< 1 Chroniques 24 >

1 Et quant aux enfants d'Aaron, ce sont ici leurs départements. Les enfants d'Aaron furent, Nadab, Abihu, Eléazar et Ithamar.
Magulu a ana a Aaroni anali awa: Ana a Aaroni anali Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
2 Mais Nadab et Abihu moururent en la présence de leur père, et n'eurent point d'enfants; et Eléazar et Ithamar exercèrent la sacrificature.
Koma Nadabu ndi Abihu anamwalira abambo awo asanamwalire, ndipo analibe ana aamuna. Kotero Eliezara ndi Itamara ankatumikira monga ansembe.
3 Or David les distribua, savoir, Tsadoc, qui était des enfants d'Eléazar; et Ahimélec, qui était des enfants d'Ithamar, pour leurs charges, dans le service qu'ils avaient à faire.
Mothandizidwa ndi Zadoki chidzukulu cha Eliezara ndi Ahimeleki chidzukulu cha Itamara, Davide anawagawa mʼmagulu molingana ndi ntchito yawo yotumikira.
4 Et quand on les distribua, on trouva un beaucoup plus grand nombre des enfants d'Eléazar pour être Chefs de famille, que des enfants d'Ithamar, y ayant eu des enfants d'Eléazar, seize Chefs, selon leurs familles, et [n'y en ayant eu que] huit, des enfants d'Ithamar, selon leurs familles.
Atsogoleri ambiri anapezeka pakati pa zidzukulu za Eliezara kusiyana ndi zidzukulu za Itamara ndipo anagawidwa moyenera: atsogoleri 16 a mabanja ochokera kwa Eliezara, ndipo atsogoleri asanu ndi atatu a mabanja ochokera kwa zidzukulu za Itamara.
5 Et on fit leurs départements par sort, les entremêlant les uns parmi les autres; car les Gouverneurs du Sanctuaire, et les Gouverneurs [de la maison] de Dieu furent tirés tant des enfants d'Eléazar, que des enfants d'Ithamar.
Anawagawa mosakondera pochita maere, pakuti iwo anali akuluakulu a ku malo opatulika ndi akuluakulu a Mulungu pakati pa zidzukulu za Eliezara ndi Itamara.
6 Et Sémahja fils de Nathanaël scribe, qui était de la Tribu de Lévi, les mit par écrit en la présence du Roi, des principaux [du peuple], de Tsadoc le Sacrificateur, d'Ahimélec, fils d'Abiathar, et des Chefs des pères [des familles] des Sacrificateurs, et de celles des Lévites. Le [chef] d'une maison de père se tirait pour Eléazar, et celui qui était tiré [après], se tirait pour Ithamar.
Mlembi Semaya mwana wa Netaneli, Mlevi, analemba mayina awo pamaso pa mfumu ndi akuluakulu ake: wansembe Zadoki, Ahimeleki mwana wa Abiatara ndi atsogoleri a mabanja a ansembe ndiponso Alevi, banja limodzi kuchokera kwa Eliezara kenaka limodzi kuchokera kwa Itamara.
7 Le premier sort donc échut à Jéhojarib, le second à Jédahia,
Maere woyamba anagwera Yehoyaribu, achiwiri anagwera Yedaya,
8 Le troisième à Harim, le quatrième à Sehorim,
achitatu anagwera Harimu, achinayi anagwera Seorimu,
9 Le cinquième à Malkija, le sixième à Mijamin,
achisanu anagwera Malikiya, achisanu ndi chimodzi anagwera Miyamini,
10 Le septième à Kots, le huitième à Abija,
achisanu ndi chiwiri anagwera Hakozi, achisanu ndi chitatu anagwera Abiya,
11 Le neuvième à Jésuah, le dixième à Sécania,
achisanu ndi chinayi anagwera Yesuwa, a khumi anagwera Sekaniya,
12 L'onzième à Eliasib, le douzième à Jakim,
a 11 anagwera Eliyasibu, a 12 anagwera Yakimu,
13 Le treizième à Huppa, le quatorzième à Jésébab,
a 13 anagwera Hupa, a 14 anagwera Yesebeabu,
14 Le quinzième à Bilga, le seizième à Immer,
a 15 anagwera Biliga, a 16 anagwera Imeri,
15 Le dix-septième à Hézir, le dix-huitième à Pitsets,
a 17 anagwera Heziri, a 18 anagwera Hapizezi,
16 Le dix-neuvième à Péthahja, le vingtième à Ezéchiel,
a 19 anagwera Petahiya, a 20 anagwera Ezekieli,
17 Le vingt et unième à Jakim, et le vingt et deuxième à Gamul,
a 21 anagwera Yakini, a 22 anagwera Gamuli,
18 Le vingt et troisième à Délaja, le vingt et quatrième à Mahazia.
a 23 anagwera Delaya, ndipo a 24 anagwera Maaziya.
19 Tel fut leur dénombrement pour le service qu'ils avaient à faire, lorsqu'ils entraient dans la maison de l'Eternel, selon qu'il leur avait été ordonné par Aaron leur père, comme l'Eternel le Dieu d'Israël le lui avait commandé.
Umu ndi mmene anasankhidwira kuti azigwira ntchito yotumikira pamene alowa mʼNyumba ya Yehova, motsatira dongosolo limene anapatsidwa ndi kholo lawo Aaroni, monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli anamulamulira.
20 Et quant aux enfants de Lévi qu'il y avait eu de reste des enfants de Hamram, il y eut Subaël, et des enfants de Subaël Jehdéja.
Za zidzukulu zina zonse za Levi: Kuchokera kwa ana a Amramu: Subaeli; kuchokera kwa ana a Subaeli: Yehideya.
21 De ceux de Réhabia, des enfants, [dis-je], de Réhabia, Jisija était le premier.
Kwa Rehabiya, kuchokera kwa ana ake: Mtsogoleri anali Isiya.
22 Des Jitsharites, Sélomoth; des enfants de Sélomoth, Jahath.
Kuchokera ku banja la Izihari: Selomoti; kuchokera kwa ana a Selomoti: Yahati.
23 Et des enfants de Jérija, Amaria le second; Jahaziël le troisième, Jékamham le quatrième.
Ana a Hebroni: woyamba anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, wachitatu anali Yahazieli ndipo Yekameamu anali wachinayi.
24 Des enfants de 'Huziël, Mica; des enfants de Mica, Samir.
Mwana wa Uzieli: Mika; kuchokera kwa ana a Mika: Samiri.
25 Le frère de Mica, était Jisija; des enfants de Jisija, Zacharie.
Mʼbale wa Mika: Isiya; kuchokera kwa ana a Isiya: Zekariya.
26 Des enfants de Mérari, Mahli, et Musi. Des enfants de Jahazija, son fils.
Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Mwana wa Yaaziya: Beno.
27 Des enfants [donc] de Mérari, de Jahazija, son fils, et Soham, Zaccur et Hibri.
Ana a Merari: Kuchokera kwa Yaaziya: Beno, Sohamu, Zakuri ndi Ibiri.
28 De Mahli, Eléazar, qui n'eut point de fils.
Kuchokera kwa Mahili: Eliezara, amene analibe ana aamuna.
29 De Kis, les enfants de Kis, Jérahméël.
Kuchokera kwa Kisi: Mwana wa Kisi: Yerahimeeli.
30 Et des enfants de Musi, Mahli, Héder, et Jérimoth. Ce sont là les enfants des Lévites, selon les maisons de leurs pères.
Ndipo ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yerimoti. Awa anali Alevi potsata mabanja a makolo awo.
31 Et ils jetèrent pareillement les sorts selon le nombre de leurs frères les enfants d'Aaron, en la présence du Roi David, de Tsadoc, et d'Ahimélec, et des Chefs des pères [des familles] des Sacrificateurs et des Lévites; les Chefs des pères [de famille] correspondant à leurs plus jeunes frères.
Iwonso anachita maere, monga anachitira abale awo, zidzukulu za Aaroni, pamaso pa mfumu Davide, ndi Zadoki ndi Ahimeleki, atsogoleri a mabanja a ansembe ndi Alevi. Mabanja a mwana wamkulu anachita nawo mofanana ndi a mwana wamngʼono.

< 1 Chroniques 24 >