< Job 1 >

1 Il y avait en la terre de Hus, un homme appelé Job; et cet homme était intègre, irréprochable, juste, pieux, et il s'abstenait de toute mauvaise action.
Mʼdziko la Uzi munali munthu wina, dzina lake Yobu. Munthu ameneyu anali wosalakwa ndi wolungama mtima, ankaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa.
2 Et il avait sept fils et trois filles.
Anali ndi ana aamuna asanu ndi awiri ndi ana aakazi atatu,
3 Et ses troupeaux étaient sept mille moutons, trois mille chamelles, cinq cents paires de bœufs, cinq cents ânesses au pâturage, et il avait une multitude de serviteurs et de grands travaux sur la terre; et cet homme avait la noblesse des fils de l'Orient.
ndipo anali ndi nkhosa 7,000, ngamira 3,000, ngʼombe zantchito 1,000 ndi abulu aakazi 500, ndiponso anali ndi antchito ambiri. Iye anali munthu wotchuka kwambiri pakati pa anthu onse a mʼmayiko a kummawa.
4 Et ses fils, se réunissant tour à tour, faisaient chaque jour un festin, et ils accueillaient aussi leurs trois sœurs pour boire et manger avec eux.
Ana ake aamuna ankachita phwando mosinthanasinthana mʼnyumba zawo, ndipo ankayitana alongo awo atatu aja kudzadya ndi kumwa nawo.
5 Et dès que leurs jours de repas étaient écoulés, Job, s'étant levé de grand matin, les convoquait; et il les purifiait, et il immolait autant de victimes que le comportait leur nombre et de plus un bœuf pour le péché de leurs âmes. Car Job disait: Qui sait si les fils au fond du cœur, n'ont pas eu de mauvaises pensées contre Dieu? Ainsi faisait donc Job toutes les fois.
Masiku aphwandowo atatha, Yobu ankawayitana kuti adzawayeretse. Mmamawa iye ankapereka nsembe yopsereza kuperekera mwana aliyense, poganiza kuti, “Mwina ana anga achimwa ndi kutukwana Mulungu mʼmitima yawo.” Umu ndi mmene Yobu ankachitira nthawi zonse.
6 Or, l'un de ces jours-là, les anges de Dieu s'en vinrent comparaître devant le Seigneur, et le diable vint avec eux.
Ana a Mulungu atabwera kudzadzionetsa pamaso pa Yehova, nayenso Satana anafika nawo limodzi.
7 Et le Seigneur dit au diable: D'où viens-tu? Et le diable répondit: J'arrive après avoir fait le tour de la terre et parcouru tout ce qui est sous le ciel.
Yehova anati kwa Satanayo, “Kodi iwe ukuchokera kuti?” Satana anayankha Yehova kuti, “Ndakhala ndikungoyendayenda ndi kumangozungulira mʼdzikoli.”
8 Et le Seigneur reprit: As-tu remarqué Job, mon serviteur? as-tu reconnu qu'il n'a point son pareil sur la terre, que c'est un homme irréprochable, sincère, pieux, et qui s'abstient de toute mauvaise action?
Pamenepo Yehova anati kwa Satana, “Kodi unalingalirapo za mtumiki wanga Yobu? Palibe wina pa dziko lapansi wofanana naye; ndi munthu wosalakwa ndi wolungama mtima, munthu amene amaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa.”
9 Et le diable répondit et dit devant le Seigneur: Est-ce gratis que Job honore le Seigneur?
Satana anayankha kuti, “Kodi Yobu amaopa Mulungu popanda chifukwa?”
10 N'avez-vous point fortifié sa maison, au-dedans comme au dehors, et, alentour tout ce qui lui appartient? n'avez-vous béni ses œuvres et multiplié ses troupeaux sur la terre?
“Kodi Inu simumamuteteza iyeyo, nyumba yake ndi zonse zimene ali nazo? Mwadalitsa ntchito ya manja ake, kotero kuti nkhosa ndi ngʼombe zake zili ponseponse mʼdzikomo.
11 Mais étendez votre main et qu'elle touche à ce qu'il possède, sinon il vous bénira en face.
Koma tatambasulani dzanja lanu ndi kukantha zonse ali nazo ndipo iyeyo adzakutukwanani ndithu pamaso panu.”
12 Alors le Seigneur dit au diable: Tu vois tout ce qui est à lui, je te le livre, mais ne touche pas à sa personne. Et le diable sortit de devant le Seigneur.
Yehova anati kwa Satana, “Chabwino, tsono zonse zimene ali nazo ndaziyika mʼmanja mwako, koma iye yekhayo usamukhudze.” Pamenepo Satana anachoka pamaso pa Yehova.
13 Or, peu de temps après ce jour-là, les fils de Job et ses filles buvaient du vin en la maison de l'aîné de leurs frères.
Tsiku lina pamene ana aamuna ndi ana aakazi a Yobu ankachita phwando ndi kumwa vinyo mʼnyumba mwa mkulu wawo,
14 Et un messager entra chez Job et il lui dit: Tes attelages de bœufs étaient au labour et les ânesses paissaient tout auprès.
wamthenga anabwera kwa Yobu ndipo anati, “Ngʼombe zanu zotipula ndipo abulu anu amadya chapafupi pomwepo,
15 Et des hommes en armes sont venus et ils les ont enlevés, et ils ont tué tes serviteurs à coups de glaive; j'ai seul échappé et j'accours t'en apporter la nouvelle.
tsono panabwera Aseba kudzatithira nkhondo ndi kutenga zonse. Apha antchito ndi lupanga, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
16 Comme celui-ci parlait encore survint un autre messager, et il dit à Job: Le feu du ciel est tombé et il a brûlé tes brebis, et il a dévoré pareillement les bergers; j'ai seul échappé et j'accours t'en apporter la nouvelle.
Iyeyo akuyankhulabe, wamthenga wina anabwera nati, “Kunagwa mphenzi ndipo yapsereza nkhosa ndi antchito anu onse, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
17 Comme celui-ci parlait encore survint un autre messager, et il dit à Job: Des cavaliers nous ont attaqués sur trois points, et ils ont enveloppé tes chamelles, et ils les ont enlevées; et ils ont tué tes serviteurs à coups de glaive; j'ai seul échappé et j'accours t'en apporter la nouvelle.
Iyeyo akuyankhulabe, wamthenga wina anabwera nati, “Akasidi anadzigawa mʼmagulu atatu ankhondo ndipo anafika pa ngamira zanu ndi kuzitenga. Apha antchito anu onse ndi lupanga, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
18 Comme celui-ci parlait encore survint un autre messager, et il dit à Job: Tandis que tes fils et tes filles étaient à manger et à boire chez leur frère aîné,
Iyeyo akuyankhulabe, panafikanso wamthenga wina nati, “Ana anu aamuna ndi aakazi amachita phwando ndi kumwa vinyo mʼnyumba ya mkulu wawo,
19 Soudain un grand vent est venu du désert et il a saisi les quatre coins de la maison; et elle s'est écroulée sur tes enfants; et ils sont morts; j'ai seul échappé et j'accours t'en apporter la nouvelle.
mwadzidzidzi chinayamba chimphepo champhamvu chochokera ku chipululu, nʼkudzawomba nyumba mbali zonse zinayi. Nyumbayo yawagwera ndipo afa, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
20 Or, Job s'étant levé déchira ses vêtements, et il se coupa toute la chevelure, et, s'est prosternant la face contre terre, il adora, et il dit:
Atamva zimenezi, Yobu anayimirira nangʼamba mkanjo wake, ndi kumeta tsitsi lake. Kenaka anadzigwetsa pansi napembedza Mulungu,
21 Nu je suis sorti des entrailles de ma mère, nu je partirai d'ici; le Seigneur n'avait donné, le Seigneur m'a ôté, il est advenu comme il a plu au Seigneur; béni soit le nom du Seigneur.
nati, “Ndinatuluka maliseche mʼmimba mwa amayi anga, namonso mʼmanda ndidzalowa wamaliseche. Yehova ndiye anapereka ndipo Yehova watenga; litamandike dzina la Yehova.”
22 Malgré tout ce qui lui est arrivé, Job ne pécha point contre le Seigneur; et il n'accusa point Dieu d'avoir manqué de sagesse.
Mu zonsezi, Yobu sanachimwe kapena kunena kuti, “Mulungu walakwa.”

< Job 1 >