< 1 Chroniques 11 >

1 Et tous ceux d'Israël s'assemblèrent auprès de David à Hébron, et [lui] dirent: Voici, nous sommes tes os, et ta chair.
Aisraeli onse anasonkhana pamaso pa Davide ku Hebroni ndipo anati, “Ife ndife abale anu.
2 Et même ci-devant, quand Saül était Roi, tu étais celui qui menais et qui ramenais Israël. Et l'Eternel ton Dieu t'a dit: Tu paîtras mon peuple d'Israël, et tu seras le Conducteur de mon peuple d'Israël.
Kale lija, ngakhale pamene Sauli anali mfumu, inu ndinu amene munkatsogolera Aisraeli pa nkhondo zawo. Ndipo Yehova Mulungu wanu anakuwuzani kuti, ‘Iwe udzaweta anthu anga Aisraeli, ndipo udzakhala mfumu yawo.’”
3 Tous les Anciens donc d'Israël vinrent vers le Roi à Hébron; et David traita alliance avec eux à Hébron devant l'Eternel; et ils oignirent David pour Roi sur Israël, suivant la parole que l'Eternel avait proférée par le moyen de Samuël.
Akuluakulu onse a Israeli atafika kwa Mfumu Davide ku Hebroni, iye anachita nawo pangano pamaso pa Yehova, ndipo anamudzoza Davide kukhala mfumu ya Israeli, monga momwe Yehova analonjezera kudzera mwa Samueli.
4 Or David et tous ceux d'Israël s'en allèrent à Jérusalem, qui est Jébus; car là étaient encore les Jébusiens qui habitaient au pays.
Davide ndi Aisraeli onse anapita ku Yerusalemu (ku Yebusi). Ayebusi amene ankakhala kumeneko
5 Et ceux qui habitaient à Jébus, dirent à David: Tu n'entreras point ici. Mais David prit la forteresse de Sion, qui est la Cité de David.
anamuwuza Davide kuti, “Simulowa muno.” Komabe Davide analanda linga la Ziyoni, limene ndi mzinda wa Davide.
6 Car David avait dit: Quiconque aura le premier frappé les Jébusiens, sera Chef et Capitaine. Et Joab fils de Tséruiä monta le premier, et fut fait Chef.
Davide anali atanena kuti “Aliyense amene adzatsogolere kukathira nkhondo Ayebusi adzakhala mkulu wa asilikali.” Yowabu mwana wa Zeruya ndiye anayamba kupita, motero anakhala mkulu wa asilikali.
7 Et David habita dans la forteresse; c'est pourquoi on l'appela la Cité de David.
Tsono Davide anakhazikika mu lingamo, ndipo mzindawu anawutcha Mzinda wa Davide.
8 Il bâtit aussi la ville tout alentour, depuis Millo jusqu'aux environs; mais Joab répara le reste de la ville.
Iye anamanga malo onse ozungulira, kuyambira ku matsitso ozungulira khoma. Ndipo Yowabu anakonzanso mbali ina ya mzindawu.
9 Et David allait toujours en avançant et en croissant; car l'Eternel des armées était avec lui.
Ndipo mphamvu za Davide zinkakulirakulira chifukwa anali ndi Yehova Wamphamvuzonse.
10 Ce sont ici les principaux des hommes forts que David avait, qui se portèrent vaillamment avec lui, [et] avec tout Israël, pour son Royaume, afin de le faire régner suivant la parole de l'Eternel touchant Israël.
Awa ndiye anali atsogoleri amphamvu a Davide. Iwo pamodzi ndi Aisraeli onse, anathandiza kulimbikitsa ufumu wake kuti ukwanire madera onse, monga momwe Yehova analonjezera.
11 Ceux-ci donc sont du nombre des hommes forts que David avait; Jasobham fils de Hacmoni, Chef entre les trois principaux, qui lançant sa hallebarde contre trois cents hommes, les blessa à mort en une seule fois.
Nawa mayina a ankhondo amphamvu a Davide: Yasobeamu Mhakimoni anali mkulu wa atsogoleri. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 300 nthawi imodzi.
12 Après lui était Eléazar fils de Dodo Ahohite, qui fut un des trois hommes forts.
Wotsatana naye anali Eliezara mwana wa Dodo Mwahohi, mmodzi mwa ankhondo atatu amphamvu.
13 Ce fut lui qui se trouva avec David à Pasdammim, lorsque les Philistins s'étaient assemblés pour combattre; or il y avait une partie d'un champ semée d'orge, et le peuple s'en était fui devant les Philistins.
Iye anali ndi Davide ku Pasi-Damimu pamene Afilisti anasonkhana kudzachita nkhondo. Ankhondo anathawa Afilistiwo pamalo pamene panali munda wodzaza ndi barele.
14 Et eux s'arrêtèrent au milieu de cette partie du champ, et la garantirent, et battirent les Philistins. Ainsi l'Eternel accorda une grande délivrance.
Koma awiriwo anayima pakati pa mundawo. Iwo anawuteteza, nakantha Afilistiwo ndipo Yehova anawapambanitsa koposa.
15 Il en descendit encore trois d'entre les trente Capitaines près du rocher, vers David, en la caverne de Hadullam, lorsque l'armée des Philistins était campée dans la vallée des Réphaïms.
Atatu mwa atsogoleri makumi atatu aja anabwera kwa Davide ku thanthwe ku phanga la Adulamu pamene gulu la Afilisti linali litamanga misasa mʼchigwa cha Refaimu.
16 Et David était alors dans la forteresse, et la garnison des Philistins était en ce même temps-là à Bethléhem.
Nthawi imeneyo Davide anali mu linga, ndipo boma la Afilisti linali ku Betelehemu.
17 Et David fit un souhait, et dit: Qui est-ce qui me ferait boire de l'eau du puits qui est à la porte de Bethléhem?
Davide analakalaka madzi ndipo anati, “Haa, pakanapezeka munthu wokanditungira madzi a mʼchitsime chomwe chili pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu!”
18 Alors ces trois hommes passèrent tout au travers du camp des Philistins, et puisèrent de l'eau du puits qui était à la porte de Bethléhem; et l'ayant apportée, la présentèrent à David, qui n'en voulut point boire, mais la répandit à l'honneur de l'Eternel.
Choncho anthu atatuwa anadutsa mizere ya Afilisti, natunga madzi amene anali mʼchitsime chomwe chinali pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu nabwera nawo kwa Davide. Koma iye anakana kumwa. Mʼmalo mwake anathira pansi pamaso pa Yehova.
19 Car il dit: A Dieu ne plaise que je fasse une telle chose! Boirais-je le sang de ces hommes [qui ont fait un tel voyage] au péril de leur vie; car ils m'ont apporté cette eau au péril de leur vie; ainsi il n'en voulut point boire. Ces trois vaillants hommes firent cette action-là.
Iye anati, “Inu Mulungu, musalole kuti ine ndichite chinthu ichi! Kodi ndimwe magazi a anthu amene anayika miyoyo yawo pachiswe?” Chifukwa iwo anayika miyoyo yawo pachiswe kuti abweretse madziwo, Davide sanamwe. Zimenezi ndi zimene anachita anthu amphamvu atatuwo.
20 Et Abisaï frère de Joab était Chef des trois, lequel lançant sa hallebarde contre trois cents hommes, les blessa à mort, et il fut célèbre entre les trois.
Abisai mʼbale wa Yowabu ndiye anali mtsogoleri wa anthu atatuwa. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 300. Choncho iyeyo anali wotchuka pakati pa anthu atatu aja.
21 Entre les trois il fut plus honoré que les deux autres, et il fut leur Chef; cependant il n'égala point ces trois autres.
Iye analandira ulemu woposa atatuwo. Kotero anakhala mtsogoleri wawo ngakhale kuti iyeyo sanali mʼgulu la anthu atatu aja.
22 Bénéja aussi fils de Jéhojadah, fils d'un vaillant homme de Kabtséël, avait fait de grands exploits. Il tua deux des plus puissants hommes de Moab; et il descendit et frappa un lion au milieu d'une fosse, en un jour de neige.
Benaya mwana wa Yehoyada wa ku Kabizeeli anali munthu wolimba mtima amene anachita zinthu zamphamvu. Iye anakantha ankhondo awiri otchuka a ku Mowabu. Tsiku lina kukuzizira kwambiri, iye analowa mʼdzenje ndi kuphamo mkango.
23 Il tua aussi un homme Egyptien qui était haut de cinq coudées. Cet Egyptien avait en sa main une hallebarde [grosse] comme une ensuble de tisserand; mais il descendit contre lui avec un bâton, et arracha la hallebarde de la main de l'Egyptien, et le tua de sa propre hallebarde.
Ndipo iye anakanthanso Mwigupto amene anali wotalika mamita awiri ndi theka. Ngakhale kuti Mwiguptoyo anali ndi mkondo wofanana ndi ndodo yowombera nsalu mʼdzanja mwake, Benaya anapita kukamenyana naye ali ndi chibonga chokha mʼmanja. Iye analanda mkondo mʼdzanja la Mwiguptoyo ndi kumupha ndi mkondo wake womwe.
24 Bénéja fils de Jéhojadah fit ces choses-là, et fut célèbre entre ces trois vaillants hommes.
Izi ndi zamphamvu zimene Benaya mwana wa Yehoyada anachita. Iyeyo analinso wotchuka ngati anthu atatu amphamvu aja.
25 Voilà, il était honoré plus que les trente; cependant il n'égala point ces trois-là; et David l'établit sur ses gens de commandement.
Iye ankalemekezedwa kuposa wina aliyense mwa anthu makumi atatu, koma sanali mʼgulu la anthu atatu aja. Ndipo Davide anamuyika kukhala woyangʼanira asilikali omuteteza.
26 Et les plus vaillants d'entre les gens de guerre furent, Hazaël, frère de Joab; et Elhanan fils de Dodo, de Bethléhem,
Ankhondo amphamvuwa anali: Asaheli mʼbale wa Yowabu, Elihanani mwana wa Dodo wa ku Betelehemu,
27 Sammoth Harorite, Helets Pelonien,
Samoti Mharori, Helezi Mpeloni.
28 Hira fils de Hikkes Tékohite, Abihézer Hanathothite,
Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa, Abiezeri wa ku Anatoti,
29 Sibbécaï Husathite, Hilaï Ahohite,
Sibekai Mhusati, Ilai Mwahohi,
30 Maharaï Nétophathite, Héled fils de Bahana Nétophathite,
Maharai Mnetofa, Heledi mwana wa Baana Mnetofa,
31 Ithaï fils de Ribaï, de Guibha des enfants de Benjamin, Bénéja Pirhathonite,
Itai mwana wa Ribai wa ku Gibeya ku Benjamini, Benaya Mpiratoni,
32 Huraï des vallées de Gahas, Abiël Harbathite,
Hurai wa ku zigwa za Gaasi, Abieli Mwaribati,
33 Hazmaveth Baharumite, Eliachba Sahalbonite,
Azimaveti Mbaharumi, Eliyahiba Msaaliboni,
34 Des enfants de Hasen Guizonite, Jonathan fils de Sagué Hararite,
ana a Hasemu Mgizoni, Yonatani mwana wa Sage Mharari,
35 Ahiam fils de Sacar Hararite, Eliphal fils d'Ur,
Ahiamu mwana wa Sakari Mharari, Elifali mwana wa Uri,
36 Hépher Mékérathite, Ahija Pélonien,
Heferi Mmekerati, Ahiya Mpeloni,
37 Hetsro de Carmel, Naharaï fils d'Ezbaï,
Heziro wa ku Karimeli Naara mwana wa Ezibai,
38 Joël frère de Nathan, Mibhar fils de Hagri,
Yoweli mʼbale wa Natani, Mibihari mwana wa Hagiri,
39 Tselek Hammonite, Naharaï Bérothite, qui portait les armes de Joab fils de Tséruiä,
Zeleki Mwamoni, Naharai wa ku Beeroti, mnyamata wonyamula zida za Yowabu mwana wa Zeruya.
40 Hira Jithrite, Gareb Jithrite,
Ira Mwitiri, Garebu Mwitiri,
41 Urie Héthien, Zabad fils d'Ahlaï,
Uriya Mhiti, Zabadi mwana wa Ahilai,
42 Hadina fils de Siza Rubénite, Chef des Rubénites, et trente avec lui.
Adina mwana wa Siza Mrubeni, amene anali mtsogoleri wa Arubeni ndi anthu makumi atatu pamodzi naye,
43 Hanan fils de Mahaca, et Josaphat Mithnite,
Hanani mwana wa Maaka, Yehosafati Mmitini,
44 Huzija Hastérathite, Samah et Jéhiël fils de Hotham Harohérite,
Uziya Mwasiterati, Sama ndi Yeiyeli ana a Hotamu Mwaroeri,
45 Jédihaël fils de Simri, et Joha son frère, Titsite,
Yediaeli mwana wa Simiri, ndi Yoha Mtizi mʼbale wake,
46 Eliël Hammahavim, Jéribaï, et Josavia enfants d'Elnaham, et Jithma Moabite,
Elieli Mhavati, Yeribai ndi Yosaviya ana a Elinaamu, Itima Mmowabu,
47 Eliël, et Hobed, et Jasiël de Metsobaja.
Elieli, Obedi ndi Yaasieli Mmeobai.

< 1 Chroniques 11 >