< 1 Jean 3 >

1 Voyez quelle charité le Père a eue pour nous, que nous soyons appelés les enfants de Dieu; mais le monde ne nous connaît point, parce qu'il ne l'a point connu.
Taonani kukula kwake kwa chikondi chimene Atate anatikonda nacho, kuti titchedwe ana a Mulungu! Ndipo nʼchimene ife tili! Nʼchifukwa chake dziko lapansi silitidziwa chifukwa silinamudziwe Iye.
2 Mes bien-aimés, nous sommes maintenant les enfants de Dieu, mais ce que nous serons n'est pas encore manifesté; or nous savons que lorsque [le fils de Dieu] sera apparu, nous lui serons semblables; car nous le verrons tel qu'il est.
Abale okondedwa, tsopano ndife ana a Mulungu, ndipo sichinaoneke chimene tidzakhala. Koma tikudziwa kuti Yesu akadzaonekera, tidzafanana naye, pakuti tidzamuona Iyeyo monga momwe alili.
3 Et quiconque a cette espérance en lui, se purifie, comme lui aussi est pur.
Aliyense amene ali ndi chiyembekezo ichi mwa Iye adziyeretse yekha, monga Iye ali woyera.
4 Quiconque fait un péché, agit contre la Loi; car le péché est ce qui est contre la Loi.
Aliyense amene amachimwa amaphwanya lamulo; pakuti tchimo ndi kuphwanya lamulo.
5 Or vous savez qu'il est apparu, afin qu'il ôtât nos péchés; et il n'y a point de péché en lui.
Koma inu mukudziwa kuti Yesu anabwera kuti adzachotse machimo athu. Ndipo mwa Iye mulibe tchimo.
6 Quiconque demeure en lui, ne pèche point: quiconque pèche, ne l'a point vu, ni ne l'a point connu.
Aliyense wokhala mwa Khristu sachimwa. Aliyense amene amachimwa sanamuone kapena kumudziwa.
7 [Mes] petits enfants, que personne ne vous séduise. Celui qui fait ce qui est juste, est une personne juste, comme Jésus-Christ est juste;
Ana okondedwa, musalole kuti aliyense akusocheretseni. Munthu amene amachita chilungamo ndi wolungama, monga Khristu ali wolungama.
8 Celui qui vit dans le péché est du Diable; car le Diable pèche dès le commencement; or le Fils de Dieu est apparu pour détruire les œuvres du Diable.
Iye amene amachimwa ndi wa Satana, chifukwa mdierekezi wakhala akuchimwa kuyambira pa chiyambi. Mwana wa Mulungu anaonekera kuti awononge ntchito za mdierekezi.
9 Quiconque est né de Dieu ne vit point dans le péché; car la semence de Dieu demeure en lui; et il ne peut pécher, parce qu'il est né de Dieu.
Aliyense amene ndi mwana wa Mulungu, sachimwirachimwira, popeza mbewu ya Mulungu ili mwa iye, sangathe kuchimwa, chifukwa ndi mwana wa Mulungu.
10 [Et] c'est à cela que sont connus les enfants de Dieu, et les enfants du Diable. Quiconque ne fait pas ce qui est juste, et qui n'aime pas son frère n'est point de Dieu.
Mmenemu ndi mmene timadziwira ana a Mulungu ndi amene ali ana a mdierekezi. Aliyense amene sachita chilungamo si mwana wa Mulungu; ngakhalenso amene sakonda mʼbale wake.
11 Car c'est ici ce que vous avez ouï annoncer dès le commencement; [savoir] que nous nous aimions l'un l'autre;
Uthenga umene munawumva kuyambira pachiyambi ndi uwu: Tizikondana wina ndi mnzake.
12 Et que nous ne soyons point comme Caïn, qui était du malin [esprit] et qui tua son frère. Mais pour quel sujet le tua-t-il? c'est parce que ses œuvres étaient mauvaises, et que celles de son frère étaient justes.
Musakhale ngati Kaini, amene anali wa woyipayo ndipo anapha mʼbale wake. Nanga anamupha chifukwa chiyani? Chifukwa zochita zake zinali zoyipa ndipo zochita za mʼbale wake zinali zolungama.
13 Mes frères, ne vous étonnez point si le monde vous hait.
Abale anga, musadabwe ngati dziko lapansi lidana nanu.
14 En ce que nous aimons nos frères, nous savons que nous sommes transférés de la mort à la vie: celui qui n'aime point son frère, demeure en la mort.
Ife tikudziwa kuti tinatuluka mu imfa ndi kulowa mʼmoyo, chifukwa timakonda abale athu. Aliyense amene sakonda mʼbale wake akanali mu imfa.
15 Quiconque hait son frère est un meurtrier; et vous savez qu'aucun meurtrier ne possède point la vie éternelle. (aiōnios g166)
Aliyense amene amadana ndi mʼbale wake ndi wakupha, ndipo inu mukudziwa kuti wopha anthu mwa iye mulibe moyo wosatha. (aiōnios g166)
16 A ceci nous avons connu la charité, c'est qu'il a exposé sa vie pour nous; nous devons donc aussi exposer nos vies pour nos frères.
Mmene timadziwira chikondi chenicheni ndi umu: Yesu anapereka moyo wake chifukwa cha ife. Ndipo nafenso tiyenera kupereka miyoyo yathu chifukwa cha abale athu.
17 Or celui qui voyant son frère dans la nécessité, lui fermera ses entrailles, comment est-ce que la charité de Dieu demeure en lui?
Ngati wina ali ndi chuma ndipo nʼkuona mʼbale wake akusowa, koma wosamvera chisoni, kodi mwa iyeyo muli chikondi cha Mulungu?
18 Mes petits enfants, n'aimons pas de paroles, ni de langue, mais par des effets, et en vérité.
Ana okondedwa, chikondi chathu chisakhale cha pakamwa pokha koma cha ntchito zathu ndi mʼchoonadi.
19 Car c'est par là que nous connaissons que nous sommes de la vérité; et nous assurons [ainsi] nos cœurs devant lui.
Pamenepo tidzadziwa kuti tili pa choonadi ndipo tidzakhala okhazikika mtima pamaso pa Mulungu,
20 Que si notre cœur nous condamne, certes Dieu est plus grand que notre cœur, et il connaît toutes choses.
nthawi zonse pamene mtima wathu utitsutsa. Pakuti Mulungu ndi wamkulu kuposa mitima yathu ndipo Iye amadziwa zonse.
21 Mes bien-aimés, si notre cœur ne nous condamne point, nous avons assurance envers Dieu.
Anzanga okondedwa, ngati mitima yathu sikutitsutsa, tili nako kulimbika mtima pamaso pa Mulungu.
22 Et quoi que nous demandions, nous le recevons de lui; parce que nous gardons ses commandements, et que nous faisons les choses qui lui sont agréables.
Ndipo timalandira chilichonse chimene tichipempha kwa Iye, chifukwa timamvera malamulo ake ndi kuchita zimene zimamukondweretsa.
23 Et c'est ici son commandement, que nous croyions au Nom de son Fils Jésus-Christ, et que nous nous aimions l'un l'autre, comme il nous en a donné le commandement.
Ndipo lamulo lake ndi ili: kukhulupirira dzina la Mwana wake, Yesu Khristu, ndi kukondana wina ndi mnzake monga Iye anatilamulira.
24 Et celui qui garde ses commandements demeure en Jésus-Christ, et Jésus-Christ [demeure] en lui; et par ceci nous connaissons qu'il demeure en nous, [savoir] par l'Esprit qu'il nous a donné.
Iwo amene amamvera malamulo ake amakhala mwa Iye, ndipo Iye amakhala mwa iwo. Ndipo mmenemu ndi momwe timadziwira kuti Iye akukhala mwa ife. Timadziwa mwa Mzimu Woyera amene anatipatsa.

< 1 Jean 3 >