< Néhémie 13 >

1 En ce jour-là, on lut à haute voix au peuple le livre de Moïse, et on y trouva écrit: Que les Ammonites et les Moabites ne devaient jamais entrer dans l'Église de Dieu.
Pa tsiku limenelo anawerenga buku la Mose anthu akumva. Ndipo anapeza mawu akuti, Mwamoni kapena Mmowabu asalowe konse mu msonkhano wa Mulungu.
2 Parce qu'ils n'étaient point venus au-devant d'Israël avec du pain et de l'eau, et qu'ils avaient salarié Balaam pour le maudire; mais, notre Dieu changea la malédiction en bénédiction.
Paja iwowa sanawachingamire Aisraeli kukawapatsa chakudya ndi madzi. Mʼmalo mwake analemba ganyu Baalamu kuti adzawatemberere. Komabe Mulungu wathu anasandutsa tembererolo kukhala mdalitso.
3 Et lorsqu'ils eurent ouï la loi, tous ceux qui s'étaient mêlés à Israël en furent séparés.
Anthu atamva lamuloli, anachotsa pakati pawo onse amene anali achilendo.
4 Or, avant cela, Eliasib, le prêtre, très-proche allié de Tobias, demeurait dans le trésor du temple de notre Dieu.
Izi zisanachitike, wansembe Eliyasibu anali atasankhidwa kukhala woyangʼanira zipinda zosungiramo katundu za Nyumba ya Mulungu. Iyeyu ankagwirizana kwambiri ndi Tobiya.
5 Et il s'était fait faire un vaste magasin dans le lieu où l'on déposait jadis les offrandes, l'encens, les vases, la dîme du blé, du vin et de l'huile, ce qui était dû aux lévites, aux chantres et aux portiers, et les prémices destinées aux prêtres.
Choncho anamupatsa chipinda chachikulu chimene kale ankasungamo zopereka zakudya, lubani, ziwiya, zopereka za chakhumi za tirigu, vinyo ndi mafuta zoyenera kuperekedwa kwa Alevi, oyimba nyimbo ndi alonda a ku Nyumba ya Mulungu, komanso mphatso zoyenera kupereka kwa ansembe.
6 Et, en ce temps-là, je n'étais pas à Jérusalem. Car, dans la trente- deuxième année du règne d'Arthasastha, roi de Babylone, j'étais allé auprès du roi. Et, un certain nombre de jours étant accompli, je demandai au roi la permission de partir.
Koma pamene izi zonse zinkachitika mu Yerusalemu, ine kunalibe popeza mʼchaka cha 32 cha Aritasasita mfumu ya Babuloni ine ndinabwerera kwa mfumu. Patapitanso nthawi ndinapempha chilolezo kwa mfumuyo
7 Et je revins à Jérusalem, et je reconnus le mal qu'avait fait Eliasib avec Tobias en lui faisant un magasin dans le parvis du temple de Dieu.
ndipo ndinabwerera ku Yerusalemu. Kumeneko ndinamva za chinthu choyipa chimene Eliyasibu anachita pomupatsa Tobiya chipinda mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu.
8 Et cela me parut très-mal; et je jetai hors du magasin tous les meubles de la maison de Tobias.
Ndinapsa mtima kwambiri ndipo ndinataya kunja katundu yense wa Tobiya amene anali mʼchipindamo.
9 Et je parlai, et on purifia le magasin, et j'y fis replacer les vases du temple, les offrandes et l'encens.
Ndinalamulira kuti ayeretse zipinda, ndipo kenaka ndinabwezeramo zida za mʼNyumba ya Mulungu, pamodzi ndi chopereka cha zakudya ndi lubani.
10 Et je reconnus qu'on n'avait plus donné la part des lévites, de sorte que les lévites et les chantres faisant œuvre au temple s'étaient enfuis chacun en sa terre.
Ndinapezanso kuti Alevi sankalandira magawo awo amene amayera kulandira. Chotsatira chake Alevi onse pamodzi ndi oyimba nyimbo amene ankagwira ku Nyumba ya Mulungu anathawa, aliyense kupita ku munda wake.
11 Et je fis des reproches aux officiers, et je leur dis: D'où vient que le temple du Seigneur est abandonné? Puis, je rassemblai les lévites et les Chantres, et je les rétablis dans leurs fonctions.
Choncho ndinadzudzula akuluakulu aja ndipo ndinawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani Nyumba ya Mulungu yasiyidwa?” Ndipo ine ndinawayitanitsa pamodzi ndi kuwayika mʼmalo awo.
12 Alors, tout Juda apporta dans les trésors la dîme du froment; de l'huile et du vin,
Pambuyo pake Ayuda anayambanso kubwera ndi zopereka zawo za chakhumi cha tirigu, vinyo ndi mafuta kuti ziperekedwe ku nyumba yosungiramo chuma.
13 Entre les mains de Sélémias le prêtre, de Sadoc le scribe, et de Phadaïa, l'un des lévites. Et ils avaient auprès d'eux Anan, fils de Zacchur, fils de Matthanias; car ils étaient réputés fidèles, et ils furent chargés de faire les distributions à leurs frères.
Ndipo ndinasankha wansembe Selemiya, mlembi Zadoki, ndi Mlevi wotchedwa Pedaya kukhala oyangʼanira zipinda zosungiramo. Ndinasankhanso Hanani mwana wa Zakuri mwana wa Mataniya kukhala wowathandizira chifukwa ndinaona kuti anthu awa anali odalirika. Ntchito yawo inali yogawira abale awo zinthu zofunika.
14 Souvenez-vous de moi, ô mon Dieu, à cause de cela; que mes bonnes œuvres dans le temple du Seigneur Dieu ne soient point effacées.
Inu Mulungu wanga, mundikumbukire pa zimenezi, ndipo musafafanize ntchito zanga zimene ndachita mokhulupirika pa Nyumba yanu pofuna kukutumikirani.
15 En ces jours-là, je vis que dans Juda quelques-uns pressuraient le vin le jour du sabbat; je vis que d'autres transportaient des gerbes, que d'autres encore chargeaient leurs ânes de vin, de grappes, de figues, de toutes sortes de fardeaux, et qu'ils les conduisaient à Jérusalem le jour du sabbat. Et je les avertis des jours où ils pouvaient trafiquer.
Nthawi imeneyo ndinaona anthu a mu Yuda akuponda ndi kufinya mphesa pa tsiku la Sabata. Ena ankawunjika tirigu milumilu ndi kumasenzetsa abulu. Enanso ankabwera ndi vinyo, mphesa, mkuyu ndi katundu wa mitundumitundu ku Yerusalemu pa tsiku la Sabata. Choncho ndinawachenjeza za kugulitsa zakudya pa tsiku la Sabata.
16 Et des gens s'étaient établis à Jérusalem, apportant du poisson, vendant toutes sortes de marchandises aux Juifs, le jour du sabbat.
Nawonso anthu a ku Turo amene ankakhala mu Yerusalemu ankabweretsa nsomba ndi akatundu ena onse amalonda kudzagulitsa pa Sabata kwa anthu a mʼdziko la Yuda ndi a mu Yerusalemu.
17 Et je réprimandai les fils de Juda de condition libre, et je leur dis: Quelle est cette mauvaise action que vous faites, en profanant le jour du sabbat?
Ndipo ndinadzudzula anthu olemekezeka a dziko la Yuda. Ndinawafunsa kuti, “Nʼchoyipa chanji mukuchitachi, kumayipitsa tsiku la Sabata chotere?
18 N'est-ce point là ce que faisaient vos pères? n'est-ce point la cause de tous les malheurs dont notre Dieu les à frappés, eux et notre ville? Et vous, n'attirerez-vous pas un surcroît de colère sur Israël en profanant le sabbat?
Makolo anu anachita zomwezi ndipo Mulungu wathu anadzetsa mavuto pa ife ndi pa mzinda uwu. Kodi inu mukufuna kuwutsanso mkwiyo wa Mulungu pa Israeli pamene mukudetsa tsiku la Sabata?”
19 Or, quand les portes de Jérusalem furent rétablie, la veille d'un sabbat, je parlai, et on ferma les portes; je parlai, et on ne les ouvrit qu'après le sabbat, et je mis de mes serviteurs à chaque porte pour qu'on ne pût introduire des fardeaux le jour du sabbat.
Nʼchifukwa chake ndikulamula kuti pamene kuyamba kuda, tsiku la Sabata lisanayambe, azitseka zipata zonse za Yerusalemu ndipo asazitsekule mpaka sabata litatha. Ndinayika ena mwa antchito anga oyangʼanira pa zipata kuti katundu aliyense asalowe mu Yerusalemu pa tsiku la Sabata.
20 Et tous les marchands passèrent la nuit en plein air, et ils vendirent une ou deux fois hors de Jérusalem.
Choncho kamodzi kapena kawiri anthu amalonda ndi anthu ogulitsa katundu osiyanasiyana ankagona usiku wonse kunja kwa Yerusalemu.
21 Et je les avertis, et je leur dis: Pourquoi passez-vous la nuit devant les remparts? Si vous recommencez, j'étendrai la main sur vous. Depuis lors, ils ne vinrent plus le jour du sabbat.
Koma ndinawachenjeza ndi kuwafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukugona pafupi ndi khoma? Ngati muchitanso zimenezi, ine ndidzakugwirani.” Kuyambira nthawi imeneyo, sanabwerenso pa tsiku la Sabata.
22 Et je dis aux lévites qui s'étaient purifiés, et qui étaient venus garder les portes, de sanctifier le jour du sabbat: à cause de cela, souvenez-vous de moi, mon Dieu, et épargnez-moi, selon la plénitude de votre miséricorde.
Ndipo ndinalamulira Alevi kuti adziyeretse okha ndi kubwera kudzalonda pa zipata ndi cholinga choti tsiku la Sabata likhale tsiku loyera. Inu Mulungu wanga, kumbukireninso ine pa zimenezi ndipo mundisunge malingana ndi chikondi chanu chachikulu chosasinthika.
23 Or, en ces jours-là, je vis que des Juifs avaient épousé des femmes d'Azot, et des Ammonites et des Moabites.
Masiku amenewo ndinaonanso anthu a ku Yuda amene anakwatira akazi ochokera ku Asidodi, Amoni ndi Mowabu.
24 Et leurs fils parlaient à demi la langue d'Azot, et ils ne savaient point parler juif.
Theka la ana awo linkayankhula chiyankhulo cha Asidodi kapena chiyankhulo chimodzi cha anthu ena, ndipo sankathanso kuyankhula chiyankhulo cha Ayuda.
25 Et je les réprimandai, et je les maudis, et j'en frappai quelques-uns, et je leur rasai la tête, et je leur fis jurer devant Dieu de ne point donner leurs filles aux fils des étrangers, et de ne point faire épouser par leurs fils des filles étrangères, disant:
Tsono ndinakangana nawo ndi kuwatemberera. Ndinamenya ena mwa anthuwo ndi kuzula tsitsi lawo. Ine ndinawalumbiritsa mʼdzina la Mulungu kuti, “Inu musapereke ana anu aakazi kuti akwatiwe ndi ana awo aamuna kapena inuyo ngakhale ana anu aamuna kukwatira ana awo aakazi.
26 N'est-ce pas là le péché de Salomon, roi d'Israël? Il n'y avait point son pareil parmi les rois des nations: il aimait Dieu, Dieu lui avait donné le royaume entier d'Israël, et les femmes étrangères le pervertirent.
Kodi Solomoni mfumu ya Israeli suja anachimwa chifukwa cha ukwati ngati umenewu. Pakati pa mitundu yambiri panalibe mfumu ngati iyi. Iye anakondedwa ndi Mulungu wake, ndipo Mulungu anamuyika kukhala mfumu ya Israeli yense, koma iyeyo anachimwa chifukwa cha akazi achilendo.
27 Que nous n'apprenions plus que vous faites ce péché; que vous violez l'alliance avec notre Dieu; que vous épousez des femmes étrangères.
Kodi tsopano ife tizimva inu kuti mukuchita choyipa chachikulu chimenechi, kupandukira Yehova Mulungu wathu pomakwatira akazi achilendo?”
28 Or, l'un des fils de Joad, le grand prêtre Elisab, était gendre de Sanaballat l'Horonite; je le chassai loin de moi.
Mmodzi mwa ana aamuna a Yehoyada mwana Eliyasibu mkulu wa ansembe nʼkuti nthawi imeneyi ali mpongozi wa Sanibalati wa ku Horoni. Choncho ndinamuthamangitsa pamaso panga.
29 Souvenez-vous d'eux, ô Seigneur, à cause de la violation du sacerdoce, et de votre alliance, touchant les prêtres et les lévites.
Inu Mulungu wanga, mukumbukire mmene iwo anayipitsira unsembe, pangano la unsembe komanso la Alevi.
30 Et je les purifiai de leur contact avec des étrangères, et je réglai les services journaliers des prêtres et des lévites,
Motero ndinayeretsa ansembe ndi Alevi powachotsera kalikonse kachilendo. Ndipo ndinakhazikitsa ntchito zawo, kuti aliyense akhale pa ntchito yake.
31 Et l'offrande du bois des holocaustes au temps prescrit, lorsque l'on taille la vigne. Souvenez-vous de moi, ô mon Dieu, dans votre mansuétude.
Ndiponso kupereka nkhuni ndi zipatso zoyamba kucha pa nthawi yake. Ndikumbukireni pondikomera mtima, Inu Mulungu wanga.

< Néhémie 13 >