< Psaumes 58 >

1 Jusqu'à la Fin, avec cette inscription de David: Ne détruis pas. O fils des hommes, si vous parlez sincèrement de la justice, jugez donc avec droiture.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Kodi inu olamulira mumayankhuladi molungama? Kodi mumaweruza mwachilungamo pakati pa anthu?
2 Car vous faites en votre cœur des iniquités sur la terre, et vos mains trament l'injustice.
Ayi, mʼmitima mwanu mumakonzekera zosalungama, ndipo manja anu amatulutsa zachiwawa pa dziko lapansi.
3 Dès le sein de leur mère, les pécheurs ont dévié; à peine hors de ses entrailles, ils se sont égarés; ils ont dit des mensonges.
Ngakhale kuchokera tsiku lawo lobadwa oyipa amasochera; kuchokera mʼmimba ya amayi awo, iwo ndi otayika ndipo amayankhula mabodza.
4 Leur colère est comme le venin du serpent, ou du sourd aspic, dont les oreilles sont bouchées,
Ululu wawo uli ngati ululu wa njoka, ngati uja wa mphiri imene yatseka mʼmakutu mwake.
5 Qui n'entendra point la voix des enchanteurs, et résistera aux charmes les plus subtils.
Imene simva liwu la munthu wamatsenga, ngakhale akhale wa luso lotani munthu wamatsengayo.
6 Dieu leur a brisé les dents dans la bouche; le Seigneur a broyé la mâchoire des lions.
Gululani mano mʼkamwa mwawo, Inu Mulungu, Yehova khadzulani mano a mikango!
7 Ils s'écouleront comme un flot qui passe; le Seigneur tiendra son arc tendu contre eux, jusqu'à ce qu'ils aient péri.
Mulole kuti asowe ngati madzi oyenda pamene iwo akoka uta mulole kuti mivi yawo ikhale yosathwa.
8 Ils seront réduits à rien, comme la cire qui se fond; le feu est tombé sur eux, ils n'ont plus vu le soleil.
Akhale ngati nkhono imene imasungunuka pamene ikuyenda; ngati mwana wakufa asanabadwe, iwo asaone dzuwa.
9 Avant que vos épines approchent de la hauteur d'un arbrisseau, le Seigneur vous dévorera même pleins de vie, dans l'excès de sa colère.
Miphika yanu isanagwire moto waminga ya mkandankhuku, kaya iyo ndi yobiriwira kapena yowuma, oyipa adzachotsedwa.
10 Le juste se réjouira, lorsqu'il verra la punition des impies; il se lavera les mains dans le sang des pécheurs.
Olungama adzasangalala poona kubwezera chilango, pamene adzasambitsa mapazi awo mʼmagazi a anthu oyipa.
11 Et l'on dira: Puisqu'il y a des fruits pour les justes, il est donc un Dieu qui les juge sur la terre.
Ndipo anthu adzanena kuti, “Zoonadi, olungama amalandirabe mphotho; zoonadi kuli Mulungu amene amaweruza dziko lapansi.”

< Psaumes 58 >