< Nombres 29 >

1 Le septième mois, le premier jour de la lune sera solennel et saint pour vous; vous ne ferez aucune œuvre servile; c'est pour vous le jour des signaux que donnent les trompettes.
“‘Pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Ili ndi tsiku limene muziliza malipenga.
2 Et vous offrirez en holocauste, comme sacrifice d'odeur de suavité pour le Seigneur, un veau pris parmi les bœufs, un bélier et sept agneaux d'un an, sans tache.
Muzipereka mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi wopanda chilema monga nsembe zopsereza, fungo lokoma kwa Yehova.
3 Leur oblation sera de fleur de farine pétrie dans l'huile, trois décimes par veau, deux décimes par bélier,
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzipereka chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa yayimuna iliyonse muzipereka makilogalamu awiri.
4 Un décime de décime par agneau, pour les sept agneaux.
Pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja muzipereka kilogalamu imodzi.
5 Et vous offrirez pour le péché un bouc pris parmi les chèvres qui expiera les péchés de vous tous;
Muziperekanso mbuzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
6 Outre les holocaustes, à cause de la nouvelle lune, et leurs oblations et leurs libations, et outre l'holocauste perpétuel: les oblations et les libations seront faites selon la règle; ce sera le sacrifice d'odeur de suavité pour le Seigneur.
Izi ndi zowonjezera pa nsembe zopsereza za mwezi ndi mwezi komanso za tsiku ndi tsiku pamodzi ndi zopereka za chakudya ndi zopereka za chakumwa potsata malamulo ake. Izi ndi zopereka zotentha pa moto, zoperekedwa kwa Yehova, fungo lokoma.
7 Le dixième jour de la même lune sera solennel et saint pour vous, et vous ne ferez aucune œuvre servile.
“‘Pa tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiriwu, muzichita msonkhano wopatulika. Muzisala zakudya ndipo musamagwire ntchito.
8 Vous offrirez en holocauste, comme sacrifice d'odeur de suavité pour le Seigneur, un veau pris parmi les bœufs, un bélier et sept agneaux d'un an, tous à vos yeux sans tache.
Muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza, yotulutsa fungo lokoma lokondweretsa Yehovayo; ngʼombe yayimuna imodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi. Zimenezi zizikhala zopanda chilema.
9 Et leur oblation sera de fleur de farine pétrie dans l'huile, trois décimes par veau, deux décimes par bélier.
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri;
10 Un décime de décime par agneau, pour les sept agneaux.
kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiriwo.
11 Et vous offrirez pour le péché un bouc pris parmi les chèvres qui expiera le péché de vous tous, outre celui de la purification, et outre l'holocauste perpétuel; les oblations et les libations se feront selon la règle; ce sera le sacrifice d'odeur de suavité pour le Seigneur.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe yopepesera machimo ya pa tsiku la mwambo ija, kuwonjezanso pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija, pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi cha chakumwa.
12 Le quinzième jour de ce septième mois sera solennel et saint pour vous; vous ne ferez aucune œuvre servile, et vous ferez pendant sept jours la fête du Seigneur.
“‘Pa tsiku la mwezi wachisanu ndi chiwiri, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Muzichita madyerero a Yehova masiku asanu ndi awiri.
13 Vous offrirez en holocauste, comme sacrifice d'odeur de suavité pour le Seigneur: le premier jour, treize veaux pris parmi les bœufs, deux béliers, quatorze agneaux d'un an, tous sans tache.
Muzipereka nsembe yotentha pa moto, kuti izikhala fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu, nkhosa zazimuna ziwiri, ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
14 Leurs oblations seront de fleur de farine pétrie dans l'huile, trois décimes par veau pour les treize veaux, deux décimes par bélier pour les deux béliers,
Pa mwana wangʼombe aliyense mwa ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu aja, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa iliyonse mwa nkhosa ziwiri zija, mukonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri.
15 Un décime de décime par agneau, pour les quatorze agneaux.
Pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa aamuna khumi ndi anayiwo, muzipereka chakudya cha kilogalamu imodzi.
16 Et vous offrirez pour le péché un bouc pris parmi les chèvres, outre les offrandes de l'holocauste perpétuel, leurs oblations et leurs libations;
Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhale nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
17 Et le second jour: douze veaux, deux béliers, quatorze agneaux d'un an, tous sans tache.
“‘Pa tsiku lachiwiri muzipereka ana angʼombe aamuna khumi ndi awiri aja, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi aja, zonse zopanda chilema.
18 Les oblations et les libations seront quant aux veaux, aux béliers et aux agneaux, selon leur nombre et selon la règle.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
19 Et vous offrirez pour le péché un bouc pris parmi les chèvres; outre les offrandes de l'holocauste perpétuel, leurs oblations et leurs libations;
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
20 Le troisième jour: onze veaux, deux béliers, quatorze agneaux sans tache.
“‘Pa tsiku lachitatu muzipereka ngʼombe zazimuna khumi ndi imodzi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
21 Les oblations et les libations pour les veaux, les béliers et les agneaux se feront selon le nombre des victimes, et selon la règle.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
22 Vous offrirez, pour le péché, un bouc pris parmi les chèvres, outre les offrandes de l'holocauste perpétuel, leurs oblations et leurs libations;
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
23 Et le quatrième jour: dix veaux, deux béliers, quatorze agneaux d'un an sans tache.
“‘Pa tsiku lachinayi muzipereka ngʼombe zazimuna khumi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
24 Les oblations, les libations, pour les veaux, les béliers et les agneaux, se feront selon le nombre des victimes et selon la règle,
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
25 Vous offrirez aussi pour le péché un bouc pris parmi les chèvres, outre les offrandes de l'holocauste perpétuel, leurs oblations et leurs libations;
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
26 Et le cinquième jour: neuf veaux, deux béliers, quatorze agneaux d'un an sans tache.
“‘Pa tsiku lachisanu muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zinayi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
27 Les oblations et les libations, pour les veaux, les béliers et les agneaux se feront selon le nombre des victimes et selon la règle.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
28 De plus vous offrirez pour le péché un bouc pris parmi les chèvres, outre les offrandes de l'holocauste perpétuel, leurs oblations et leurs libations;
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
29 Et le sixième jour: huit veaux, deux béliers, quatorze agneaux d'un an sans tache.
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zitatu, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
30 Les oblations et les libations, pour les veaux, les béliers et les agneaux, se feront selon le nombre des victimes et selon la règle.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
31 Et vous offrirez pour le péché un bouc pris parmi les chèvres, outre les offrandes de l'holocauste perpétuel, leurs oblations et leurs libations;
Muziperekenso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
32 Le septième jour: sept veaux, deux béliers, quatorze agneaux d'un an sans tache.
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa amuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
33 Les oblations et les libations, pour les veaux, les béliers et les agneaux, se feront selon le nombre des victimes et selon la règle.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
34 Vous offrirez ensuite pour le péché un bouc pris parmi les chèvres, outre les offrandes de l'holocauste perpétuel, leurs oblations et leurs libations.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
35 Le huitième jour sera pour vous la fin de la fête; vous ne ferez ce jour-là aucune œuvre servile.
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzichita msonkhano ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
36 Et vous offrirez en holocauste, comme sacrifice d'odeur de suavité pour le Seigneur, un veau, un bélier, sept agneaux d'un an sans tache.
Muzipereka chopereka chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ngʼombe imodzi yayimuna, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa amuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
37 Les oblations et les libations seront selon le nombre des victimes et selon la règle,
Pamodzi ndi ngʼombe yayimunayo, nkhosa yayimunayo ndi ana ankhosawo, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
38 Et vous offrirez pour le péché un bouc pris parmi les chèvres, outre les offrandes de l'holocauste perpétuel, leurs oblations et leurs libations.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
39 Tels sont les sacrifices que vous ferez au Seigneur en vos fêtes; il y aura en outre vos vœux, vos dons volontaires, vos holocaustes, vos oblations et libations, et vos hosties pacifiques.
“‘Kuwonjezera pa zopereka zimene munalumbirira ndi pa zopereka zanu zaufulu, muzipereka zimenezi kwa Yehova pa masiku osankhika a chikondwerero chanu. Nsembe zanu zachakumwa ndi nsembe zanu zachiyanjano.’”
40 Moïse rapporta aux fils d'Israël tout ce que lui avait prescrit le Seigneur,
Mose anawuza Aisraeli zonse zimene Yehova anamulamulira.

< Nombres 29 >