la Eli kuyambira poyamba mpaka pomaliza.
13 Car je l'ai averti que je m'en allais punir sa maison pour jamais, à cause de l'iniquité laquelle il a bien connue, qui est que ses fils se sont rendus infâmes, et il ne les a point réprimés.
Pakuti ndinamudziwitsa kuti Ine ndikhoza kulanga banja lake kwamuyaya chifukwa cha zoyipa zimene ana ake ankadziyipitsa nazo. Iye ankadziwa zimenezi koma osawaletsa.
14 C'est pourquoi j'ai juré contre la maison d'Héli; si jamais il se fait propitiation pour l'iniquité de la maison d'Héli, par sacrifice ou par oblation.
Nʼchifukwa chake ndinalumbira kuti, ‘Zoyipa zimene banja la Eli linandichita sizidzafafanizidwa mpaka muyaya ngakhale adzapereke nsembe kapena zopereka zina.’”
15 Et Samuel demeura couché jusqu'au matin, puis il ouvrit les portes de la maison de l'Eternel. Or Samuel craignait de déclarer cette vision à Héli.
Samueli anagona mpaka mmawa. Atadzuka anatsekula zitseko za Nyumba ya Yehova. Iye anachita mantha kumuwuza Eli za masomphenya ake.
16 Mais Héli appela Samuel, et lui dit: Samuel mon fils, et il répondit: Me voici.
Koma Eli anamuyitana nati, “Samueli mwana wanga.” Samueli anayankha kuti, “Wawa.”
17 Et [Héli] dit: Quelle est la parole qui t'a été dite? Je te prie ne me la cache point. Ainsi Dieu te fasse, et ainsi il y ajoute, si tu me caches un seul mot de tout ce qui t'a été dit.
Tsono Eli anafunsa kuti, “Yehova wakuwuza chiyani? Usandibisire. Mulungu akulange ndithu ngati undibisira chilichonse cha zimene wakuwuza.”
18 Samuel donc lui déclara tout ce qui lui avait été dit, et ne lui en cacha rien. Et [Héli] répondit: C'est l'Eternel; qu'il fasse ce qui lui semblera bon.
Choncho Samueli anamuwuza zonse, sanamubisire kalikonse. Ndipo Eli anati, “Iye ndi Yehova, mulekeni achite chimene chamukomera.”
19 Or Samuel devenait grand, et l'Eternel était avec lui, qui ne laissa point tomber à terre une seule de ses paroles.
Yehova anali ndi Samueli pamene amakula, ndipo zonse zimene ankayankhula zinkachitikadi.
20 Et tout Israël, depuis Dan jusqu'à Béersebah, connut que c'était une chose assurée que Samuel serait Prophète de l'Eternel.
Ndipo Aisraeli onse kuyambira ku dera la Dani mpaka ku Beeriseba anazindikira kuti Yehova analozadi chala pa Samueli kuti akhale mneneri wake.
21 Et l'Eternel continua de se manifester dans Silo; car l'Eternel se manifestait à Samuel dans Silo par la parole de l'Eternel.
Yehova anapitiriza kuoneka ku Silo, ndipo kumeneko anadziwulula yekha kwa Samueli mwa mawu ake.

< 1 Samuel 3 >