< Nombres 33 >

1 Voici les stations des fils d'Israël, après que Moïse et Aaron les eurent fait sortir d'Egypte.
Malo otsatirawa ndi omwe Aisraeli anayima pa maulendo awo atatuluka mʼdziko la Igupto mʼmagulu awo motsogozedwa ndi Mose ndi Aaroni.
2 Par les ordres du Seigneur, Moïse écrivit leurs départs et leurs campements. Or, voici ces stations:
Mose analemba malo amene anayambira maulendo awo molamulidwa ndi Yehova. Maulendo awo ndi malo omwe anayambira ndi awa:
3 Ils partirent de Rhamessès le premier mois, le quinzième jour de la lune; le lendemain de la pâque, les fils d'Israël partirent sous une haute et puissante main, devant tous les fils de l'Egypte.
Aisraeli ananyamuka kuchokera ku Ramesesi pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, itangotha Paska. Iwo anatuluka nayenda molimba mtima Aigupto onse akuona,
4 Les Egyptiens ensevelirent chez eux tous les morts qu'avait frappés le Seigneur, tous les premiers-nés de la terre d'Egypte, et le Seigneur tira vengeance de leurs dieux.
pamene ankayika maliro a ana awo oyamba kubadwa, omwe Yehova anawakantha pakati pawo chifukwa Yehova anaweruza milungu yawo.
5 Partis de Rhamessès, les fils d'Israël campèrent en Soccoth.
Aisraeli atachoka ku Ramesesi, anamanga misasa yawo ku Sukoti.
6 Partis de Soccoth, ils campèrent à Etham (Othom), qui est à l'extrémité du désert.
Atachoka ku Sukoti anakamanga misasa yawo ku Etamu, mʼmbali mwa chipululu.
7 Ils partirent d'Etham, et campèrent vers le golfe de Phihahiroth, qui est en face de Béelséphon, et ils étaient campés vis-à-vis Magdole.
Ndipo atachoka ku Etamu, anabwerera ku Pihahiroti, kummawa kwa Baala-Zefoni, ndipo anamanga misasa yawo pafupi ndi Migidoli.
8 Partis de Phihahiroth, ils passèrent au milieu de la mer Rouge pour gagner le désert, et ils firent trois journées de marche dans le désert, et ils campèrent à Mara.
Atachoka ku Pihahiroti anadutsa mʼkati mwa nyanja kupita ku chipululu ndipo atayenda masiku atatu mʼchipululu cha Etamu, anamanga misasa yawo ku Mara.
9 Ils quittèrent Mara, et vinrent en Elim. Or, il y avait à Elim douze fontaines et soixante-dix tiges de palmiers; ils campèrent en ce lieu, à cause de l'eau.
Atachoka ku Mara anafika ku Elimu, kumene kunali akasupe a madzi khumi ndi awiri ndi mitengo ya migwalangwa 70 ndipo anamanga misasa yawo kumeneko.
10 Puis, ils partirent d'Elim, et ils campèrent au bord de la mer Rouge.
Atachoka ku Elimu anakamanga misasa yawo mʼmbali mwa Nyanja Yofiira.
11 Et ils partirent de la mer Rouge, et ils campèrent dans le désert de Sin.
Atachoka ku Nyanja Yofiira anakamanga misasa yawo mʼchipululu cha Sini.
12 Partis du désert de Sin, ils vinrent camper en Daphca.
Atachoka ku chipululu cha Sini anakamanga ku Dofika.
13 Et ils partirent de Daphca, et ils campèrent en Alus.
Atachoka ku Dofika anakamanga misasa yawo ku Alusi.
14 Et ils partirent d'Alus, et ils campèrent à Rhaphidin; or, il n'y avait point là de l'eau pour que le peuple put boire.
Atachoka ku Alusi anakamanga misasa yawo ku Refidimu, kumene kunalibe madzi woti anthu ndi kumwa.
15 Ayant quitte Rhaphidin, ils dressèrent leurs tentes dans le désert de Sina.
Atachoka ku Refidimu anakamanga ku chipululu cha Sinai
16 Du désert de Sina, ils vinrent camper aux Sépulcres de concupiscence.
Atachoka ku chipululu cha Sinai anakamanga misasa yawo ku Kiburoti-Hataava.
17 Ils s'éloignèrent des Sépulcres de concupiscence, et campèrent à Haseroth.
Atachoka ku Kiburoti-Hataava anakamanga misasa yawo ku Heziroti.
18 Partis d'Haseroth, ils allèrent camper à Rethma.
Atachoka ku Heziroti anakamanga ku Ritima.
19 De Rethma, ils vinrent camper en Rhemmompharès.
Atachoka ku Ritima anakamanga ku Rimoni-Perezi.
20 Ils partirent de Rhemmompharès, et ils campèrent en Lebna.
Atachoka ku Rimoni-Perezi anakamanga ku Libina.
21 Partis de Lebna, ils campèrent en Ressa.
Atachoka ku Libina anakamanga ku Risa.
22 De Ressa, ils vinrent dresser leurs tentes en Céélatha.
Atachoka ku Risa anakamanga ku Kehelata.
23 Et ils partirent de Céélatha, pour aller camper à Sépher.
Atachoka ku Kehelata anakamanga ku phiri la Seferi.
24 Ayant quitté Sépher, ils campèrent en Arada.
Atachoka ku phiri la Seferi anakamanga ku Harada.
25 Ils partirent d'Arada, et campèrent en Maceloth.
Atachoka ku Harada anakamanga ku Mekheloti.
26 De Maceloth, ils dressèrent leurs tentes en Thabath.
Atachoka ku Mekheloti anakamanga ku Tahati.
27 Et ils partirent de Thabath, pour venir camper à Tharé.
Atachoka ku Tahati anakamanga ku Tera.
28 Partis de Tharé, ils campèrent à Methca.
Atachoka ku Tera anakamanga ku Mitika.
29 De Methca, ils vinrent camper à Hesmona.
Atachoka ku Mitika anakamanga ku Hasimona.
30 Et ils partirent de Hesmona, pour aller camper à Moserotb.
Atachoka ku Hasimona anakamanga ku Moseroti.
31 Ayant quitté Moseroth, ils campèrent à Béné-Jaacan.
Atachoka ku Moseroti anakamanga ku Beni Yaakani.
32 Partis de Béné-Jaacan, ils vinrent camper en la montagne de Gadgad.
Atachoka ku Beni Yaakani anakamanga ku Hori-Hagidigadi.
33 De la montagne de Gadgad, ils vinrent camper à Jétébatba.
Atachoka ku Hori-Hagidigadi anakamanga ku Yotibata.
34 Et ils partirent de Jétébatba, pour aller dresser leurs tentes en Hébrona.
Atachoka ku Yotibata anakamanga ku Abirona.
35 Puis, ayant quitté Hebrona, ils campèrent en Asion-Gaber.
Atachoka ku Abirona anakamanga ku Ezioni-Geberi.
36 Partis d'Asion-Gaber, ils vinrent camper dans le désert de Sin, d'où, étant sortis, ils campèrent dans le désert de Pharan qui est Cadès.
Atachoka ku Ezioni-Geberi anakamanga ku Kadesi, mʼchipululu cha Zini chimene ndi Kadesi.
37 Partis de Cadès-Barné, ils vinrent camper sur la montagne de Hor, près de la terre d'Edom.
Anachoka ku Kadesi ndi kukamanga ku phiri la Hori, mʼmalire mwa dziko la Edomu.
38 Et Aaron monta sur la montagne par ordre du Seigneur, et il y mourut, en la quarantième année de la sortie d'Egypte, le cinquième mois, le premier de la lune.
Molamulidwa ndi Yehova, wansembe Aaroni anakwera ku phiri la Hori kumene anakamwalirira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu, mʼchaka cha makumi anayi, Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.
39 Aaron avait cent vingt-trois ans lorsqu'il mourut sur la montagne de Hor.
Aaroni anamwalira pa phiri la Hori ali ndi zaka 123.
40 Et, le Chananéen, roi d'Arad, qui demeurait en la terre de Chanaan, apprit que les fils d'Israël étaient en marche.
Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi yomwe inkakhala ku Negevi kummwera kwa Kanaani, inamva kuti Aisraeli akubwera.
41 Ils partirent ensuite de la montagne de Hor, et vinrent camper en Salmona.
Atachoka ku phiri la Hori anakamanga ku Zalimoni.
42 Ayant quitté Salmona, ils campèrent en Phunon.
Atachoka ku Zalimoni anakamanga ku Punoni.
43 Partis de Phunon, ils dressèrent leurs tentes à Oboth.
Atachoka ku Punoni anakamanga ku Oboti.
44 Puis, ils s'éloignèrent d'Obotb, pour venir camper à Gié-Abarim, au delà et près des frontières de Moab.
Atachoka ku Oboti anakamanga ku Iye-Abarimu.
45 Et ils partirent de Gié-Abarim, pour séjourner à Dibon-Gad.
Atachoka ku Iye-Abarimu anakamanga ku Diboni Gadi.
46 De Dibon-Gad, ils vinrent camper à Helmon-Déblathaïm.
Atachoka ku Diboni Gadi anakamanga ku Alimoni-Dibulataimu.
47 Partis de Helmon-Déblathaïm, ils campèrent sur les montagnes d'Abarim, en face de Nébo.
Atachoka ku Alimoni-Dibulataimu anakamanga mʼmapiri a Abarimu, pafupi ndi Nebo.
48 Ayant quitté les montagnes d'Abarim, ils campèrent à l'Occident de Moab, sur le Jourdain, en face de Jéricho.
Atachoka ku mapiri a Abarimu anakamanga ku zigwa za Mowabu mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi Yeriko.
49 Ensuite, ils campèrent aux bords du Jourdain de Beth-Simoth, à Abelsatim, à l'occident de Moab.
Ali ku zigwa za Mowabu anamanga mʼmbali mwa Yorodani kuchokera ku Beti-Yesimoti mpaka ku Abeli-Sitimu.
50 Et le Seigneur parla à Moïse, à l'occident de Moab, sur le Jourdain, en face de Jéricho, et il lui dit:
Pa zigwa za Mowabu, mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi ku Yeriko, Yehova anawuza Mose kuti,
51 Parle aux fils d'Israël, et dis-leur: Vous allez traverser le Jourdain pour entrer en la terre de Chanaan.
“Nena kwa Aisraeli kuti, ‘Pamene muwoloka Yorodani kulowa mʼdziko la Kanaani,
52 Et, devant vous, vous exterminerez tous ceux qui habitent cette terre; vous détruirez leurs tours, leurs idoles jetées en fonte, et leurs colonnes.
mukathamangitse nzika zonse za mʼdzikomo pamaso panu. Mukawononge mafano awo onse a miyala ndi osula ndi malo awo achipembedzo.
53 Vous détruirez tous les peuples de la terre promise, et vous l'habiterez; car je vous la donne pour héritage.
Mukalande dzikolo ndi kukhalamo chifukwa ndakupatsani dziko limenelo kuti mukhalemo.
54 Vous la partagerez entre vos tribus; donnant plus aux plus nombreux, et moins aux moindres en nombre. Quelle que soit la part qu'à chacun désignera le sort, chacun la possèdera; le partage se fera par tribus paternelles.
Mukagawane dzikolo pochita maere monga mwa mafuko anu. Kwa omwe ali ambiri, cholowa chambiri, ndipo amene ali ocheperapo, chocheperanso. Chilichonse chimene chidzawagwere iwo mwa maere chidzakhala chawo. Mukaligawane monga mwa mafuko a makolo anu.
55 Mais, si vous n'exterminez pas devant vous tous les habitants de la terre, ceux que vous aurez épargnés seront des traits en vos yeux, des flèches en vos flancs; ils seront vos ennemis sur la terre que vous habiterez.
“‘Koma ngati simukathamangitsa nzika zimene zili mʼdzikomo, amene mukawalole kukhalamo adzakhala ngati zisonga mʼmaso mwanu ndi ngati minga mʼmbali mwanu. Adzakubweretserani mavuto mʼdziko limene mudzakhalemolo.
56 Et alors, je vous traiterai vous-mêmes comme j'avais résolu de les traiter.
Ndipo pamenepo ndidzachitira inu zomwe ndinaganiza kuwachitira iwowo.’”

< Nombres 33 >