< 1 Jean 5 >

1 Quiconque croit que Jésus est le Christ, est né de Dieu; et quiconque aime celui qui l'a engendré, aime aussi celui qui est né de lui.
Aliyense amene amakhulupirira kuti Yesu ndi Khristu, iyeyo ndi mwana wa Mulungu, ndipo aliyense amene amakonda Atate amakondanso Mwana wake.
2 Nous connaissons à cette marque que nous aimons les enfants de Dieu, c'est lorsque nous aimons Dieu, et que nous gardons ses commandements.
Chodziwira kuti timakonda ana a Mulungu nʼchakuti timakonda Mulungu ndi kusunga malamulo ake.
3 Car c'est en ceci que consiste [notre] amour pour Dieu; que nous gardions ses commandements; et ses commandements ne sont point pénibles.
Pakuti kukonda Mulungu ndiye kusunga malamulo ake. Ndipo malamulo ake siwolemetsa,
4 Parce que tout ce qui est né de Dieu surmonte le monde; et ce qui nous fait remporter la victoire sur le monde, c'est notre foi.
chifukwa aliyense amene ndi mwana wa Mulungu amagonjetsa dziko lapansi. Chikhulupiriro chathu ndicho timagonjetsera dziko lapansi.
5 Qui est celui qui surmonte le monde, sinon celui qui croit que Jésus est le Fils de Dieu?
Ndani amagonjetsa dziko lapansi? Yekhayo amene amakhulupirira kuti Yesu ndi Mwana wa Mulungu.
6 C'est ce Jésus qui est venu par eau et par sang, et non-seulement par l'eau, mais par l'eau et le sang; et c'est l'Esprit qui en rend témoignage; or l'Esprit est la vérité.
Uyu ndiye anabwera mwa madzi ndi magazi, ndiye Yesu Khristu. Sanabwere mwa madzi okha, koma mwa madzi ndi magazi. Ndipo ndi Mzimu Woyera amene akuchitira umboni, chifukwa Mzimu Woyera ndi choonadi.
7 Car il y en a trois dans le Ciel qui rendent témoignage, le Père, la Parole, et le Saint-Esprit; et ces trois-là ne sont qu'un.
Pakuti pali atatu amene amachitira umboni.
8 Il y en a aussi trois qui rendent témoignage sur la terre, savoir l'Esprit, l'eau, et le Sang; et ces trois-là se rapportent à un.
Mzimu Woyera, madzi ndi magazi; ndipo atatu amavomerezana.
9 Si nous recevons le témoignage des hommes, le témoignage de Dieu est plus considérable, or c'est là le témoignage de Dieu, lequel il a rendu de son Fils.
Timalandira umboni wa anthu, koma umboni wa Mulungu ndi wopambana. Umboniwo ndi umene anachitira Mwana wake.
10 Celui qui croit au Fils de Dieu, il a au-dedans de lui-même le témoignage de Dieu; mais celui qui ne croit point Dieu, il l'a fait menteur; car il n'a point cru au témoignage que Dieu a rendu de son Fils.
Aliyense amene amakhulupirira Mwana wa Mulungu ali nawo umboniwu mu mtima mwake, koma aliyense amene sanakhulupirire Mulungu amayesa kuti Mulunguyo ndi wonama, chifukwa sanakhulupirire umboni umene Mulungu anachitira wa Mwana wake.
11 Et c'est ici le témoignage, [savoir] que Dieu nous a donné la vie éternelle; et cette vie est en son Fils. (aiōnios g166)
Ndipo umboniwo ndi uwu: Mulungu anatipatsa moyo wosatha, ndipo moyowu uli mwa Mwana wake. (aiōnios g166)
12 Celui qui a le Fils, a la vie, celui qui n'a point le Fils de Dieu, n'a point la vie.
Iye amene ali ndi Mwana ali ndi moyo, amene alibe Mwana wa Mulungu alibe moyo.
13 Je vous ai écrit ces choses, à vous qui croyez au Nom du Fils de Dieu, afin que vous sachiez que vous avez la vie éternelle, et afin que vous croyiez au Nom du Fils de Dieu. (aiōnios g166)
Ine ndikulemba zimenezi kwa inu, amene mwakhulupirira dzina la Mwana wa Mulungu kuti mudziwe kuti muli ndi moyo wosatha. (aiōnios g166)
14 Et c'est ici la confiance que nous avons en Dieu, que si nous demandons quelque chose selon sa volonté, il nous exauce.
Ife timalimba mtima tikamafika pamaso pa Mulungu, popeza kuti ngati tipempha kanthu kalikonse monga mwa chifuniro chake, amatimvera.
15 Et si nous savons qu'il nous exauce, en quoi que nous demandions, nous le savons parce que nous obtenons les choses que nous lui avons demandées.
Ndipo ngati tikudziwa kuti amatimvera, chilichonse chimene timapempha, tikudziwanso kuti tili nacho chimene tamupempha Iye.
16 Si quelqu'un voit son frère pécher d'un péché qui n'est point à la mort, il priera [pour lui], et [Dieu] lui donnera la vie; savoir à ceux qui ne pèchent point à la mort. Il y a un péché à la mort; je ne te dis point de prier pour ce péché-là.
Ngati wina aona mʼbale wake akuchita tchimo losadzetsa imfa, apemphere ndipo Mulungu adzamupatsa moyo mʼbale wakeyo. Ndikunena za ochita tchimo losadzetsa imfa. Pali tchimo lodzetsa imfa. Ine sindikunena kuti apemphere ayi.
17 Toute iniquité est un péché; mais il y a quelque péché qui n'est point à la mort.
Chilichonse chosalungama ndi tchimo ndipo pali tchimo losadzetsa imfa.
18 Nous savons que quiconque est né de Dieu, ne pèche point; mais celui qui est engendré de Dieu, se conserve soi-même, et le malin [esprit] ne le touche point.
Tikudziwa kuti aliyense amene ndi mwana wa Mulungu sachimwirachimwirabe. Yesu, Mwana wa Mulungu, amamusunga ndipo woyipa uja sangamukhudze.
19 Nous savons que nous sommes [nés] de Dieu; mais tout le monde est plongé dans le mal.
Tikudziwa kuti ndife ana a Mulungu ndi kuti dziko lonse lapansi lili pansi pa ulamuliro wa woyipayo.
20 Or nous savons que le Fils de Dieu est venu, et il nous a donné l'intelligence pour connaître le Véritable; et nous sommes dans le Véritable, [savoir], en son Fils Jésus-Christ; il est le vrai Dieu, et la vie éternelle. (aiōnios g166)
Tikudziwa kuti Mwana wa Mulungu anafika ndipo anatipatsa nzeru, kuti timudziwe Iye amene ali woona. Ndipo ife tili mwa Iye amene ndi woona, Mwana wake, Yesu Khristu. Iye ndi Mulungu woona ndi moyo wosatha. (aiōnios g166)
21 Mes petits enfants, gardez-vous des idoles. Amen.
Ana okondedwa, dzisungeni bwino, osapembedza mafano.

< 1 Jean 5 >