< 1 Samuel 29 >

1 Or les Philistins assemblèrent toutes leurs armées à Aphek; et les Israëlites étaient campés près de la fontaine de Jizréhel.
Afilisti anasonkhanitsa asilikali awo onse ku Afeki, ndipo Israeli anamanga misasa yawo pa chitsime cha Yezireeli.
2 Et les Gouverneurs des Philistins passèrent par [leurs] centaines et par [leurs] milliers; et David et ses gens passèrent sur l'arrière-garde avec Akis.
Pamene atsogoleri a Afilisti ankatsogolera magulu awo ankhondo a miyandamiyanda, Davide ndi ankhondo ake ankayenda pambuyo pamodzi ndi Akisi.
3 Et les chefs des Philistins dirent: Qu'est-ce que ces Hébreux-là? Et Akis répondit aux chefs des Philistins: N'est-ce pas ici ce David, serviteur de Saül Roi d'Israël, qui a déjà été avec moi quelque temps, même quelques années? et je n'ai rien trouvé à redire en lui depuis le jour qu'il s'est rendu [à moi], jusqu'à ce jour.
Tsono atsogoleri a Afilisti aja anafunsa kuti, “Kodi Ahebri awa akufuna chiyani?” Akisi anayankha kuti, “Uyu ndi Davide, mtumiki wa Sauli mfumu ya Israeli. Iye wakhala ndi ine kwa masiku ndithu, kapena titi zaka ndipo kuyambira tsiku limene anachoka kwa Sauli mpaka lero, ine sindinapeze cholakwa mwa iye.”
4 Mais les chefs des Philistins se mirent en colère contre lui, et lui dirent: Renvoie cet homme, et qu'il s'en retourne dans le lieu où tu l'as établi, et qu'il ne descende point avec nous dans la bataille, de peur qu'il ne se tourne contre nous dans la bataille; car comment pourrait-il se remettre en grâce avec son Seigneur? ne serait-ce pas par le moyen des têtes de ces hommes-ci?
Koma atsogoleri a ankhondo a Afilisti anamukwiyira Akisi kwambiri ndipo anati, “Mubweze munthuyu kuti abwerere ku malo amene unamupatsa. Iye asapite nafe ku nkhondo kuopa kuti angadzasanduke mdani wathu. Kodi iyeyu adzadziyanjanitsa bwanji ndi mbuye wake? Iyeyutu adzadziyanjanitsa ndi mbuye wake pakupha anthu ali panowa?
5 N'est-ce pas ici ce David, duquel on s'entre-répondait aux danses, en disant? Saül en a frappé ses mille et David ses dix mille?
Paja ameneyu ndi Davide yemwe ankamuvinira namuyimbira kuti, “‘Sauli wapha anthu 1,000 koma Davide wapha miyandamiyanda?’”
6 Akis donc appela David, et lui dit: L'Eternel est vivant, que tu es certainement un homme droit, et que ta conduite au camp m'a paru bonne, car je n'ai point trouvé de mal en toi, depuis le jour que tu es venu à moi jusqu'à ce jour; mais tu ne plais point aux Gouverneurs.
Kotero Akisi anayitana Davide ndipo anamuwuza kuti, “Pali Yehova wamoyo, iwe wakhala wodalirika ndipo chikanakhala chinthu chabwino kuti uzimenya nkhondo pamodzi nane popeza chibwerere iwe kuno ine sindinapeze cholakwa chilichonse ndi iwe. Koma atsogoleri enawa ndiwo sakukufuna.
7 Maintenant donc retourne-t'en, et t'en va en paix, afin que tu ne fasses aucune chose qui déplaise aux Gouverneurs des Philistins.
Tsono bwerera. Upite mu mtendere kuopa kuti ungachite kanthu kena koyipira atsogoleri a Afilistiwa.”
8 Et David dit à Akis: Mais qu'ai-je fait? et qu'as-tu trouvé en ton serviteur depuis le jour que j'ai été avec toi jusqu'à ce jour, que je n'aille point combattre contre les ennemis du Roi mon Seigneur?
Davide anafunsa Akisi kuti, “Kodi ndachita chiyani? Kodi mwapeza cholakwa chotani mwa ine mtumiki wanu chiyambire kukutumikirani mpaka lero? Tsono chifukwa chiyani sindingapite kukamenya nkhondo ndi adani a mbuye wanga mfumu?”
9 Et Akis répondit et dit à David: Je le sais: car tu es agréable à mes yeux, comme un Ange de Dieu; mais c'est seulement que les chefs des Philistins ont dit: Il ne montera point avec nous dans la bataille.
Akisi anayankha kuti, “Ine ndikudziwa kuti ndiwe wangwiro ngati mngelo wa Mulungu. Komabe atsogoleri a ankhondo a Afilisti akuti, ‘Davide asapite nafe ku nkhondo.’
10 C'est pourquoi lève-toi de bon matin, avec les serviteurs de ton Seigneur qui sont venus avec toi; et étant levés de bon matin, sitôt que vous verrez le jour, allez-vous-en.
Tsono udzuke mmamawa, pamodzi ndi ankhondo ako amene unabwera nawo, ndipo unyamuke kukangocha.”
11 Ainsi David se leva de bon matin, lui et ses gens, pour partir dès le matin, [et] s'en retourner au pays des Philistins; mais les Philistins montèrent à Jizréhel.
Choncho Davide ndi anthu ake anadzuka mmamawa kubwerera ku dziko la Afilisti. Koma Afilistiwo anapita ku Yezireeli.

< 1 Samuel 29 >