< Lamentations 1 >

1 Aleph. Comment cette ville, jadis pleine de peuple, est-elle assise solitaire? Elle est devenue comme une veuve celle qui avait grandi parmi les nations; la reine des provinces est assujettie au tribut.
Haa! Mzinda uja wasiyidwa wokhawokha, umene kale unali wodzaza ndi anthu! Kale unali wotchuka pakati pa mitundu ya anthu! Tsopano wasanduka ngati mkazi wamasiye. Kale unali mfumukazi ya onse pa dziko lapansi, tsopano wasanduka kapolo.
2 Beth. Elle pleure, elle a pleuré la nuit, et les larmes sont encore sur ses joues, et de tous ceux qui l'aimaient, il n'en est pas, un qui la console; ses amis l'ont méprisée, et sont devenus ses ennemis.
Ukulira mowawidwa mtima usiku wonse, misozi ili pa masaya pake. Mwa abwenzi ake onse, palibe ndi mmodzi yemwe womutonthoza. Abwenzi ake onse amuchitira chiwembu; onse akhala adani ake.
3 Ghimel. La fille de Juda s'est expatriée dans son humiliation, et dans l'excès de sa servitude; elle s'est assise parmi les nations et n'y a point trouvé de repos; et tous ses persécuteurs l'ont prise au milieu de ses angoisses.
Yuda watengedwa ku ukapolo, kukazunzika ndi kukagwira ntchito yolemetsa. Iye akukhala pakati pa anthu a mitundu ina; ndipo alibe malo opumulira. Onse omuthamangitsa iye amupitirira, ndipo alibe kwina kothawira.
4 Daleth. Les voies de Sion pleurent, parce que nul ne vient plus à ses solennités; toutes ses portes sont en ruine; ses prêtres gémissent; ses vierges ont été emmenées; elle-même est pleine d'amertume.
Misewu yopita ku Ziyoni ikulira, chifukwa palibe ndi mmodzi yemwe akubwera ku maphwando ake. Zipata zake zonse zili pululu, ansembe akubuwula. Anamwali ake akulira, ndipo ali mʼmasautso woopsa.
5 Hé. Les oppresseurs sont montés sur sa tête; ses ennemis prospèrent, parce que le Seigneur l'a humiliée, à cause de la multitude de ses péchés; ses jeunes gens sont partis en captivité, devant la face de l'oppresseur.
Adani ake asanduka mabwana ake; odana naye akupeza bwino. Yehova wamubweretsera mavuto chifukwa cha machimo ake ambiri. Ana ake atengedwa ukapolo pamaso pa mdani.
6 Vav. Toute la beauté de la fille de Sion lui a été ravie; ses princes sont devenus comme des béliers qui ne trouvent point de pâturage; ils sont partis énervés devant la face des persécuteurs.
Ulemerero wonse wa mwana wamkazi wa Ziyoni wachokeratu. Akalonga ake ali ngati mbawala zosowa msipu; alibe mphamvu zothawira owathamangitsa.
7 Zaïn. Jérusalem s'est souvenue de ses jours d'humiliation et de ses prévarications, et de tout ce que, depuis les anciens jours, elle avait accumulé de choses désirables, quand son peuple est tombé dans les mains de l'oppresseur; et nul n'était là pour la secourir, et ses ennemis l'ont raillée en la voyant captive.
Pa masiku a masautso ndi kuzunzika kwake, Yerusalemu amakumbukira chuma chonse chimene mʼmasiku amakedzana chinali chake. Anthu ake atagwidwa ndi adani ake, panalibe aliyense womuthandiza. Adani ake ankamuyangʼana ndi kumuseka chifukwa cha kuwonongeka kwake.
8 Cheth. Jérusalem a grandement péché, c'est pourquoi elle est comme une mer agitée. Tous ceux qui l'honoraient l'ont affligée; car ils ont vu sa honte, et, en gémissant, elle s'est détournée.
Yerusalemu wachimwa kwambiri ndipo potero wakhala wodetsedwa. Onse amene ankamulemekeza pano akumunyoza, chifukwa aona umaliseche wake. Iye mwini akubuwula ndipo akubisa nkhope yake.
9 Teth. Son impureté est devant ses pieds, et elle ne s'est point souvenue de sa fin; mais elle a rabattu sa fierté; il n'est personne qui la console. Voyez, Seigneur, mon abaissement; voyez comme mon ennemi s'est glorifié.
Uve wake umaonekera pa zovala zake; iye sanaganizire za tsogolo lake. Nʼchifukwa chake kugwa kwake kunali kwakukulu; ndipo analibe womutonthoza. “Inu Yehova, taonani masautso anga, pakuti mdani wapambana.”
10 Iod. L'oppresseur a étendu la main sur tout ce qu'elle a de plus précieux; elle a vu les gentils entrer dans son sanctuaire; et pourtant vous aviez défendu qu'ils entrassent jamais dans son enceinte.
Adani amulanda chuma chake chonse; iye anaona mitundu ya anthu achikunja ikulowa mʼmalo ake opatulika, amene Inu Mulungu munawaletsa kulowa mu msonkhano wanu.
11 Caph. Tout son peuple gémissant cherche du pain; ils ont donné leurs choses les plus précieuses pour avoir des aliments, afin de ranimer leurs âmes. Voyez, Seigneur, considérez comme elle est tombée dans le mépris.
Anthu ake onse akubuwula pamene akufunafuna chakudya; asinthanitsa chuma chawo ndi chakudya kuti akhale ndi moyo. “Inu Yehova, taonani ndipo ganizirani, chifukwa ine ndanyozeka.”
12 Lamed. O vous tous qui passez par la voie, retournez-vous, et voyez s'il est une douleur semblable à la douleur qui m'est venue. Le Seigneur a parlé contre moi; il m'a humilié au jour de sa colère.
“Kodi zimenezi mukuziyesa zachabe, inu nonse mukudutsa? Yangʼanani ndipo muone. Kodi pali mavuto ofanana ndi amene andigwerawa, amene Ambuye anandibweretsera pa tsiku la ukali wake?
13 Mem. De ses hautes demeures, il m'a lancé un feu, et il l'a fait entrer dans mes os. Il a déployé un filet sous mes pieds; il m'a ramenée en arrière; il m'a détruite et contristée durant tout le jour.
“Anatumiza moto kuchokera kumwamba, unalowa mpaka mʼmafupa anga. Anayala ukonde kuti ukole mapazi anga ndipo anandibweza. Anandisiya wopanda chilichonse, wolefuka tsiku lonse.
14 Noun. Il a veillé sur toutes mes impiétés; elles ont enlacé mes mains; elles sont descendues autour de mon cou; il m'a ôté ma force; le Seigneur m'a chargé les mains de douleurs que je ne pourrai supporter.
“Wazindikira machimo anga onse ndipo ndi manja ake anawaluka pamodzi. Machimowa afika pakhosi panga, ndipo Ambuye wandithetsa mphamvu. Iye wandipereka kwa anthu amene sindingalimbane nawo.
15 Samech. Le Seigneur a enlevé du milieu de moi tous mes forts; il a appelé le temps contre moi, pour broyer mes hommes d'élite; le Seigneur a foulé le pressoir de la vierge fille de Juda, et c'est pourquoi je pleure.
“Ambuye wakana anthu anga onse amphamvu omwe ankakhala nane: wasonkhanitsa gulu lankhondo kuti lilimbane nane, kuti litekedze anyamata anga; mʼmalo ofinyira mphesa Ambuye wapondereza anamwali a Yuda.
16 Aïn. Mes yeux fondent en larmes, parce que mon consolateur, celui qui ranimait mon âme, s'est éloigné de moi; mes fils ont péri; l'ennemi a prévalu.
“Chifukwa cha zimenezi ndikulira ndipo maso anga adzaza ndi misozi. Palibe aliyense pafupi woti anditonthoze, palibe aliyense wondilimbitsa mtima. Ana anga ali okhaokha chifukwa mdani watigonjetsa.
17 Phé. Sion a eu beau tendre la main, il n'est personne qui la console; le Seigneur a donné ses ordres contre Jacob; ses oppresseurs l'entourent; Jérusalem, au milieu d'eux, est comme une femme assise dans sa souillure.
“Ziyoni wakweza manja ake, koma palibe aliyense womutonthoza. Yehova walamula kuti abale ake a Yakobo akhale adani ake; Yerusalemu wasanduka chinthu chodetsedwa pakati pawo.
18 Tsadé. Le Seigneur est juste, car j'ai irrité sa bouche. Écoutez donc, ô peuples et considérez ma douleur. Mes vierges et mes jeunes gens, ont été emmenés captifs.
“Yehova ndi wolungama, koma ndine ndinawukira malamulo ake. Imvani inu anthu a mitundu yonse; onani masautso anga. Anyamata ndi anamwali anga agwidwa ukapolo.
19 Coph. J'ai appelé mes amants, et ils m'ont trompée; mes prêtres et mes anciens sont morts dans la ville; ils ont cherché des aliments pour ranimer leur âme, et ils n'en ont point trouvé.
“Ndinayitana abwenzi anga koma anandinyenga. Ansembe ndi akuluakulu anga anafa mu mzinda pamene ankafunafuna chakudya kuti akhale ndi moyo.
20 Resch. Voyez, Seigneur, comme je suis affligée; mes entrailles sont troublées, mon cœur en moi-même est confondu, parce que je suis pleine d'amertume. Dans les rues, c'est le glaive qui m'a privée de mes enfants; dans ma maison, c'est la peste.
“Inu Yehova, onani mmene ine ndavutikira! Ndikuzunzika mʼkati mwanga, ndipo mu mtima mwanga ndasautsidwa chifukwa ndakhala osamvera. Mʼmisewu anthu akuphedwa, ndipo ku mudzi kuli imfa yokhayokha.
21 Schin. Écoutez donc, je gémis, et il n'est personne qui me console; mes ennemis ont ouï parler de mes maux, et ils se sont réjouis, parce que c'est vous qui avez fait cela; mais vous avez amené le jour de la consolation; vous avez appelé le moment, et, ils sont devenus semblables à moi.
“Anthu amva kubuwula kwanga, koma palibe wonditonthoza. Adani anga onse amva masautso anga; iwo akusangalala pa zimene Inu mwachita. Lifikitseni tsiku limene munalonjeza lija kuti iwonso adzakhale ngati ine.
22 Thav. Que toute leur malice apparaisse devant votre face; grappillez en eux comme vous avez grappillé pour chacun de mes péchés; car mes sanglots redoublent, et mon cœur est contristé.
“Lolani kuti ntchito zawo zoyipa zifike pamaso panu; muwalange ngati mmene mwandilangira ine chifukwa cha machimo anga onse. Ndikubuwula kwambiri ndipo mtima wanga walefuka.”

< Lamentations 1 >