< Proverbes 20 >

1 Le vin est déréglé, et l'ivresse insolente; l'insensé se laisse prendre dans leurs filets;
Vinyo amachititsa munthu kukhala wonyoza ndipo chakumwa choledzeretsa chimachititsa munthu kukhala wolongolola; aliyense wosochera nazo zimenezi alibe nzeru.
2 La menace d'un roi ne diffère point de la colère du lion; celui qui le provoque pèche contre sa propre vie.
Ukali wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango; amene amawuputa mkwiyowo amataya moyo wake.
3 C'est une gloire pour un homme de se détourner des contestations; au contraire, le fou s'y laisse prendre.
Nʼchaulemu kwa munthu kupewa mikangano, koma chitsiru chilichonse chimafulumira kulongolola.
4 Le paresseux, quand on le blâme, n'en a point honte; il en est de même de celui qui emprunte du blé à usure pendant la moisson.
Munthu waulesi satipula mʼmunda pa nthawi yoyenera; kotero pa nthawi yokolola adzafunafuna zinthu koma sadzapeza kanthu kalikonse.
5 Le conseil dans le cœur de l'homme est une eau profonde; l'homme prudent y saura puiser.
Zolinga za mtima wa munthu zili ngati madzi akuya, munthu womvetsa zinthu ndiye yekha angawatunge.
6 Un homme est une grande chose; un homme miséricordieux est un trésor; mais un homme fidèle est difficile à trouver.
Anthu ambiri amayankhula za kukhulupirika kwawo, koma munthu wokhulupirika angamupeze ndani?
7 L'homme irréprochable qui se tourne vers la justice laissera ses enfants heureux.
Munthu wolungama amakhala ndi makhalidwe abwino; odala ndi ana ake amene amatsanzira moyo wake.
8 Lorsqu'un roi juste s'est assis sur son trône, nul mal ne résiste à ses regards.
Mfumu ikhala pa mpando wake wa chiweruzo, imapeta ndi maso ake anthu onse oyipa.
9 Qui peut se vanter d'avoir le cœur chaste? Qui osera dire: Je suis pur de tout péché?
Ndani amene anganene kuti, “Ndawuyeretsa mtima wanga; ndilibe tchimo lililonse?”
10 Avoir deux poids et deux mesures, et en faire usage: deux choses infâmes devant le Seigneur.
Masikelo ndi miyeso ya zinthu imene ili yachinyengo zonsezi Yehova zimamunyansa.
11 Le jeune homme en compagnie d'un saint sera réservé dans ses mœurs, et sa voie sera droite.
Ngakhale mwana amadziwika ndi zochita zake, ngati zochita zake zili zoyera ndi zoyenera.
12 L'oreille entend, et l'œil voit; l'un et l'autre sont l'œuvre du Seigneur.
Makutu amene amamva ndi maso amene amaona, zonsezi anazilenga ndi Yehova.
13 Ne te plais pas à médire, si tu ne veux être chassé. Ouvre les yeux, et rassasie-toi de pain.
Usakonde tulo ungasauke; khala maso ndipo udzakhala ndi chakudya chambiri.
Munthu wogula chinthu amati, “Sichabwino, sichabwino.” Koma akagula nʼkuchokapo amayamba kudzitama.
Pali golide ndi miyala yamtengowapatali, koma milomo yoyankhula zanzeru ndi yamtengowapatali koposa zonsezi.
Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; kuti chikhale chikole chako chifukwa waperekera chikole munthu wachilendo.
Chakudya chochipeza mwachinyengo chimukomera munthu, koma pa mapeto pake chimasanduka ngati mchenga mʼkamwa mwake.
Zokonzekera zimapindula utafunsira uphungu; ndipo usanamenye nkhondo yamba wapempha malangizo oyenera.
Amene amanka nanena miseche amawulula zachinsinsi. Choncho usamagwirizane naye munthu woyankhula zopusayo.
20 La lampe de celui qui décrie son père ou sa mère s'éteindra; les prunelles de ses yeux verront les ténèbres.
Ngati munthu atemberera abambo ake kapena amayi ake, moyo wake udzazimitsidwa ngati nyale mu mdima wandiweyani.
21 Le bien acquis tout d'abord à la hâte, à la fin ne sera pas béni.
Cholowa chochipeza mofulumira poyamba, sichidzakhala dalitso pa mapeto pake.
22 Garde-toi de dire: Je me vengerai de mon ennemi; mais attends le Seigneur, afin qu'Il te seconde.
Usanene kuti, “Ine ndidzabwezera choyipa chimenechi!” Dikira Yehova, ndipo Iye adzakupulumutsa.
23 Le double poids est en abomination au Seigneur, et les fausses balances ne sont point bonnes à Ses yeux.
Miyeso yosintha imamunyansa Yehova; ndipo masikelo onyenga si abwino.
24 La marche d'un homme est maintenue droite par le Seigneur; car comment un mortel discernerait-il ses voies?
Mayendedwe a munthu amawalamulira ndi Yehova, tsono munthu angadziwe bwanji njira yake?
25 L'homme tombe dans un piège, quand il se hâte trop de consacrer ses biens; car après le vœu vient le repentir.
Ndi msampha kwa munthu kuyankhula mofulumira kuti “Chinthu ichi nʼchopatulika kwa Yehova,” popeza mwina atha kusintha maganizo utalumbira kale.
26 Un roi sage est le vanneur des impies, et il fait passer sur eux une roue.
Mfumu ya nzeru imapeta kwathunthu anthu oyipa.
27 L'esprit de l'homme est une lumière du Seigneur, qui éclaire jusqu'au fonds des entrailles.
Mpweya wa munthu uli ngati nyale ya Yehova; imafufuza ziwalo zake zonse zamʼkati.
28 La miséricorde et la vérité sont la garde du roi, et avec la justice elles font cercle autour de son trône.
Kukoma mtima ndi kukhulupirika ndizo zimasunga mfumu; chilungamo chimalimbikitsa mpando wake waufumu.
29 L'ornement des jeunes gens c'est la sagesse; la parure des vieillards, ce sont leurs cheveux qui grisonnent.
Ulemerero wa achinyamata uli mu mphamvu zawo, imvi ndi ulemerero wa anthu okalamba.
30 Les confusions et les blessures sont le partage des méchants; ils ont des plaies jusqu'au fond des entrailles.
Mikwingwirima yopweteka ndiyo imachotsa zoyipa, ndipo mikwapulo ndiyo imachotsa zamʼkatikati mwa munthu.

< Proverbes 20 >