< Nombres 4 >

1 Et le Seigneur parla à Moïse et à Aaron, disant:
Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni:
2 Prends, parmi les fils de Lévi, le total des fils de Caath, par branches, par maisons paternelles,
“Werengani Akohati omwe ndi gawo limodzi la Alevi monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo.
3 Depuis vingt-cinq ans et au-dessus jusqu'à cinquante, de tous ceux qui entrent pour le service divin, et pour faire toutes les œuvres du tabernacle du témoignage.
Werengani amuna onse amene ali ndi zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu amene amabwera kudzagwira ntchito mu tenti ya msonkhano.
4 Voici le ministère des fils de Caath dans le tabernacle du témoignage et le Saint des saints.
“Ntchito ya Akohati mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kusamalira zinthu zopatulika kwambiri.
5 Lorsque Israël lèvera le camp, Aaron et ses fils entreront dans le tabernacle, et ils détendront le voile intérieur, et ils envelopperont l'arche.
Pamene anthu akusamuka pa msasa, Aaroni ndi ana ake aamuna azilowa mu tenti ndi kuchotsa chinsalu chotchingira ndi kuphimba nacho bokosi la umboni.
6 Ils placeront par-dessus une couverture de peaux bleues, et par-dessus encore ils jetteront un voile bleu, puis, ils passeront les leviers;
Ndipo azikuta bokosilo ndi zikopa za akatumbu ndi kuyala pamwamba pake nsalu ya mtundu wa thambo ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.
7 Et sur la table de proposition, ils étendront une nappe pourpre, sur laquelle ils mettront les plats, les encensoirs, les urnes, les coupes à libations, avec les pains qui sont toujours exposés sur cette table.
“Pa tebulo pamene pamakhala buledi wa ansembe aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo, ndipo aziyikapo mbale, mabeseni, zipande ndi mitsuko yoperekera nsembe yachakumwa. Aziyikaponso buledi wokhala pamenepo nthawi zonse.
8 Ils jetteront par-dessus une nappe écarlate qu'ils envelopperont d'une couverture de peaux bleues, et ils passeront les leviers.
Tsono pamwamba pa izi aziyalapo nsalu yofiira, ndi kuzikuta mʼzikopa za akatumbu ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.
9 Ils prendront ensuite une nappe bleue, et ils en envelopperont le chandelier, les lampes, les pincettes, les burettes et tous les vases à l'huile qui servent à leurs fonctions saintes;
“Azitenga nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira choyikapo nyale, pamodzi ndi nyale zake, zopanira zake, zotengera zake ndi mitsuko yonse yosungiramo mafuta.
10 Et ils déposeront le chandelier avec tous ses accessoires dans une couverture de peaux bleues, et ils le placeront sur des brancards.
Kenaka achikulunge pamodzi ndi zipangizo zake zonse mʼzikopa za akatumbu ndi kuchiyika pa chonyamulira chake.
11 Sur l'autel d'or, ils étendront une nappe bleue, et par-dessus une couverture de peaux couleur d'hyacinthe; puis ils passeront les leviers.
“Pamwamba pa guwa la golide aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira ndi zikopa za akatumbu ndi kuyika mʼmalo mwake mitengo yonyamulira.
12 Ils prendront tous les vases, tous les instruments liturgiques employés dans le sanctuaire, et ils les déposeront sur une nappe bleue, puis, ils les envelopperont d'une couverture de peaux, et ils les placeront sur des brancards.
“Azitenga zipangizo zonse zogwiritsira ntchito ku malo wopatulika, azizikulunga mʼnsalu ya mtundu wa thambo, azizikuta ndi zikopa za akatumbu ndi kuziyika pa zonyamulira zake.
13 Ils mettront aussi le couvercle sur l'autel des holocaustes, et ils le couvriront d'une nappe pourpre.
“Azichotsa phulusa la pa guwa lansembe lamkuwa ndi kuyalapo nsalu yapepo pamwamba pake.
14 Et ils y placeront tous les vases employés dans la liturgie, les foyers, les crochets, les coupes, le couvercle, tout l'ameublement de l'autel; ils les envelopperont d'une couverture de peaux bleues, puis, ils passeront les leviers. Et ils prendront une nappe pourpre, et ils en envelopperont le réservoir avec sa base qu'ils poseront dans une couverture de peaux bleues, et ils le mettront sur des brancards.
Kenaka aziyikapo zipangizo zonse zogwiritsira ntchito potumikira pa guwa, kuphatikizapo miphika yowotchera nyama, mafoloko otengera nyama, zowolera phulusa ndi mbale zowazira magazi pa guwa lansembe ndipo pamwamba pake aziyalapo zikopa za akatumbu ndi kuziyika mʼzonyamulira zake.
15 Et lorsque, aux levers du camp, Aaron et ses fils auront achevé d'envelopper les choses saintes, ainsi que tous les vases sacrés, les fils de Caath entreront dans le tabernacle pour les enlever, et ils ne toucheront pas aux choses saintes, s'ils ne veulent pas mourir; les fils de Caath les transporteront ensuite hors du tabernacle du témoignage.
“Aaroni ndi ana ake aamuna akamaliza kukutira ziwiya za ku malo wopatulika ndi zipangizo zopatulika zonse, ndipo akakonzeka kusamuka pamalopo, Akohati abwere kudzazinyamula koma asagwire zinthu zopatulikazo. Akatero adzafa. Izi ndizo zinthu zimene Akohati ayenera kunyamula mu tenti ya msonkhano.
16 Eléazar, fils du grand prêtre Aaron, veillera à l'huile du chandelier, à l'encens composé, aux sacrifices quotidiens, et à l'huile de l'onction; il aura l'inspection du tabernacle entier et de tout ce qu'il contient à l'usage des œuvres saintes.
“Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe, aziyangʼanira mafuta a nyale, ndi lubani wa nsembe zofukiza, nsembe yaufa yoperekedwa nthawi zonse ndi mafuta odzozera. Aziyangʼaniranso chihema ndi zonse zili mʼmenemo, kuphatikizapo zida ndi ziwiya zonse zopatulika.”
17 Et le Seigneur parla à Moïse et à Aaron, disant:
Yehova anawuzanso Mose ndi Aaroni kuti,
18 Gardez-vous d'exposer à périr, parmi la tribu de Lévi, la famille de Caath.
“Onetsetsani kuti mabanja a fuko la Kohati asachotsedwe kwa Alevi.
19 Faites ce que je vais dire, et ils vivront; ils ne mourront pas lorsqu'ils s'approcheront du Saint des saints: qu'Aaron et ses fils les précèdent et les placent chacun à son brancard.
Koma muziwachitira izi kuti asafe, akhalebe ndi moyo pamene ayandikira zinthu za ku malo wopatulika kwambiri: Aaroni ndi ana ake aamuna azipita ku malo wopatulika ndi kumamupatsa munthu aliyense ntchito yake ndi zimene ayenera kunyamula.
20 Et qu'ils n'entrent pas de manière à voir soudain les choses saintes, car ils mourraient.
Koma Akohati asalowe kukaona zinthu zopatulika, ngakhale kanthawi pangʼono, chifukwa akatero adzafa.”
21 Le Seigneur dit aussi à Moïse:
Yehova anawuza Mose kuti,
22 Prends le total des fils de Gerson par maisons paternelles, par branches,
“Werenganso Ageresoni monga mwa mabanja ndi mafuko awo.
23 Depuis vingt-cinq ans et au-dessus jusqu'à cinquante, de tous ceux qui entrent dans le tabernacle du témoignage, pour le service divin et pour faire leurs œuvres.
Uwerenge amuna onse a zaka makumi atatu mpaka a zaka makumi asanu zakubadwa amene amabwera kudzatumikira ku tenti ya msonkhano.
24 Voici le ministère de la famille des fils de Gerson: servir et enlever.
“Ntchito ya mafuko a Ageresoni pamene akugwira ntchito ndi kunyamula katundu ndi iyi:
25 Ils enlèveront les couvertures du tabernacle et le tabernacle du témoignage lui-même, sa première couverture et la couverture bleue d'en haut, avec le voile de l'entrée du tabernacle du témoignage,
Azinyamula makatani a ku chihema, tenti ya msonkhano, zokutira zake ndi zokutira kunja za zikopa za akatumbu, makatani a pa khomo la ku tenti ya msonkhano,
26 Et les tentures du parvis qui l'entourent; ils prendront soin aussi de tous les instruments liturgiques se rapportant à leur service.
makatani wotchingira bwalo lozungulira chihema ndi guwa, katani ya pa khomo, zingwe ndi zida zonse zimene zimagwiritsidwa ntchito mʼchihema. Ageresoni azichita zonse zofunika kuchitika ndi zinthu zimenezi.
27 Le ministère des fils de Gerson, en tous leurs devoirs et en toutes leurs œuvres, s'exercera sous la direction d'Aaron et de ses fils, et tu noteras, en prenant les noms de chacun, toutes les choses qu'ils enlèveront.
Ntchito yawo yonse, kaya kunyamula kapena kugwira ntchito zina, achite Ageresoni motsogozedwa ndi Aaroni ndi ana ake aamuna. Uwagawire ntchito zonse zimene akuyenera kugwira.
28 Tel est le ministère des fils de Gerson dans le tabernacle du témoignage, et ils l'exerceront sous la direction d'Ithamar, fils d'Aaron.
Iyi ndiye ntchito ya fuko la Ageresoni ku tenti ya msonkhano. Ntchito zawo zichitike motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.
29 Faites le recensement des fils de Mérari, par branches, par maisons paternelles,
“Werenga Amerari monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo.
30 Depuis vingt-cinq ans et au-dessus jusqu'à cinquante, de tous ceux qui entrent dans le tabernacle du témoignage, pour le service de ses œuvres.
Werenga amuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu zakubadwa amene akatumikire mu tenti ya msonkhano.
31 Et voici leur fonction et leur part de travail dans le tabernacle du témoignage: ils porteront les chapiteaux du tabernacle, ses leviers, ses colonnes et leurs bases, le voile intérieur, avec ses colonnes et leurs bases, ainsi que le voile de la porte du tabernacle,
Ntchito yawo pamene azikatumikira mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kunyamula matabwa a chihema, mitanda, mizati ndi matsinde,
32 Et aussi les colonnes du parvis qui l'entoure, avec leurs bases, les colonnes du voile de la porte du parvis et leurs bases, leurs piquets et cordages, leurs divers accessoires, et tout ce qui leur appartient. Vous noterez, en prenant les noms de chacun, toutes les choses qu'ils enlèveront.
ndiponso mizati yozungulira bwalo ndi matsinde ake, zikhomo za chihema, zingwe ndi zipangizo zake zonse ndiponso zonse zokhudzana ndi ntchito yake. Uwuze munthu aliyense chomwe ayenera kuchita.
33 Tel est le ministère de la famille des fils de Mérari, en toutes leurs œuvres dans le tabernacle du témoignage; ils l'exerceront sous la direction d'Ithamar, fils d'Aaron.
Iyi ndiyo ntchito ya mafuko a Amerari pamene akugwira ntchito ku tenti ya msonkhano motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.”
34 Et Moïse, avec Aaron et les chefs d'Israël, recensa par branches, par maisons paternelles,
Mose, Aaroni ndi atsogoleri a magulu a anthu anawerenga Akohati monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
35 De vingt-cinq ans et au-dessus jusqu'à cinquante, tous les fils de Gaath, qui entraient dans le tabernacle du témoignage, pour les œuvres du service divin.
Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano,
36 Et leur recensement par branches donna deux mille sept cent cinquante âmes.
atawawerenga mwa mafuko awo, anali 2,750.
37 Tel fut, selon l'ordre donné par le Seigneur à Moïse, le recensement fait par Moïse et Aaron, des fils de Caath, qui servaient dans le tabernacle du témoignage.
Ichi chinali chiwerengero cha mafuko a Akohati onse omwe ankatumikira mu tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.
38 Et ils recensèrent par branches, par maisons paternelles,
Ageresoni anawerengedwanso monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
39 De vingt-cinq ans et au-dessus jusqu'à cinquante, tous les fils de Gerson, qui entraient, pour le service divin et pour faire leurs œuvres, dans le tabernacle du témoignage.
Amuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano,
40 Et leur recensement par branches, par maisons paternelles, donna deux mille six cents âmes.
atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 2,630.
41 Tel fut le recensement fait par Moïse et Aaron, selon l'ordre donné par le Seigneur à Moïse, de tous les fils de Gerson, qui servaient dans le tabernacle du témoignage.
Ichi chinali chiwerengero cha Ageresoni mwa mabanja awo amene ankatumikira ku tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.
42 Ils recensèrent également par branches, par maisons paternelles,
Amerari anawawerenga monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
43 De vingt-cinq ans et au-dessus jusqu'à cinquante, tous les fils de Mérari, qui entraient dans le tabernacle du témoignage pour les œuvres du service divin.
Amuna onse kuyambira zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzatumikira ntchito mu tenti ya msonkhano,
44 Et le recensement par branches, par maisons paternelles, donna trois mille deux cents âmes.
atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 3,200.
45 Tel fut le recensement des fils de Mérari, fait par Moïse et Aaron, selon l'ordre donné par le Seigneur a Moïse.
Ichi ndicho chinali chiwerengero cha mabanja a Amerari. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga momwe Yehova anawalamulira kudzera mwa Mose.
46 Tous les recensés que dénombrèrent Moïse, Aaron et les chefs lévites d'Israël, par branches et par maisons paternelles,
Kotero Mose, Aaroni ndi atsogoleri a Israeli anawerenga Alevi onse monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
47 De vingt-cinq ans et au-dessus jusqu'à cinquante, tous ceux qui entraient dans le tabernacle du témoignage, pour l'œuvre des œuvres, et pour transporter ce qu'il y avait à enlever,
Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu omwe anabwera kudzagwira ntchito yonyamula zinthu ku tenti ya msonkhano
48 Tous ces recensés furent au nombre de huit mille cinq cent quatre-vingts.
analipo 8,580.
49 On les recensa selon l'ordre donné par le Seigneur à Moïse, homme par homme, en désignant à chacun sa part de labeur, et ce qu'il aurait à emporter; le recensement s'opéra comme le Seigneur l'avait prescrit à Moïse.
Aliyense anamupatsa ntchito ndi kumuwuza choti anyamule monga mwa lamulo la Yehova kudzera mwa Mose. Anawawerenga chomwechi potsata zimene Yehova analamula Mose.

< Nombres 4 >