< 1 Pierre 5 >

1 Je prie les Anciens qui sont parmi vous, moi qui suis Ancien avec eux, et témoin des souffrances de Christ, et participant de la gloire qui doit être révélée, [et je leur dis]:
Ine ndikupempha akulu a mpingo amene ali pakati panu, monga inenso mkulu mnzawo, mboni ya zowawa za Khristu ndiponso amene ndidzalandira nawo ulemerero umene uti udzaonetsedwe.
2 Paissez le Troupeau de Christ qui vous est commis, en prenant garde sur lui, non point par contrainte, mais volontairement; non point pour un gain déshonnête, mais par un principe d'affection.
Wetani gulu la Mulungu limene lili mʼmanja mwanu, muziliyangʼanira. Muzichita osati mowumirizidwa, koma mwakufuna kwanu, monga momwe Mulungu akufunira kuti mutero. Musachite chifukwa chadyera la ndalama, koma ndi mtima ofuna kutumikira.
3 Et non point comme ayant domination sur les héritages [du Seigneur], mais en telle manière que vous soyez pour modèle au Troupeau.
Musakhale ngati mafumu pa amene mukuwayangʼanira, koma mukhale chitsanzo kwa gululo.
4 Et quand le souverain Pasteur apparaîtra, vous recevrez la couronne incorruptible de gloire.
Ndipo Mʼbusa wamkulu akadzaonekera, mudzalandira chipewa cha ulemerero chosafota.
5 De même, vous jeunes gens, soyez soumis aux Anciens, et ayant tous de la soumission l'un pour l'autre, soyez parés par-dedans d'humilité, parce que Dieu résiste aux orgueilleux, mais il fait grâce aux humbles.
Momwemonso, inu anyamata gonjerani amene ndi akulu. Inu nonse mukhale odzichepetsa kuti mutumikirane, chifukwa, “Mulungu amatsutsana nawo odzikuza, koma amapereka chisomo kwa odzichepetsa.”
6 Humiliez-vous donc sous la puissante main de Dieu, afin qu'il vous élève quand il en sera temps;
Choncho, mudzichepetse pamaso pa Mulungu wamphamvu, kuti pa nthawi yake adzakukwezeni.
7 Lui remettant tout ce qui peut vous inquiéter: car il a soin de vous.
Tayani pa Iye nkhawa zanu zonse chifukwa ndiye amakusamalani.
8 Soyez sobres, [et] veillez: car le diable, votre adversaire, tourne autour de vous comme un lion rugissant, cherchant qui il pourra dévorer.
Khalani odziretsa ndi atcheru. Mdani wanu mdierekezi amayendayenda monga mkango wobangula kufunafuna wina kuti amumeze.
9 Résistez-lui [donc] en [demeurant] fermes dans la foi, sachant que les mêmes souffrances s'accomplissent en la compagnie de vos frères, qui sont dans le monde.
Mukaneni iye, ndipo mukhazikike mʼchikhulupiriro, chifukwa mukudziwa kuti abale anzanu pa dziko lonse lapansi nawonso akumva zowawa zomwezi.
10 Or le Dieu de toute grâce, qui nous a appelés à sa gloire éternelle en Jésus-Christ, après que vous aurez souffert un peu de temps, vous rende accomplis, vous affermisse, vous fortifie, [et] vous établisse. (aiōnios g166)
Ndipo Mulungu wachisomo chonse, amene anakuyitanani ku ulemerero wake wamuyaya mwa Khristu, mutamva zowawa pa kanthawi, adzakukonzaninso ndi kukulimbitsani pa maziko olimba. (aiōnios g166)
11 A lui soit la gloire et la force, aux siècles des siècles, Amen! (aiōn g165)
Kwa Iye kukhale mphamvu mpaka muyaya, Ameni. (aiōn g165)
12 Je vous ai écrit brièvement par Silvain notre frère, que je crois vous être fidèle, vous déclarant et vous protestant que la grâce de Dieu dans laquelle vous êtes est la véritable.
Mothandizidwa ndi Sila, amene ndi mʼbale wokhulupirika, ndakulemberani mwachidule kukulimbikitsani ndi kuchita umboni kuti ichi ndi chisomo choona cha Mulungu.
13 [L'Eglise] qui est à Babylone, élue avec vous, et Marc mon fils, vous saluent.
Imani mwamphamvu mʼchisomochi. Mlongo wanu amene ali ku Babuloni, wosankhidwa pamodzi nanu akupereka moni, nayenso Marko, mwana wanga, akupereka moni.
14 Saluez-vous l'un l'autre par un baiser de charité. Que la paix soit à vous tous, qui êtes en Jésus-Christ, Amen!
Mupatsane moni ndi mpsopsono wachikondi. Mtendere ukhale ndi inu nonse amene muli mwa Khristu.

< 1 Pierre 5 >