< Psaumes 94 >

1 Psaume de David pour le quatrième jour de la semaine. Le Seigneur Dieu des vengeances, le Dieu des vengeances a agi librement.
Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango, Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.
2 Lève-toi, ô toi qui juge la terre, rétribue les superbes comme ils le méritent.
Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi; bwezerani kwa odzikuza zowayenera.
3 Jusques à quand, mon Dieu, subsisteront les pécheurs; jusques à quand les pécheurs se glorifieront-ils?
Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova, mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?
4 Ils parleront, et ils diront des choses iniques; ainsi parleront tous les ouvriers d'iniquité.
Amakhuthula mawu onyada; onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.
5 Seigneur, ils ont humilié ton peuple, et ils ont tourmenté ton héritage.
Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova; amapondereza cholowa chanu.
6 Ils ont tué la veuve et l'orphelin, et ils ont mis à mort l'étranger.
Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko; amapha ana amasiye.
7 Et ils ont dit: Le Seigneur ne le verra pas; le Dieu de Jacob ne s'en apercevra point.
Iwo amati, “Yehova sakuona; Mulungu wa Yakobo salabadirako.”
8 Comprenez maintenant, peuples fous et sans raison; soyez sages enfin.
Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu; zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?
9 Celui qui a créé l'oreille n'entendra-t-il pas? Celui qui a créé l'œil ne verra-t-il point?
Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva? Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?
10 Celui qui châtie les nations ne punira-t-il pas, lui qui apprend la science à l'homme?
Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga? Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?
11 le Seigneur connaît les pensées des hommes, et il sait qu'elles sont vaines.
Yehova amadziwa maganizo a munthu; Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.
12 Seigneur, heureux l'homme que toi-même tu as instruit, et à qui tu enseigneras ta loi,
Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza, munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;
13 Pour le traiter avec douceur après les mauvais jours, jusqu'à ce que soit creusée la fosse du pécheur.
mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto, mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.
14 Car le Seigneur ne répudiera pas son peuple; et il ne délaissera pas son héritage,
Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake; Iye sadzasiya cholowa chake.
15 Jusqu'à ce que sa justice apparaisse dans le jugement, et qu'il en fasse jouir tous ceux qui ont le cœur droit.
Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo, ndipo onse olungama mtima adzachitsata.
16 Qui s'élèvera pour moi contre les pécheurs, ou qui m'assistera contre les ouvriers d'iniquité?
Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa? Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?
17 Si le Seigneur ne m'eût aidé, peu s'en est fallu que mon âme n'ait habité l'enfer. (questioned)
Yehova akanapanda kundithandiza, bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.
18 Si je disais: Mon pied a été ébranlé, ta miséricorde me secourait, Seigneur.
Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,” chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.
19 Seigneur, ton amour a consolé mon âme, selon la multitude de mes douleurs.
Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga, chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.
20 Le siège de l'iniquité peut-il se dresser près de toi, quand tu attaches la peine à tes préceptes?
Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?
21 Il tendront des filets pour prendre l'âme des justes, et ils condamneront le sang innocent.
Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.
22 Mais le Seigneur est devenu pour moi un refuge, et mon Dieu est l'appui de mon espérance.
Koma Yehova wakhala linga langa, ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.
23 Et il rétribuera leur injustice et leur méchanceté; le Seigneur notre Dieu les punira.
Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo; Yehova Mulungu wathu adzawawononga.

< Psaumes 94 >