< Lévitique 10 >

1 Les fils d’Aaron, Nadab et Abihu, prirent chacun un brasier, y mirent du feu, et posèrent du parfum dessus; ils apportèrent devant l’Éternel du feu étranger, ce qu’il ne leur avait point ordonné.
Ana a Aaroni, Nadabu ndi Abihu, aliyense anatenga chofukizira lubani chake nayikamo makala a moto ndi kuthiramo lubani. Iwo anapereka pamaso pa Yehova moto wachilendo, moto umene Yehova sanawalamule.
2 Alors le feu sortit de devant l’Éternel, et les consuma: ils moururent devant l’Éternel.
Choncho moto unatuluka pamaso pa Yehova ndi kuwapsereza, ndipo anafa pamaso pa Yehova.
3 Moïse dit à Aaron: C’est ce que l’Éternel a déclaré, lorsqu’il a dit: Je serai sanctifié par ceux qui s’approchent de moi, et je serai glorifié en présence de tout le peuple. Aaron garda le silence.
Pamenepo Mose anawuza Aaroni kuti, “Pajatu Yehova ananena kuti, “‘Kwa iwo amene amandiyandikira ndidzaonetsa ulemerero wanga; pamaso pa anthu onse ndidzalemekezedwa.’” Aaroni anakhala chete wosayankhula.
4 Et Moïse appela Mischaël et Eltsaphan, fils d’Uziel, oncle d’Aaron, et il leur dit: Approchez-vous, emportez vos frères loin du sanctuaire, hors du camp.
Mose anayitana Misaeli ndi Elizafani, ana a Uzieli, abambo angʼono a Aaroni, ndipo anawawuza kuti, “Bwerani kuno mudzachotse abale anuwa pa malo wopatulika ndi kuwatulutsira kunja kwa msasa.”
5 Ils s’approchèrent, et ils les emportèrent dans leurs tuniques hors du camp, comme Moïse l’avait dit.
Choncho anabwera atavala minjiro yawo ndipo anawatenga ndi kuwatulutsa kunja kwa msasawo monga momwe Mose analamulira.
6 Moïse dit à Aaron, à Éléazar et à Ithamar, fils d’Aaron: Vous ne découvrirez point vos têtes, et vous ne déchirerez point vos vêtements, de peur que vous ne mouriez, et que l’Éternel ne s’irrite contre toute l’assemblée. Laissez vos frères, toute la maison d’Israël, pleurer sur l’embrasement que l’Éternel a allumé.
Ndipo Mose anawuza Aaroni ndi ana ake Eliezara ndi Itamara kuti, “Musalileke tsitsi lanu nyankhalala ndipo musangʼambe zovala zanu kuti mungafe, ndi mkwiyo wa Yehova ungagwere anthu onsewa. Koma abale anu okha, kutanthauza fuko lonse la Israeli ndiwo ayenera kulira omwalira aja amene Yehova wawapsereza ndi moto.
7 Vous ne sortirez point de l’entrée de la tente d’assignation, de peur que vous ne mouriez; car l’huile de l’onction de l’Éternel est sur vous. Ils firent ce que Moïse avait dit.
Musatuluke kunja kwa tenti ya msonkhano, mungafe, chifukwa munadzozedwa ndi mafuta a Yehova kukhala ansembe.” Choncho iwo anachita monga Mose ananenera.
8 L’Éternel parla à Aaron, et dit:
Pambuyo pake Yehova anayankhula ndi Aaroni nati,
9 Tu ne boiras ni vin, ni boisson enivrante, toi et tes fils avec toi, lorsque vous entrerez dans la tente d’assignation, de peur que vous ne mouriez: ce sera une loi perpétuelle parmi vos descendants,
“Iwe ndi ana ako musamamwe vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa pamene mukulowa mu tenti ya msonkhano kuti mungafe. Ili ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse.
10 afin que vous puissiez distinguer ce qui est saint de ce qui est profane, ce qui est impur de ce qui est pur,
Muzisiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba, pakati pa zinthu zodetsedwa ndi zinthu zoyeretsedwa,
11 et enseigner aux enfants d’Israël toutes les lois que l’Éternel leur a données par Moïse.
ndipo muyenera kuphunzitsa Aisraeli onse malamulo amene Yehova wakupatsani kudzera mwa Mose.”
12 Moïse dit à Aaron, à Éléazar et à Ithamar, les deux fils qui restaient à Aaron: Prenez ce qui reste de l’offrande parmi les sacrifices consumés par le feu devant l’Éternel, et mangez-le sans levain près de l’autel: car c’est une chose très sainte.
Mose anawuza Aaroni ndi ana ake otsalawo, Eliezara ndi Itamara kuti, “Tengani zopereka zachakudya zopanda yisiti zimene zatsala pa nsembe zopsereza za kwa Yehova ndipo muzidye pafupi ndi guwa pakuti ndi zopatulika kwambiri.
13 Vous le mangerez dans un lieu saint; c’est ton droit et le droit de tes fils sur les offrandes consumées par le feu devant l’Éternel; car c’est là ce qui m’a été ordonné.
Muzidye pa malo wopatulika chifukwa zimenezi ndi gawo lako ndi la ana ako pa zopereka zopsereza kwa Yehova. Izitu ndi zimene Yehova anandilamulira.
14 Vous mangerez aussi dans un lieu pur, toi, tes fils et tes filles avec toi, la poitrine qu’on a agitée de côté et d’autre et l’épaule qui a été présentée par élévation; car elles vous sont données, comme ton droit et le droit de tes fils, dans les sacrifices d’actions de grâces des enfants d’Israël.
Koma iwe pamodzi ndi ana ako aamuna ndi aakazi muzidya chidale chimene chinaweyulidwa ndi ntchafu zimene zinaperekedwa nsembe. Muzidye pamalo woyeretsedwa. Zimenezi zaperekedwa kwa iwe ndi ana ako monga gawo lanu pa zopereka zachiyanjano zimene apereka Aisraeli.
15 Ils apporteront, avec les graisses destinées à être consumées par le feu, l’épaule que l’on présente par élévation et la poitrine que l’on agite de côté et d’autre devant l’Éternel: elles seront pour toi et pour tes fils avec toi, par une loi perpétuelle, comme l’Éternel l’a ordonné.
Ntchafu imene inaperekedwayo ndi chidale chomwe chinaweyulidwacho abwere nazo pamodzi ndi nsembe ya mafuta ya Yehova yotentha pa moto, ndipo uziweyule kuti zikhale zopereka zoweyula pamaso pa Yehova. Zimenezi zizikhala zako ndi ana ako nthawi zonse monga walamulira Yehova.”
16 Moïse chercha le bouc expiatoire; et voici, il avait été brûlé. Alors il s’irrita contre Éléazar et Ithamar, les fils qui restaient à Aaron, et il dit:
Pambuyo pake Mose anafunafuna mbuzi ya nsembe yopepesera machimo koma anapeza kuti anayitentha kale. Apa Mose anakalipira Eliezara ndi Itamara, ana a Aaroni otsala aja nati,
17 Pourquoi n’avez-vous pas mangé la victime expiatoire dans le lieu saint? C’est une chose très sainte; et l’Éternel vous l’a donnée, afin que vous portiez l’iniquité de l’assemblée, afin que vous fassiez pour elle l’expiation devant l’Éternel.
“Chifukwa chiyani simunadyere pamalo wopatulika nsembe yopepesera machimo ija? Kodi imene ija siyopatulika? Kodi Yehova sanapereke nyamayo kwa inu kuti muchotse machimo a mpingo wonse powachitira mwambo wa nsembe yopepesera machimo pamaso pa Yehova?
18 Voici, le sang de la victime n’a point été porté dans l’intérieur du sanctuaire; vous deviez la manger dans le sanctuaire, comme cela m’avait été ordonné.
Pakuti magazi ake sanalowe nawo ku Malo Wopatulika, mukanadya nyama ya mbuziyo pa malo wopatulikawo monga Yehova analamulira.”
19 Aaron dit à Moïse: Voici, ils ont offert aujourd’hui leur sacrifice d’expiation et leur holocauste devant l’Éternel; et, après ce qui m’est arrivé, si j’eusse mangé aujourd’hui la victime expiatoire, cela aurait-il été bien aux yeux de l’Éternel?
Aaroni anamuyankha Mose kuti, “Lero anthu apereka nsembe yawo yopepesera machimo ndiponso nsembe yawo yopsereza pamaso pa Yehova komabe zinthu zoterezi zandichitikira. Kodi Yehova akanakondwa ndikanadya nsembe yopepesera machimo lero?”
20 Moïse entendit et approuva ces paroles.
Pamene Mose anamva zimenezi, anakhutira.

< Lévitique 10 >