< Psaumes 34 >

1 Psaume de David, quand il changea de contenance devant Abimélech, qui le laissa partir, et il partit. En tout temps je bénirai le Seigneur; sa louange sera en tout temps dans ma bouche.
Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka. Ndidzayamika Yehova nthawi zonse; matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
2 Mon âme se réjouira dans le Seigneur; que les doux écoutent et se réjouissent.
Moyo wanga udzanyadira Yehova; anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
3 Glorifiez avec moi le Seigneur, et exaltons son nom tous ensemble.
Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine; tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
4 J'ai cherché le Seigneur, et il m'a exaucé; il m'a tiré de toutes mes afflictions.
Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha; anandilanditsa ku mantha anga onse.
5 Approchez-vous de lui, éclairez-vous de sa lumière, et vos faces ne seront point confondues.
Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira; nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
6 Le pauvre a crié et le Seigneur l'a exaucé, et il l'a délivré de toutes ses afflictions.
Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva; Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
7 L'ange du Seigneur veillera autour de ceux qui craignent Dieu, et il les sauvera.
Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye ndi kuwalanditsa.
8 Goûtez et voyez combien le Seigneur est doux; heureux l'homme qui espère en lui.
Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino; wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
9 Craignez le Seigneur, vous tous qui êtes ses saints; car rien ne manque à ceux qui le craignent.
Wopani Yehova inu oyera mtima ake, pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
10 Les riches sont devenus pauvres et ils ont eu faim; mais ceux qui cherchent le Seigneur ne manqueront d'aucun bien. Interlude.
Mikango itha kulefuka ndi kumva njala koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
11 Venez, enfants, écoutez-moi; je vous enseignerai la crainte du Seigneur.
Bwerani ana anga, mundimvere; ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
12 Quel est l'homme qui veut la vie, qui désire voir des jours heureux?
Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
13 Que sa langue s'abstienne du mal, et ses lèvres du mensonge.
asunge lilime lake ku zoyipa ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
14 Détourne-toi du mal, et fais le bien; cherche la paix et la poursuis.
Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; funafuna mtendere ndi kuwulondola.
15 Les yeux du Seigneur sont sur les justes, et ses oreilles vers leurs prières.
Maso a Yehova ali pa olungama ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
16 Le visage du Seigneur est tourné contre ceux qui font le mal, pour effacer de la terre leur souvenir.
nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa, kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
17 Les justes ont crié, et le Seigneur les a exaucés; et il les a délivrés de toutes leurs afflictions.
Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva; Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
18 Le Seigneur est près de ceux dont le cœur est affligé; il sauvera les humbles d'esprit.
Yehova ali pafupi kwa osweka mtima ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
19 Les afflictions du juste sont nombreuses, et de toutes le Seigneur le délivrera.
Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri, Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
20 Le Seigneur garde tous leurs os, pas un seul ne sera broyé.
Iye amateteza mafupa ake onse, palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
21 La mort des pécheurs est leur grand malheur, et ceux qui haïssent le juste périront.
Choyipa chidzapha anthu oyipa; adani a olungama adzapezeka olakwa.
22 Le Seigneur affranchira les âmes de ceux qui le servent, et ceux qui espèrent en lui ne défailliront pas.
Yehova amawombola atumiki ake; aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.

< Psaumes 34 >